1 Manje ise tili olimba timnvelele anzathu ofoka, ndipo tisazisangalase. 2 Lekani aliyense amnvese bwino mnzake, pali icho chabwino, kuti amulimbikise. 3 Pakuti Yesu sanazimnvese bwino eve eka, koma mwamene chinalembewa, manyozo ya baja banamunyozani yanagwela pali ine. 4 Pakuti chamene chinalembewa kudala, chinalembewa kuti ise tilondole, kuti kupitila mukuleza mtima, na chilimbikiso cha malemba, tikankhale nacho chisimikizo. 5 Manje Mulungu oleza mtima na chilimbikiso alengese kuti munkhale na nzelu zimozi, kuli wina ndi mnzake kulingana na Yesu Christu. 6 Lekani achite ichi kuti na nzelu zimozi kuti muyamike na kamwa kamozi, Mulungu na tate wa mbuye wathu Yesu Christu. 7 Motelo landilani wina ndi mnzake, monga mwamene Yesu anamulandilani, kuchiyamiko cha Mulungu. 8 Pakuti nikamba kuti Christu anapangiwa kapolo, wa mdulidwe, kamba ka choonadi cha Mulungu. Kuti akasimikizile malonjezano yanapasiwa kuli azitate, 9 ndipo kwa akunja, kuulemelelo wa Mulungu muchifundo chake. Chilimonga chinalembedwa, motelo nizapeleka mayamiko kwa imwe pakati pa akunja nakuimbila mayamiko ku zina lanu. 10 Nafuti ikamba kuti,sangalalani imwe akunja nabanthu bake, 11 nafuti yamikani Mulungu, monse imwe akunja, lekani banthu onse bayamike mulungu. 12 Nafuti Esaya akamba kuti,kuzankhala mkoka wa Jessie, ndipo ndiye azaima nakulamulila pa akunja. Akunja azankhalanacho chisimikizo. 13 Lomba lekani Mulungu wahisimikizo akuzleni na chimwemwe chonse na mtendere pakuti mukhulupilila, kuti mukachuluke muchisimikizo, mwa mphamnvu ya Muzimu oyera. 14 Naine nilinacho chisimikizilo pali imwe abale, nilina chisimikizo kuti imwe namwe ndimwe ozula na ubwino, wozula na nzelu, nilinachisimikizo kuti mukwanisa kulimbikisana wina ndi mnzake. 15 Koma nilemba izi molimba mtima, kumukumbusani kamba ka mphaso inapasiwa kuli ine na Mulungu. 16 Iyi mphaso inali yakuti ine ninkhale kapolo wa Yesu Christu ku akunja, kuzipeleka monga wansembe ku uthenga wa Mulungu. Nifanuka kuchita ichi kuti chopeleka kwa akunja chikalandilidwe, kusambisiwa na Muzimu oyera. 17 Motelo kusangalala kwanga kuli mwa Yesu Christu na muvinthu va Mulungu. 18 Pakuti sinizakamba chilichonse koma Yesu Christu anakwanilisa kupitila muli ine ku kumnvela kwa akunja. Ivi ndiye vinthu vochitika na mau na machitidwe, 19 mwamphamnvu ya chiwoneselo, na zoziziswa, na mphamnvu ya Muzimu oyera. Ichi chinankhala telo kuti kuyambila ku yerusalemu,na madela yapafupi, kufika ku illyricum, kuti nikanyamule wonse uthenga wa Yesu Christu. 20 Munjila iyi, kufuna kwanga kwankhla kulalikila uthenga, koma osati kwamene Yesu azibika naine, kuti nisamange pa maziko ya munthu wina. 21 Chilimonga chinalembedwa, kulibaja bamene mau yake siyanabwele, bazamuona, ndipo bamene sibanamnvele bazaziba. 22 Nainenso zinalipo zolesa kuti nibwele kwa imwe, 23 koma pali pano nilibe nthawi yonkhala futi mumadela yakuno, ndipo kwazaka zambili, nankhala nifunisisa kubwela kuli imwe. 24 Pamene nizapita ku Spain, nifuna kumuonani popitilapo, nakuti mukanitume imwe munjila yanga, pamene nizankhala na imwe panthawi itali. 25 Koma apa niyenda ku Yerusalemu, kumikila okhulupilila. 26 Pakuti chinali ubwino wa Macedonia na Achia kupeleka ku osauka, pakati pa okhulupilila ali ku Yerusalemu. 27 Inde chinali ku ubwino wao, nibankhongole bao, pakuti ngati akunja agabana muzauzimu zao, naiwonso afunika kuti abatumikile muzakuthupi. 28 Motelo ngati nasiliza ntchito iyi, nakusimikiza kuti balandila vamene vinatengewa, nizayenda ku Spain nakumutandalilani munjila. 29 Niziba kuti nikabwela kuli imwe nizabwela namadaliso mwa yesu ochuluka. 30 Manje nimulimbikisani abale,mwa mbuye Yesu Christu, na chikondi cha muzimu, kuti muvutike naine mumapemphelo kwa Mulungu pali ine. 31 Pemphelelani kuti nikapulumusiwe kulibaja osamnvela, mu ayaudeya nakuti utumiki wanga ukalandilidwe mu Yerusalemu ku okhulupilila, 32 Pemphelani kuti nikabwele kuli imwe muchimwemwe, kupitila muchifunilo cha Mulungu, nakuti pamozi naimwe nikapeze mupumulo. 33 Mulungu wa mtendere ankhale naimwe monse. Amen.