1 Manje Fesitasi anangene mu mzinda, ndipo patapita masiku yatatu, anayenda kucoka ku Sezariya anafika naku Yelusalemu. 2 Mkulu wa nsembe na Yuda bozibika bwino analeta mulandu pali Paulo kwa Fesitasi, ndipo banakambisisa maningi kwa Fesitasi. 3 Ndipo banapempha Fesitasi kuti aba citeko bwino pali Paulo, kuti amuitane kuti abwele ku Yelusalemu kuti bamupayile munjila. 4 Koma Fesitasi anayankha kuti Paulo anali kaidi waku Sezariya, ndipo kuti yeve manje manje enzobwelela kuja kwamene. 5 "Cifukwa caici, baja bamene bakwanisa," anakamba yeve, afunika kuyende pamozi naise. Ngati pali bvuto iliyonse pali uyu munthu, muzamupasa mulandu." 6 Pamene anankhalako masiku 8 olo 10, anayenda ku Sezariya. Nipo pasiku yokonkhapo, anakhala pamupando oweluzila ndipo analamulila kuti Paulo abwele kwa yeve. 7 Pamene anafika, Ayuda aku Yelusalemu anaimilila pafupi, ndipo analeta milandu yambili yamene sibana puluve. 8 Paulo anazidifenda nokamba ati, "Sininacita kanthu koipa pali lamulo ya Ayuda kapena pali tempele kapena pali Seza." 9 Koma Fesitasi anafuna kuti Ayuda amukonde , ndipo anayankha Paulo nokamba ati, "Ufuna uyende ku Yelusalemu kuti nikakuweluzila pali izi zinthu?" 10 Paulo anakamba, " Ni imilila pamaso pamupandu waciweluzo wa Seza kumwene nifunika kuweluziwa. Sininalakwila Muyuda aliyense, monga iwe uzibila bwino. 11 Koma ngati nacita coipa ndipo nacita camene cifunikila imfa, sinikana kumwalila. Koma ngati palibe milandu, kulibe wamene angani peleke kuli beve. Ni itana Siza." 12 Pamene Fesitasi anakamba naba Nkhanso, anayankha kuti, waita Siza; uzayenda kuli Siza." 13 Patapita masiku, Mfumu Agiripa na Benisi anafika ku Sizariya kuti ayendele mwapadela Fesitasi. 14 Pamene anankalako masiku yambili, Fesitasi anapeleka nkhani ya Paulo kuli mfumu; anakamba ati, Munthu winangu anamusiya Feleki kuno monga kaidi. 15 Pamene nenzeli ku Yelusalemu, mkulu wa nsembe na akulu ba Ayuda analeta milandu kwa ine pali uyu munthu, ndipo banafuna ine kuti nimuweluze. 16 Pali ici ninayakha kuti simwa mwambo wa Aroma kuweluza munthu monga mwamene bafunila; koma, koma munthu anamulandu ali namupata kuti akumane nabomupasa mulandu kuti azidifende pali milandu yamene anamupasa. 17 So, pamene anabwela pamozi kuno, sininayembekezele, koma siku yokonkhapo ninankhala pamupando oweluzila ndipo ninalamulila kuti amulete. 18 Pamene omupasa mulandu anaimilira nomupasa mulandu, ninanganiza kuti panalibe mulandu wene wene pamilandu yamene anamupasa. 19 Mmalo mwake, enzeli namukangano nayeve pali cipembezo cawo napali Yesu winangu wamene anafa, wamene Paulo akamba ati alimoyo. 20 Ninasokonezeka mwamene ningafufuzile iyi nkhani, ndipo ninamufunsa ngati tingayende ku Yelusalemu kuti akaweluzidwe kwamene uko pali izi nkhani. 21 Koma pamene Paulo anapempha kuti aganding'iwe kuti amvele nganizo ya empala, ninalamulila kuti amusunge paka nimutume kuli Siza." 22 Agiripa anakamba na Fesitasi, "Nifuna naine nimumvele uyu munthu." "Mailo," Fesitasi anakamba ati, "Uzakamumvela." 23 So siku yokonkhapo, Agiripa na Benise anabwela na mwambo maningi; banangene mu holo nasilikali nabanthu bozibika mu tauni. Pamene Fesitasi anakamba lamulo, Paulo anamubwelesa kuli yeve. 24 Fesitasi anakamba ati, "Mfumu Agiripa, naimwe onse amuna muli naise muno, mwamuona uyu munthu; onse gulu ya Ayuda anapempha nzeli kuli ine mu Yelusalemu na kuno nakweve, ndipo anapunda kwa ine kuti asankhale futi na moyo. 25 Ninazindikila kuti sanapange mulando ufunika kupaiwa; koma anaitana empala, ndipo ninaganiza kumutuma. 26 Koma nilibe cene cene kuti nilembele kuli empara. Cifukwa caici, namubwelesa kwa iwe, maka-maka kwa iwe, Mfumu Agiripa, kuti ningankhale navo volemba pali uyu mulandu. 27 Cifukwa sicioneka bwino kwa ine kupeleka kaidi ndiponso kukamba milandu yake."