1 Pamenepo analilila mukunvela kwanga na mau yonveka, nati, Lekani wolanganila akwele kumuzinda, aliyense na chisulo chake chakupaila mumanja yake. 2 Manje onani! Bamuna bali sikisi banatuluka munjila ya pachipata yakutali yolangana kumpoto, aliyense ali na chisulo chake chopaila mumanja mwake. Pakati pawo panali munthu wovala bafuta, ndipo mumbali mwake munali zisulo za mulembi. Choncho banangena mukati na kuimilila kumbali kwa guwa lansembe lamukuwa. 3 Ndipo ulemelelo wa Mulungu wa Isiraeli unakwela kuchokela pa akerubi nakufika pakomo pa nyumba. Iye anaitana munthu wovala bafutayo yamene yanali na zisulo za mulembi mumbali mwake. 4 Yehova anamuuza kuti: “Pita pakati pa muzinda, pakati pa Yerusalemu, ulembe chizibiso pamphumi pa banthu bamene balila na kuusa moyo chifukwa cha vonyansa vonse vamene vichitika pakati pa muzinda. 5 Ndiponso anakamba na benangu mumakutu mwanga, Pita mumuzi pambuyo pake na kupaya. Usalengese menso yako kunkala na chifundo, ndipo usalekelele aliyense. 6 Paya-bonongelatu-mukulu bonse, munyamata, namwali, bana bang’ono kapena bakazi. Koma usakonke aliyense wamene ali na chizibiso pamutu pake. Muyambile pa malo yanga yopatulika!", Mwaichi banayambila na bakuli bamene banali pasogolo pa nyumba. 7 Anabauza kuti, "Ipisani nyumba, na kuzulisa panja pake na banthu bakufa. Ndipo banayenda na kuononga muzinda. 8 Pamene banali kuononga muzinda, ninazipeza neka na kugwesa nkope yanga pansi na kulila na kuti, : “Ha, Ambuye Yehova, nanga muzabononga bosala bonse ba Isiraeli pakubasanulila ukali wanu pa Yerusalemu? 9 Anakamba kuli ine, Uchimo wa nyumba ya Israyeli na Yuda niyaikul kwambili. Ziko yazula na magazi na muzinda wazula na zopotoka, chifukwa bakamba kuti, Yehova aibala ziko, Yehova saona; 10 Koma kuli ine, linso yanga siizayangana na chifundo, ndipo sinizabalekelela. Mumalo mwake nibwelesa zonse pamutu pawo. 11 Onani! Munthu wovala bafuta wamene anali na zida za mulembi mumbali mwake anabwelela. Anaulusa na kuti, Nachita vonse vamene munanilamulila."