Mutu 13

1 Nafuti, mau ya Yehova yana bwela kuli ine, kuti, 2 "Mwana wa muntu, nenela za baneneli bamene banenela mu Israeli na ku kamba kuli baja bamene banenela ku chokela mu maganizo yabo, 'Nvela mau ya Yehova; 3 Mulungu Yehova akamba ichi: Soka kuli ba neneli bopusa, bamene bakonka mzimu yabo beka, koma kulibe chamene banaona! 4 Israeli, baneneli bako bankala monga mimbulu muchipululu 5 Simunayende kumalo yopwanyika yozunguluka nyumba ya Israeli kuti muikonze, kuti musiye kumenyana nabo pa siku ya Yehova. 6 Bantu bana menso mpenya yonama ndipo muma nenela vaboza, bamene bakamba, “ivi naivi ndiye vamene anakamba Yehova. Yehova sanabatume, koma apangisa bantu kuyembekezela kuti utenga wabo uzakwanilisiwa. 7 simunankale na menso penya yaboza na ku punzilila va boza, imwe bamene mukamba, Ivi naive ndiyeve anakamba Yehova" pamene ine neka sini nakambe?' 8 Pamene apo Mulungu Yehova akamba kuti, 'Popeza munaona mensompenya yonama na ku kamba vonama, chifukwa chake ni ivi vo kamba va Mulungu Yehova pali imwe: 9 kwanja yanga izankala pa ba neneli boona mensompenya yonama nabaja bamene banenela vaboza. Sibazankala pa gulu ya bantu banga, kapena kulembewa mu mabuku ya nyumba ya Israeli; basayende ku malo ya Israeli. Kuli iwe uzaziba kuti ine ndine Mulungu Yehova! 10 Chifukwa cha ichi, na chifukwa chakuti basobesa bantu banga, nati: “Mtendere! pamene palibe mtendere, akumanga mpanda wopaka laimu. 11 Nena kwa iwo opaka linga, izagwa; kuzankala mvula yampamvu, ndipo nizatumiza matalala kuti igwese, na mpepo yamkunto kuti igwese pansi. 12 Onani, chipupa chiizagwa. Sibanaku uzeni benangu, "ilikuti laimu yamene munafakako?" 13 Chifukwa cha ichi Ambuye Yehova bakamba kuti, Niza leta chimpepo chikulu, ndipo pazankala msinje ya mvula mu ukali wanga; Matalala mu ukali wanga yazauwononga kotheratu. 14 Pakuti nizagwesa linga yamene muna vininkila na laimu, ndipo nizaigweselatu pansi, ndipo pwaniyilatu paka pansi poyambila. Chotelo izagwa, ndipo naimwe muzawonongewa pakati pa ivo zonse. Pamenepo uzaziba kuti ine ndine Yehova. 15 Pakuti nizawononga chipupa na baja bamene banalipaka laimu na ku kwiya kwanga. Niza kamba kuli iwe: “chipupa sichilipo, ngakale bantu bamene banalipaka laimu, 16 baneneli ba Israeli bamene bananenela va Yerusalemu, bamene banaona mensompenya ya mtendele chifukwa pali eve, koma palibe mtendele!- uku niku nenela kwa Mulungu Yehova."' 17 Iwe, mwana wa muntu, yangana nfeshi yako pa bana bakazi bantu ba mtundu bako, bamene banenela mumaganizo mwabo, naku kubanenela zoipa. 18 Kamba, ‘Mulungu Yehova akamba: ‘Soka kuli bakazi bamene bamasoka masenga mumanja mwabo, bamene bamavala nyla zochingila pamitu pabo za ukulu ulionse, zamene amasaka bantu. Muzasaka bantu banga koma kupulumusa moyo wanu? 19 Munani tukana pakati pa bantu banga chifukwa cha balele wozaza manja na zinyenyeswa za mukate, kuti mupaye bantu bamene simufunika kupaya, na kusunga muyo ya bamene sibafunikila kupitiliza na umoyo, chifukwa cha maboza yanu ku bantu banga bamene banu kunvelani. 20 Mwaicho Mulungu Yehova, akamba ichi: ‘sini funa zama mankwala zamasenga zamene mwasebenzesa ku gwila miyoyo ya bantu monga nyoni. Inde nizabamgamba kuchoka mumanja yanu; na bantu bamene mwagwila monga nyoni nizabalekelela bayende momasuka. 21 Nizangamba zopimba zanu na kupulumusa bantu banga mumanja mwanu, kuti basankale boteyewa mumanja mwanu. Uzaziba kuti ndine Yehova. 22 Chifukwa munafokesa mutima ya muntu olungama na maboza, nangu sina mukalipise, chifukwa mumalimbikisa zochita za munthu woipa kuti asasiye njila yake kuti apulumuse moyo wake. 23 Mwaicho simuzaonapo mansompenya yonama, kapena kupunzila ufwiti, pakuti nizapulumusa bantu banga mumanja mwanu. Uzaziwa kuti ine ndine Yehova.