1 iwe, mwana wanga, limbikitsidwa mu chisomo chamene chili mwa yesu khristu. 2 zinthu zamene munamvera pakati pa mboni zambiri, ziperekeni ku banthu bokulupilika bamene bazakwanisa kupunzisa benangu. 3 Bvutikani na ine, kwati mu silikali wabwino wa yesu khristu. 4 Palibe musilikali wamene agwira nchito pamene ali na zinthu zobvuta zambiri za umoyo, kuti akondwerese basogoleri bake. 5 Komanso, ngati winangu apikisana pa kutamanga, sapasidwa mphoto pokapo ngati wasata malamulo. 6 nikofunikira kuti mulimi olimba pa nchito alandira gawo lake la mbeu poyamba. 7 Ganizirani zamene nikamba, pakuti mulungu azakupasani kumvesesa pa zonse 8 Kumbukirani yesu khristu, kuchoka ku mbeu ya davide, wamene anaukisidwa kwav akufa. Izi ni kulingana na uthenga wabwino wanga, 9 Wamene nibvutikira mpaka kunkhala kwati kawalala mu zingwe. koma mau ya mulungu siyali mu zingwe. 10 Kotero nipilila zinthu zonse kamba ka iwo bamene ni bosankhidwa, kuti nabeve bapeze chipulumuso chamene chili mwa khristu yesu na ulemelero wosatha. 11 zonena izi ndi zokulupilika: "ngati tafa nayeve, tizankhalaso na moyo nayeve. 12 Ngati tilimbika, tizalamulira nayeve. ngati timukana, nayeve azatikana, 13 ngati ndife osakulupilika, yeve ankhala okulupilika, chifukwa sangazikane yeka. 14 Pitirizani kuwakumbusa pa zinthu izi. muwachenjeze pamaso pa mulungu kuti sibafunika kuyambana pa mau. chifukwa cha ichi palibe chinthu chapindu. chifukwa cha ichi pali chionongeko kwa iwo bamene amvera. 15 Muyesese kuzipereka kwa mulungu ngati wamene avomelezedwa, wanchito wamene alibe chifukwa chochitira nsoni, wamene apunzisa mau ya chilungamo. 16 Pewani zokamba zopanda pindu, zamene zipangisa kuti munkhale kutali na umulungu. 17 Vokamba vao vizayenda monga gangari. Mwa iwo pali hymenaesus ni philetus, 18 aba ni banthu bamene baphonya choonadi. Bakamba kuti kuukisidwa kunachitika kudala. Bapindamula chikulupiliro cha benangu. 19 Koma, maziko yolimba ya mulungu yaimilira. yali na zolembedwa izi: "ambuye aziba wamene ali wake"na "aliyense wamene akamba pa zina la mulungu ayenera kuchoka ku njira zoipa." 20 Mu nyumba yochita bwino, mulibe zikopo chabe za golide na siliva. muli zikopo za mitengo na dothi. zina mwa izi ndi zogwirisa nchito molemekezeka, na zinango nchito zosalemekezeka. 21 Ngati winangu azisuka yeka pa nchito zosalemekezeka, ankhala chikopo cholemekezeka. apatulika, chofunikira kwa mwini wake, na chokonzedwa pa nchito zabwino. 22 thabani chilako-lako. funani chiyelo, chikulupiliro, chikondi na mutendere na iwo bamene baitana pa ambuye na mtima oyera. 23 Koma kanani upuba na mafunso ya ufontini. muziba kuti yamabala mukangano. 24 Kapolo wa mulungu safunika kuchita mukangano. 25 Mumalo mwake ayenera kunkhala odekha mtima kwa aliyense, okwanisa kupunzisa,na ofasa. ayenera kupunzisa mwachilungamo bamene bamushusha. mulungu angabapulumuse kamba ka nzeru za zoona. 26 Bangankhalenso bwino na kuleka musampha wa satana, pamene bagwiriwa kuchita nchito zake.