Mutu 14

1 Landilani aliyense wofoka muchikhulupililo, osaweluza na mkangano. 2 Munthu umozi alinachikhulupililo kudya chilichonse, wina wamene niwofoka akudya chabe zamasamba. 3 Wamene akudya vilivonse asapepule wamene sakudya, ndipo wamene sakudya vonse asaweluze wamene akudya vonse. Pakuti Mulungu amulandila. 4 Ndiwe ndani wamene uweluza kapolo wa munthu winangu? Anyamuka nakugwa pali mbuye wake. Koma azampanga kuimilila, pakuti ambuye akwanisa kupanga kuti aimilile. 5 Munthu umozi aona kuti siku imozi ipambana inanso.Wina aona masiku onse chimozi mozi. Lekani aliyense akhale nacho chisimikizo mumtima mwake. 6 Wamene aona siku ayiyanganila kwa ambuye ndipo iye wakudya adyele mwa ambuye. Chifukwa apeleka mayamiko kwa Mulungu. Iye wamene sakudya,azichosako kudyela kwa Ambuye, naiyenso ayamika Mulungu. 7 Pakuti palibe wamene azinkhalila yeka, kulibe wamene azifela. 8 Pakuti ngati tinkhala, tinkhalila ambuye, ngati tikufa, tifela mwa ambuye.Tafa, sitinafe ndise ba ambuye. 9 Chifukwa kamba ka ichi Yesu anafa nakuuka futi, kuti akankhale mbuye pa moyo na bamene bali na moyo. 10 Koma imwe, nichani muweluza mbale wanu? Ndipo imwe nichani mupepula mbale wanu?Pakuti tonse tizaimilila pampando wa chiweluzo cha Mulungu. 11 Pakuti nicholembedwa, Malinga nili ndi moyo atelo Ambuye, kwa ine bondo lililonse lizagwada,ndipo lilime iliyonse izapasa mayamiko kwa Mulungu. 12 Kotelo ndipo aliyense apeleka ndondomeko ya umoyo wake kwa Mulungu. 13 Kotelo, tisaweluzane wina ndi mnzake, koma muganize ichi, kulibe wamene azikila chipysinjo kapena msampha ku mbale wake. 14 15 Niziba ndipo nilinacho chisimikizo mwa Yesu Christu, kulibe chinthu chodesedwa pacheka, wamene aona chinthu kuti nichodesedwa, kwa iye nichodesedwa. Ngati kamba ka mwazi mbale wako akhumudwa, ninshi simuyenda muchikondi. Musaononge chakudya chamunthu wamene Yesu anafela. 16 Musalole chinthu chabwino kuti wina akambe kuti nichoipa. 17 Pakuti ufumu wa Mulungu sikudya na kumwa, koma chiyelo, mtendere na chimwemwe, mumuzimu oyela. 18 Pakuti wamene atumikila Christ munjila iyi, avomelezedwa na mulungu komanso banthu bamuvomeleza. 19 Kotelo, tiyeni tifunefune zinthu zobwelesa mtendere na vinthu vamene vizatimangilila pamozi wina ndi mnzake. 20 Osaononga ntchito ya Mulungu ka ka chakudya, vonse vinthu nivoyela, koma nichoipa kwa uja wamene akudya nakukhumudwisa winangu. 21 Nichabwino osadya nyama, kapena kumwa vinyu, kapena chilichonse chamene mbale akhumudwa nacho. 22 Chikhulupililo mulinacho chisungeni pakati paimwe na Mulungu, odalisika niwuja wamene sazisusa na zamene avomeleza. 23 Wamene sakhulupilila aweluzidwa ngati akudya, chifukwa simwachikhulupililo. Ndipo chamene sichichokela ku chikhulupililo nichimo.