1 Sailmo ya Davide. Nizakuyamikani ni mtima wanga onse; pameso pa tumilungu nizakuyimbilani mothokoza. 2 Nizagwada nakuyangana Kachisi yanu yoyela, na kuyamika zina yanu chifukwa chapangano ya kukhulupilika na chilungamo chanu. Mwapanga mau yanu na zina yanu kukhala yofunika manigi kuchila chilichonse. 3 Siku yamene ninakuitanani, munaniyankha; munanipanga olimba ndipo munakosesa moyo wanga. 4 Mafumu yonse ya ziko yapansi yazakuyamikani, Yehova, pakuti yazamvela mau ochka pakamwa panu. 5 Inde, bazaimba va ntchito ya Yehova, pakuti ulemelelo wa Yehova ni ukulu. 6 Pakuti ngakhale Yehova ali okwezekewa, asamalila bapansi; Koma ozimvesa amazibila pali kutali. 7 Olo niyenda pakati pa voyofya, muzasunga moyo wanga; muzatambulula kwanja yanu mukali kuli badani banga, ndipo kwanja yanu yamanja izanipulumusa. 8 Yehova ali naine kufikila posilizila; chipangano chakukhulupilika kwanu, Yehova, kukhala muyayaya. Musaibale baja bamene manja yanu yanapanga.