Mutu 3

1 Koma zibani ichi: pa masiku yosiliza pazankhala nthawi yobvuta maningi. 2 Banthu bazazikonda, bokonda ndalama, bozitukumula, banthota, bonyozela, bosamvera makolo, bosayamika na bopanda chiyelo. 3 Bopanda chikondi chobadwa nacho, wokonda kunyoza, bosazilesa, ba nkhanza, bosakonda zabwino. 4 Bamene bazapeleka banzao, bamambala, bokonda kusebela kuposa kukonda mulungu. 5 Bazankhala na maonekedwe ya umulungu koma mphamvu yake banaikana. chokani pakati pa banthu otero. 6 Chifukwa benangu ni banthu bamene bangena mumanyumba na kugwira bakazi bopusa. aba ni bakazi bamene nibozula na machimo elo bamayenda na zilako-lako zambiri. 7 Bakazi aba nthawi zonse bamapunzira, koma sibakwanisa kuziba chilungamo 8 munjira imozi-mozi mwamene jannes na jambres banaimilira mu njira ya mose. mu njira yamene iyi bapunzisi ba boza bamaimilira kusekeleza choonadi. ni banthu bowonongeka mu maganizo, bosasimikizilika pa chikulupiliro. 9 Koma sibazayenda patali maningi. kamba ka kuti upuba wabo uzazibika kuli bonse, monga mwamene chilili kuli bamuna benangu. 10 koma kwa inu, mwakonkha chipunziso changa, chinkhalidwe, chilingo, chikulupiliro, kupilira, chikondi, kuleza mtima, 11 zobvuta, manzunzo na zamene zinachitika kwa ine ku antioch, pa iconium na ku lystra. ninalimbikira kunzunzidwa. pa zonse, ambuye bananipulumusa. 12 bonse bamene bafuna kunkhala mwa mulungu mwa yesu khristu bazanzunzidwa. 13 banthu boipa na okopela chizankhala chobvuta maningi. bazasokoneza benangu. beve basokonezewa kudala. 14 Koma kwa inu, nkhalani mu zinthu zamene mwapunzira na kukulupilira mwa mphamvu. muziba kwamene mwazipunzira. 15 Muziba ati kuchoka pamene munali mwana mwaziba zolembedwa zopatulika. Ivi vikwanisa kukupangani kuti munkhale ba nzeru pa chipulumuso kupyolera mu chikulupiliro cha yesu khristu. 16 malembo yonse yanauzilidwa na mulungu. ni yaphindu pa chilamulo, pa kutsutsa, pa kukonza ni pa kupunzitsa pa chiyelo. 17 izi zili tero kuti munthu wa mulungu ankhale okwanira bwino, pa nchito zonse zabwino.