Mutu 99

1 Yehova alamulila; lekani mitundu injenjeme. Ankala pamwamba pa makerubi; ziko igwedezeka. 2 Yehova ni mukulu mu Ziyoni; ndiye niokwezekewa pamwamba pa mitundu yonse. 3 Balemekeze zina yanu ikulu na yabwino; eve ni oyela. 4 Mfumu niwa yampamvu, ndipo amakonda chilungamo. Mwakazikisa chilungamo; mwachita chilungamo na chiweluzo muli Yakobo. 5 Tamandani Yehova Mulungu watu ndipo lambilani pa chopondapo mapazi yake. eve ni oyela. 6 Mose na Aroni pamozi na bansembe bake, ndipo Samueli anali pamozi na bantu banaitana zina yake. Beve banaitana kuli Yehova, ndipo anabayanka. 7 Anakamba nabeve kuchokela mumakumbi yoima monga chipilala. Banasunga malamulo yake na malemba yamene anabapasa. 8 Munabayanka, Yehova Mulungu watu. Mulungu okululuka unali kuli beve, koma wamene anabalanga volakwa vabo. 9 Tamandani Yehova mulungu watu, ndipo lambilani pa phili yake yopatulika, pakuti Yehova Mulungu watu ni oyela.