Mutu 22

1 "Abale na batate, mvelani kuzidifenda kwanga kwamene nipeleka kwa imwe." 2 Pamene gulu inamvela Paulo kukamba nabeve mucitundu caci Heberi, banankhala zii. Anakamba ati, 3 Ndine mu Yuda, obadwila mu Tasasi ku Silisiya, koma ophunzilila mu tauni ino kuli Gamaliyelo.Ninaphunzisiwa kulingana na njila zacilamulo zamakolo bathu. Ndine wacangu pali Mulungu, monga mwamene mulili imwe monse lero. 4 Ninasausa ba kristu kufika nopaya; ninamanga bamuna nabakazi pamozi nobapeleka mujele. 5 Ndipo mkulu wa nsembe na azikulu angapelekele umboni kuti ninalandila makalata kucoka kuli beve pali ba bale ali ku Damasikasi, kuti ine niyende kuja. Nenzo funika kuleta akristu womangidwa ku Yelusalemu kuti bapanishiwe. 6 Cinacitika kuti pamene nenzo yenda nonkhala pafupi na Damasiko, camuzuba mwazizi laiti ikulu kucoka kumwamba inasanika kuzunguluka ine. 7 Ninagwa pansi nakumvela mau kukamba naine, 'Sauli, Sauli, nicifukwa nicicani unasausa ine? 8 Ninayankha, Ndimwe ndani Ambuye?' Anakamba naine kuti, 'Ndine Yesu waku Nazareti, wamene unzunza.' 9 Baja bamene anali naine banaiwona laiti, koma sibanamvesese mau yauja wamene anakamba naine. 10 Ninakamba ati, Nicite bwabji, Ambuye?' Ambuye anakamba naine ati, ' Nyamuke uyende ku Damasikasi; kuja uzauziwa zonse zamene ufunika kucita.' 11 Sinenzo kwanisa kubona cifukwa ca kuyaka ca laiti ija, so ninayenda ku Damasikasi kusogolelewa nabaja wamene enzeli na ine. 12 Kuja ninakuma namwamuna zina lake ni Ananiyasi, mwamuna ozipeleka kulingana nalamulo ndipo ba Yuda bonse bonkhala kuja banakamba zabwino pali yeve. 13 Anabwela kwa ine, noimila pafupi naine, nokamba ati, 'Mubale Sauli, landila maso yako.' Munthawi yamene iwo ninayangana. 14 Ndipo anakamba ati, Mulungu wamakolo yathu akusankha iwe kuti uzibe cifunilo cake, kuti uwone Iye Olungama, ndipo kuti umvele mau yocokela pakamwa pake. 15 Cifukwa uzankhala mboni yake kubanthu bonse pazamene waona nomvela. 16 Manje nicifukwa nicani uyembekezela? Nyamuka, nobatizika, nosunka macimo yako, kuitana pazina lake.' 17 Pamene ninabwelela ku Yelusalemu, ndipo pamene nenzopemphela mu tempele, cinacitika kuti ninapasiwa maso mphenya. 18 Ninamuwona akamba naine, Indisa yenda ku Yelusalemu mwamusanga, cifukwa sibazalandila umboni wako pali ine.' 19 Ninakamba ati, Ambuye beve beka baziba kuti ninamanga nomenya baja bamene anakhulupilila mwa imwe mu sinagoge ili yonse. 20 Pamene mwazi wa Stefano mboni yanu unatika, nenzo yembekezela nogwilizana nazo, ndipo nizogading'a malaya baja bamene anamupaya.' 21 Koma anakamaba ati kwa ine, 'Yenda, cifukwa nizakutuma kwa Akunja." 22 Banthu banamulo kuti akambe kufika apa. Koma banapunda nokamba ati, Mupayeni sitimufuna pano pacalo: sicofunikila kuti ankhale na moyo." 23 Pamene benzeli kupunda, kumuponyela malaya yabo, noponya kalukungu mumwamba, 24 kapitawo mukulu analamulila kuti Paulo apelekewe mu malo yothabila. Analamulila kuti afunsiwe namikwapu pamene, kuti yeve aziba nicifukwa nicani benzo pundila yeve monga so. 25 Pamene banamumanga navinthambo, Paulo anakamba kuli musilikali wamene enze cilili pafupi, Kansi nicololedwa kukwapula munthu wamene ni mu Roma ndipo wamene sanaweluzidwe?" 26 Pamene musilikali anamvela izi, anayenda kuli kapitawo mukulu nomuuza kuti, kansi ufuna ucite cani? Uyu munthu ni sitizeni waku Roma. 27 Kapitawo mukulu anabwela nokamba ati kwa yeve, "Niuze, ndiwe sitizeni waku Roma?" Paulo anayankha ati, "Inde." 28 Kapitawo mukulu anayankha ati, "ninasebenzesa ndalama zambili kuti ninkhale sitizeni." Koma Paulo anakamba ati, ine ninabadwa sitizeni wa Roma." 29 Ndipo banthu benzo yenda umufunsa banamusiya pamene apo. Kapitawo mukulu nayeve anayopa, pamene anaziba kuti Paulo enze sitizeni wa Roma, cifukwa anazimangilila yeka. 30 Siku yokokhapo, kapitawo mukulu enzofuna kuziba coonadi pali mulandu wamene Ayuda anapasa Paulo. So anamumasula nolamulila akulu asembe na khanso yonse kuti bakumane. Pamene apo analeta Paulo nomuyika pakati pawo.