Mutu 26

1 So Agiripa anakamba kuli Paulo, "Zikambile iwe weka." So Paulo ananyamula kwanja nozidifenda. 2 "Niziyesa okondwela ine neka, Mfumu Agiripa, kuti nikambe mulandu wanga pameso yanu siku yalero kusushana nazonse zamene Ayuda anipasa; 3 makamaka, cifukwa muziba bwino malamulo namafunso yonse ya Yuda. So nipempha kuti mumvelere bwino bwino. 4 Zoona, a Yuda onse aziba mwamene ninankhalila kucoka ku ufana wanga muzi ziko yanga namu Yelusalemu. 5 Ananiziba kucokela poyamba ndipo afunika kubvomela kuti ndine mu Falisi, kagulupu koikako nzelu pali cipembezo cathu. 6 Koma manje niimilila pano kuti niweluziwe cifukwa nisakila lonjezo yamene Mulungu anapanga kuli azitate anthu. 7 Cifukwa iyi ndiye lonjezo yamene mitundu ili 12 inayembekeza kulandila pamene enzo yamika Mulungu usiku namu zuba. Nipali ciyembekezo ici, Mfumu Agiripa, yamene Ayuda anipasila mulandu. 8 Cifukwa nicani kuti winangu waimwe kuti muganize kuti nicodabwisa kuti Mulungu aukisa akufa. 9 Panthawi inangu ninaganiza paine neka kuti nifunika kucita vinthu vambili vosushana nazina ya Yesu waku Nazareti. 10 Ninacita izi mu Yelusalemu. Nnakhomela okhulupilira ambiri mujele kupitila mu mphabvu zamene ninalandila kucokela kuli mkulu wa nsembe, ndipo pamene anapaiwa, ndipo ninaponya voti yanga kusushana nawo. 11 Ninabapasa cilango nthawi zambiri muma sinagoge ndipo nenzoyesa kubakakamiza kuti anyozele. Ananikwiisa maningi ndipo ninabasausa namumatauni yenangu. 12 Pamene nenzo cita ivi, ninayenda ku Damasikasi namphavu na malamulo yocokela kwa mkulu wa nsembe; 13 ndipo nili munjila, pakati pa siku, Mfumu, ninaona laiti kucoka ku mwamba yamene yenzeli yoyaka maningi monga zuba ndipo inasanika pali ine nabanthu enzoyenda naine. 14 Pamene tonse tinagwa pansi, ninabvela mau kukamba naine yamene inakamba mucitundu caci Heberi, 'Saulo, Saulo, nicifukwa nicani unisausa ine? Nicovuta kuti iwe umenye Mulungu. 15 Ndipo ninakamba ati, 'Ndimwe ndani, Ambuye?' Ambuye anayakha, Ndine Yesu wamene usausa. 16 Manje nyamuka ndipo imilila; cifukwa pa colinga ici ninaonekela kwa iwe, kukusankha kunkhala wanchito namboni pali zinthu zamene uziba pali ine na zinthu zamene nizakuonesa pasogolo pake; 17 ndipo nizakupulumusa kuli anthu na Akunja kwamene nikutuma, 18 kuti ukasegule menso yabo nobatembenula kucoka ku mdima kubaleta ku laita ndipo kucoka kuli satana kubabwelesa kwa Mulungu, kuti bangalandile Mulungu nakukhululukiwa macimo nakatundu wamene nibapasa wamene nipatula kwa ine mwacikhulupiliro mwa ine.' 19 Cifukwa caici, Mfumu Agiripa, sindinacitile mwano maso mphenya yakumwamba; 20 koma kwa iwo aku Damasikasi coyamba, wokokhapo ku Yelusalemu, ndipo namuziko yonse ya Yudeya, ndiponso na Akunja, ninalalikila kuti atembenuke kwa Mulungu, cocita zinthu zoyenela kulapa. 21 Cifukwa ca ici Ayuda ananimanga ine mu tempele nofuna kunipaya. 22 Mulungu anithandiza kufikila manje, so niimilira kupelekela umboni kuli anthu wamba nakuli olemekezeka sipakhani iliyonse koma zamene aneneri na Mose anakamba zizacitika, 23 kuti Kristu afunika kubvutika, ndipo azankhala oyamba kuuka kwa kufa kuti alalikile laiti kuli Ayuda na Akunja." 24 Pamene Paulo anasiliza kuzidifenda, Fesitasi anakamba mopunda, Paulo, ndiwe ofuntha; pamphunziro yako yakufunthisa." 25 Koma Paulo anakamba ati, sindine ofuntha, olemekezeka Fesitasi; koma molimbika nikamba mau ya zoona namaganizo yali bwino bwino. 26 Cifukwa mfumu iziba pali izi zinthu; ndiponso nikamba momasuka kwa yeve, cifukwa nilinaco cisimikizo kuti kulibe pali izi zili zobisika kuli yeve; cifukwa izi sizina citike mobisika. 27 Mukhulupilira aneneri, Mfumu Agiripa? Niziba kuti mukhulupilira." 28 Agiripa anakamba kwa Paulo, "Pakanthawi kocepa ufuna kuti unikoke nonipanga kunkhala mu Kristu?" 29 Paulo anakamba ati, "Nipemphela kwa Mulungu, kuti ngankhale pakanthawi kocepa kapena nthawi itali, osati imwe cabe, koma onse amene anibvela lero, mungankhale monga ine, koma osati akapolo monga ine." 30 Pamene apo Mfumu inaimilila, na govana, na Benisi, nabaja bamene enze anankhala nabo; 31 pamene anacoka mu holo, anakambisa nokamba ati, "Uyu munthu kulibe camene wacita kuti afe kapena kunkhala mujele." 32 Agiripa anakamba ati kuli Fesitasi, "Uyu munthu sembe anamasuliwa ngati sanapeleke nkhani kwa Siza."