Mutu 140

Kuli woyimba mukulu. Salimo ya Davide. 1 Yehova, nipulumuseni kuli boipa; nipulumuseni ku bantu bankanza. 2 Bakonza voipa mumitima mwao; bamayambisa nkondo siku iliyonse. 3 Malilimi yao yalasa monga njoka; Ululu wa njoka uli pa milomo zao. Selah 4 Nisungeni mumanja mwa boipa, Yehova; nipulumuseni ku bantu bankanza bamene bafuna kunigwesa. 5 Bozikuza baniteyela musampa; bayanzika sumbu; baniteyela musampa. Selah 6 Ninakamba kuli Yehova, Imwe ndimwe Mulungu wanga; mvelani kulila kwanga; 7 Yehova, Ambuye wanga, ndimwe ba mpamvu bokwanisa kunipulumusa; Munichingiliza mutu wanga siku yankondo. 8 Yehova, musapase boipa vilako lako va mitima yao; musavomeleze misampa yao kufilikizika. Selah 9 Bamene banizungulila banyamula mitu yao; voipa va milomo yao vibavininkila. 10 Malasha yoyaka mulilo ubagwele; baponyeni mumulilo, mu nganjo ya moto, kuti basakaukepo futi. 11 Bantu bamalulimi basatetezewe pa ziko ya pansi; choipa chibakonke kufika kuli muntu wankanza kuti amupaye. 12 Niziba kuti Yehova azaweluza muchilungamo bovutika, nikamba kuti azaweluza bosauka. 13 Zoona bolungama bazayamikila zina yanu; bolungama bazankala pamenso panu.