Mutu 135

1 Tamandani Yehova! Lemekezani zina Ya Yehova. Mutamandeni eve, imwe atumiki ya Yehova, 2 imwe bamene mumaimilila munyumba ya Yehova, mumabwalo ya nyumba ya Mulungu wathu. 3 Lemekezani Yehova, pakuti ndiye wabwino; imbani zotamanda zina yake, pakuti nichokondwelesa. 4 Pakuti Yehova asankha Yakobo kuti ankhale wake, Israeli ankhale chuma chake. 5 Niziba kuti Yehova ni wamukulu, kuti Ambuye wathu ni woposa milungu zonse. 6 Chilichonse chamene Yehova afuna amachichita kumwamba, paziko yapansi, munyanja na munyanja zonse zakuya. 7 Iye amabwelesa mitambo kuchokela kutali, kuchitisa mphezi kutsata mvula, na kutulusa mpempo munkhokwe yake. 8 Anapaya mwana oyamba kubadwa wa Aigupto, banthu na nyama. 9 Anatumiza zizindikilo na zodabwisa pakati pako, Aigupto, pa Farao na atumiki bake onse. 10 Anamenya mitundu yambili naku paya mafumu amphamvu, 11 Sihoni mfumu ya Aamori, na Ogi mfumu ya Bashani nama ufumu onse ya Kanani. 12 Anatipasa ziko yawo ngati cholowa, cholowa cha Aisiraeli banthu bake. 13 Zina yanu, Yehova, izankhalapo muyayaya; mbili yanu, Yehova, izankhalapo ku mibadwomibadwo. 14 Pakuti Yehova amateteza banthu bake ndipo amachitila chifundo atumiki bake. 15 Mafano ya mitundu ni siliva na golide, nchito ya manja ya banthu. 16 Mafano yali na makamwa, koma siyamakamba; manso yali nawo, koma siyamayangana ; 17 matu yali nawo, koma siyamamvela, ndipo mukamwa mwao mulibe mpweya. 18 Bamene bapanga izi ali monga vamene ivi. monga onse wamene akhulupilila muli ivi. 19 Iwe bana ba Israyeli, lemekezani Yehova; mibadwo ya Aroni, lemekezani Yehova. 20 Iwe a mbumba za Levi, lemekezani Yehova; imwe bamene amalemekeza Yehova, lemekezani Yehova. 21 Wolemekezeka Yehova mu Ziyoni, iwe wonkhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.