1 Ndiponso mau a Yehova yanabwela kwa ine, kuti, 2 Mwana wa munthu, zibisa Yerusalemu pa zonyansa zake, 3 nakukamba kuti, 'Ambuye Yehova akamba kuli Yerusalemu: Kuyamba kwako na kubadwa kwako kunachitikila mu malo ya Kanani; batate aako banali baku Maamori, na bamai banali baku Muhiti. 4 Pa siku ya kubadwa kwako, bamai bako sibanakucheke mukombo, kapena kukuyelesa na manzi, kapena kukuzoleka na muchele, kapena kukuvininkila nsalu. 5 Palibe linso linakuchitila iwe chifundo kukuchitila olo chimozi cha ivi vinthu, kuti akuchitile iwe chifundo. Pa siku yamene unabadwa, na kunyansidwa na moyo wako, unatayidwa panja pa munda. 6 Koma ninapita pafupi naiwe, ndipo ninakuona ukunyuka mumagazi yako; ndipo ninakamba kuli iwe mu magazi yako, Nkala na umoyo!" Ninakamba kuli iwe mumagazi yako, "Nkala na Umoyo!" 7 Ninakupanga iwe kukula monga zomela mumunda. Unabalana nakunkala wamukulu, ndipo unankhala ngale ya ngale. Maziba yako yanankala yolimba, na sisi yako inakula, ngakhale kuti unali wamaliseche ndipo kulbe zovala kumendo. 8 Ninapita kuli iwe nafuti, ndipo ninakuona. Ona! ntawi yachikondi inabwela kuli iwe, ninatambasula mukango pali iwe na kuvininkila chintako chako. Pamene apo ninalumbili kuli iwe nakukubwelesa mu chipangano-uku ndiko kukamba kwa AAmbuye Yehova-ndipo unankala wanga. 9 Ninakusambika na manzi na kupukuta magazi kuchoka pali iwe, nakukuzoza na mafuta. 10 ndinakuvalika zopikiwa zovala, na nsapato zachikopa kumendo kwako; Ninakuvininkila na nsalu yabwino, nakukuvininkila na siluku. 11 Mopitiliza ninakuvalika juweli, nakuikapo vibangili kumanja kwako, na cheni mumukhosi mwako. 12 Ninakuika ndolo mumpuno mwako, na ndolo mumakutu yako, na korona wabwino pamutu pako. 13 Mwaichi unaoneka bwino na golidi na siliva, ndi kuvala bafuta, na silika, na zovala zopikiwa; unadya unga wabwino, uchi, na mafuta, ndipo unali kuoneka bwino kwambili, ndipo unankhala mfumukazi. 14 Mbili yako inanveka kwa bamitundu chifukwa cha kuoneka bwino kwako, chifukwa unali wangwilo mu ukulu wamene ninakupasa- mwamene akambila Ambuye Yehova. 15 Koma unadalila mu kuoneka bwino kwako, na kuchita vinthu monga hule chifukwa cha mbili yako; unatila zochita zako za uhule pali aliyense wamene anapita kwako, kuti kuoneka bwino kwako kunkale kwake. 16 Ndipo unatenga zovala zako na kuzipangila nazo malo yokwezeka yooneka bwino, ndipo kwamene kuja unachita vinthu monga hule. Ichi sembe sichinachitike. Kapena chinthu monga ichi kunkalapo. 17 Unatenga majuweli yooneka bwino ya golide na siliva yamene ninakupasa, na kuzipangila vooneka monga bamuna, na kuchita navo monga hule angachite. 18 Unatenga vovala vako vopikiwapikiwa na kuzivininkila, na kuika mafuta yanga monga zonunkila pamenso yawo. 19 Buledi yanga ninakupasa yopangiwa na fulao yabwino, na mafuta, na uchi, kuti unkhale na fungo yonunkhila bwino, ichi ndiye chamene akamba Ambuye Yehova. 20 Koma unatenga bana bako bamuna na bakazi, bamene unanibalia ine, nakubapeleka nsembe kwa zifanizilo kuti badyewe monga vakudya. Ushe vochita vako va uhule ninkani ing'ono? 21 Unapaya bana banga kulu mafano na kubaocha mumulilo. 22 Muzonyansa zako zonse na zochita zako zachigololo siunaganizile za masiku ya ufana wako, pamene unali wopanda zovala na pamene unalibe chilichonse pamene unali kuvunvulika mumagazi yako. 23 Soka! Soka kwa iwe! Uku ndiye kukamba kwa Ambuye Yehova, mwaichi, mukuwonjezela pa vonse ivi voipa, 24 unazipangila chitunda na kuzipangia malo yapamwamba pamalo yonse yozibika. 25 Unamanga malo yako yapamwamba pa mutu wa njila iliyonse nakupanga kuoneka bwino kwako uchiwelewele, nakutambasula mendo yako kuli aliyense wamene apita, nakuchulukisa machitidwe yako ya uhule. 26 Wachita zachigololo monga hule nama Aigupto, bapafupi pako wonyansa, na iwe munachita vambili vichitidwe va uhule, kunikwiisa kuukali wanga. 27 Ona! Nizakumenya na kwanja kwanga nakujuba kuvakudya vako. Nizapeleka umoyo wako kuli badani bako, bana bakazi baku Afilisti, bamene banachita manyazi na zonyansa zako. 28 Wachita machitidwe ya uhule pamozi na Asuri chifukwa siunakhutile. Unachita monga hule ndipo siunakhutile futi. 29 Unachitanso zachiwelewele zambili muziko ya bogulisa baku Kasidi, na pali ichi siunakutile. 30 Nanga mutima wako niwofoka bwanji—Uku ndiye kukamba kwa Ambuye Yehova—kuti uzachita vonse ivi vinthu, nchito za uhule zilibe manyazi? 31 Wamanga zitunda zako pa mwamba pa museu ulibonse na kuzimangila malo yapatali mumalo yonveka yaliyonse. Koma siunankhale monga hule chifukwa unanyoza kulandila malipilo. 32 Iwe mukazi wachigololo, umalandila balendo mumalo mwa mwamuna wako. 33 Banthu bamapeleka malipilo kwa hule iliyonse, koma iwe umapeleka malipilo yako kwa mabwenzi yako yonse, nakubapasa chiphuphu kuti babwele kwa iwe kuchokela kulikonse chifukwa cha uhule wako. 34 Chifukwa cake pali kusiyana pakati pa iwe na bakazi benangu. Palibe wamene amakulipila kuti unkhale hule. Ndiwe bosiyana kwambili. Munawapasa malipilo ndipo siunapasidwe chilichonse. 35 Mwaichi, iwe hule, mvela mau ya Yehova. 36 Ambuye Yehova akamba kuti, Chifukwa watila panja kukumbwila kwako, kubonesa chintako chako mu zinchito zako zacigololo na okondewa bako na yonse mafano yako yonse yonyansa, na chifukwa unabapasa mwazi wa bana bako, 37 Ona, nizasonkhanisa bonse bokondewa bako bamene unakumana nawo,bonse bamene unakondapo na bonse bamene unazondapo, ndipo nizabasonkanisa mosusana naiwe kumbali iliyonse. Nizalangiza chintako chako kuli beve kuti bakuone. 38 Pakuti nizakulanga chifukwa cha uhule na kukesa magazi, na kukubwelesa pakukesa magazi muukali wanga na nsanje zanga. 39 Nizakupeleka iwe mumanja mwawo kuti bagwese chipinda chako chapamwamba, na kugwesa misanje yako, nakukuvula zovala zako, nakupoka zokuonesa bwino zonse. Bazakusiya chintako ndipo alibe kanthu. 40 Ndipo bazabwelesa gulu yabanthu mosusana naiwe na kukutema miyala na miyala, na kukujuba muviduswa na malupanga yawo. 41 Bazashoka nyumba zako, nakukulangiza pamenso yabakazi bambili; pakuti nizalesa uhule wako, ndipo siuzabwezapo maubwenzi yako. 42 Pamenepo nizakazikika mutima wanga pansi pa iwe na ukali wanga; mukwiyo wanga uzachoka kuli iwe, pakuti nizakhuta, ndipo sinizankala bokalipa nafuti. 43 Chifukwa siunakumbukie masiku ya ufana wako, na kunipanga ine kugwedeza ukali wanga chifukwa cha ivi vonse vinthu, mwaichi, Ona! Ine wamene nizakubwelesa pansi pa puthu wako chilango pazamene wachita-uku ndiye kukamba kwa Ambuye Yehova. Kodi siunabonjezele vigololo pa zonyansa zako zonse? 44 Onani! Aliyense wamene akamba miyambo kupitila mwa imwe azakamba kuti, Monga mayi alili, mwamene umo ali mwana wake wamkazi.” 45 Iwe ndiwe mwana wamukazi wa mayi wako, wamene amanyansidwa na mwamuna wake na bana bake, ndipo ndiwe mlongo wa alongo ako amene amanyansidwa na bamuna bawo, bana bawo, bamai bako banali Muhiti, na batate bako banali Mwaamori. 46 Kalongosi mukulu wako anali waku Samariya na bana bake bakazi banali kukhala kumpoto, pamene mung’ono wako anali kukhala kumumwela kwa iwe, ndiko kuti, Sodomu na bana bake bakazi. 47 Simunayenda munjila zawo zeka, na kutenga mankalidwe yawo na machitidwe yawo, koma munjila zanu zonse munali woipa kuchila beve. 48 Monga nili naumoyo, Ambuye Yehova akamba, kalongosi wako Sodomu na mizi yake, sibanachite choipa chili chonse monga wachichita iwe na bana bako bakazi. 49 Onani! Yamene iyi inali chimo ya kalongosi wako Sodomu, kuti iye anali wozikuza mu umoyo wake wozitukumula, wosasamala ndiponso wosaganizila kalikonse. Sanalimbise manja ya banthu osauka na wosoba. 50 Anali bozikuza na kuchita zonyansa pamenso panga, ndipo nizabachosa monga waonela. 51 Samaliya sanachite ngankale yang'ono pamachimo yako; Wachita vambili vonyansa vinthu kuchila vamene banachita, ndipo walengesa bakalongosi bako kuoneka wolungama kuchila iwe chifukwa cha vonse vonyansa vinthu vamene wachita! 52 Ubale manyazi yako, chifukwa waonesa bwino bakalongosi wako. Chifukwa cha machimo yako, yamene unachita monyansa, walengesa ba kalongosi bako kuoneka woyela kuchila iwe. Mwaichi, nkala wamanyazi na na kubala manyazi yako, chifukwa waonesa bakalongosi bako kuoneka woyela. 53 Pakuti nizabweza undende wabo, ogwidwa baku Sodomu na bana bake bakazi, na bogwidwa ba Samariya na bana bake bakazi; ndipo bogwidwa bake bazankala pakati pawo. 54 Cifukwa cha izi muzachita manyazi; uzankhala na manyazi chifukwa cha zonse zamene unachita, ndipo muli iyi njila muzankala chitontozo kuli beve. 55 mwaichi kalongosi wako Sodomu na bana bake bakazi bazankalanso mwamene banalili poyamba, ndipo Samariya na minzi yake yabakazi bazankalanso mumalo yawo yakudala. Ndipo iwe na bana bako bakazi muzabwelela mwamene munalili kudala. 56 Sodomu kalongosi wako sanakambiwepo ngankale mukamwa kako mu masiku yamene unali kuzinvela, 57 pamene zoipa zako zikalibe kuululika. Manje uli kunyozewa na bana bakazi ba Edomu na kuli bonse bana bakazi baku Afilisti womuzungulila- wonse abo wokuzungulila bakuonelamo. 58 Uzalangiza manyazi yako na zonyansa za machitidwe yako!-- uku ndiye kukamba kwa Yehovah! 59 Akamba Ambuye Yehova, Nizakuchitila iwe choyenela, iwe wamene wapepusa kulumbila kwako na kupwanya chipangano. 60 Koma ine nizakumbukila chipangano changa chamene ninachita na iwe mumasiku ya ufana wako, ndipo nizapangana nawe chipangano chamuyaya. 61 Pamenepo muzakumbukila njila zanu, na kuchita manyazi polandila mulongo wanu na bakalongosi banu; Nizapeleka kwa iwe ngati bana bakazi, koma osati chifukwa cha chipangano chake. 62 Ine wamene nizankazikisa chipangano changa na iwe, ndipo uzaziba kuti ndine Yehova. 63 Chifukwa cha ivi vinthu, uzaitana vilivonse kunzelu zako na kunkala wamanyazi, ndipo siuzasegulapo kamwa kako nakukamba chifukwa cha nsoni, pamene nakukululukila pali vonse vamene wachita-uku ndiye kukamba kwa Ambuye Yehova."