Salimo yachiyamiko. 1 Pundani mokondwela kuli Yehova, ziko yonse yapansi. 2 Tumikilani Yehova mokondwela; bwelani pamenso pake na kuyimba mokondwela. 3 Zibani kuti Yehova ndiye Mulungu; anatipanga ise, ndipo ise ndise bake. Ndise bantu bake na nkosa za pabusa pake. 4 Ngenani muzipata zake na chiyamiko na mu mukoti namatamando. Muyamikeni naku dalisa zina yake. 5 Chifukwa Yehova niwa bwino; chipangano chake chokulupilika nicha muyayaya ndipo chikulupililo chake mumibadwo yonse.