Mutu 141

Salimo ya Davide. 1 Yehova, nililila kuli imwe; bwelali kuli ine musanga. Munimvele ine pokuitanani. 2 Pempelo yanga inkale monga vofukiza pamenso panu; manja yanga mumwamba monga nsembe ya kumazulo. 3 Yehova, ikani kamalonda pakamwa panga; sungani komo ya mulomo wanga. 4 Mutima wanga usakumbwe choipa chilichonse kapena kuchita nabo pamozi voipa bantu bochita voipa. Nisadyeko vambwino vao vilivonse. 5 Muntu wolungama animenya; chizankala chabwino kuli ine; Musiyeni anibweze ine; yazankala ngati mafuta pamutu panga; mutu wanga usakane kuyalandila koma pempelo yanga ntau zonse imashushana na voipa vao. 6 Basogoleli bao bazagwesewa kuchokela pamwamba pa vimyala vikulu ; bazamvela kuti mau yanga ni yokondwelesa. 7 beve bazakamba ati, “Monga mwamene muntu amalimila na kupwanya ntaka, ndiye mwamene mabonzo yatu yamwazyikilana pamulomo pa sheol. 8 Zoona, menso yanga yali pali Imwe, Yehova, Yehova; muli Imwe ndiye mwamene nitabila; musasiye umoyo wanga ninshi ulibe chonichingiliza. 9 Munichingilize ku misampa yamene bani ikila, Ku misampa ya bochita voipa. 10 lekani boyipa bagwele mumasumbu yao, ine nipulumuke.