1 Nililila mukati kuli imwe, Yehova. 2 Ambuye, velani mau yanga; matu yanu yavesese kulila kwanga kwa chifundo . 3 Ngati imwe , Yehova, musunga machimo, Yehova, nidani anga imilile? 4 Koma kuli kukululukiwa kuli imwe, kuti tiyope imwe. 5 Niyembekeza Yehova, moyo wanga ulindila, ndipo namu mau yake nichiyembekezo changa. 6 Moyo wanga ulindila Yehova kuchila malonda oidilila kuti kuche . 7 Israyeli,chiyembekezo chili muli Yehova. Yehova ni wachifundo na chikukululukilo. 8 Ndiye azawombole Isiraeli ku machimo yake yonse.