Mutu 2 9

1 Pamene Mfumukazi yaku Seba inanvela utenga pali Solomoni, anabwela ku Yerusalemu kuti amuyese na mafunso yolimba. Anabwela na kalavani yayitali kwambili, na ngamila zozula na vonunkila, golide yambili, na myala yamutengo wapatali yambili. Pamene anafika kuli Solomoni, anamuuza vonse vamene vinali mumutima wake. 2 Solomoni anamuyanka yonse mafunso yake; kunalibe chovuta kuli Solomoni; kunalibe funso yamene sanayanke. 3 Pamene Mfumukazi yaku Seba inaona nzelu za Solomoni na nyumba yaufumu yamene anamanga, 4 vakudya pa tebulo yake, ponkala pa banchito bake, nchito za banchito bake na vovala vawo, omupelekela chiko na vovala vawo, na nsembe zoshoka zamene anapeleka ku nyumba ya Yehova, munalibe na mpepo muli eve. 5 Anakamba kuli mfumu, "Nizoona, utenga wamene ninanvela mu ziko mwanga pa mau yako na panzelu zako. 6 Sininakulupilile vamene ninanvela mpaka pamene ninabwela kuno, ndipo menso yanga yaviona. Sipakati ninauziwa paza ukulu wa nzelu na chuma chako! Wachilapo pa utenga wamene ninanvela. 7 Niwodalisika kwambili bamuna bako, ndipo niwodalisika banchito bako bamene baimilila pasogolo pako, chifukwa banvela nzelu zako. 8 Adalisike Yehova Mulungu wako, wamene amakondwela naiwe, wamene anakufaka pamupando wake, kunkala mfumu ya Yehova Mulungu wako. Chifukwa Mulungu wako anakonda Israyeli, kuti abankazikise ku ntawi zonse, ndipo anakuikani kunkala mfumu yao, kuti muchite chiweluzo na chilungamo. 9 Anapasa mfumu matalente 120 yagolide, na zonunkila zambili, na myala yamutengo wapatali. Palibe zonunkila bwino zambili kuchila izi kuchila zamene mfumukazi ya ku Seba inapasa Mfumu Solomo zinapasiwa kuli eve. 10 Banchito ba Hiramu na banchito ba Solomoni, amene anabweretsa golide kuchokera ku Ofiri, anabwelesa matabwa ya mlamu ndi myala ya mutengo wapatali. 11 Mfumu inakonza masitepe a nyumba ya Yehova, ndi nyumba yake, na zeze, na azeze ndi azeze za oimbila; Mitengo ngati yamene inalibe kuonekapo mu ziko ya Yuda. 12 Mfumu Solomoni inapeleka kwa mfumukazi ya ku Seba chilichonse chamene inkafuna na chilichonse chamene inapempa; anamupasa vambili kuchila vamene inabwelesa ku mfumu. Ndipo inachoka na kubwelela ku ziko yake, eve na banchito bake. 13 Manje kulema kwa golide yamene inali kubwela kwa Solomoni mu chaka chimozi inali matalente 666 yagolide, 14 kuwonjezela pa golide yamene bamalonda na amalonda banali kubwelesa. Mafumu yonse yaku Arabiya na babwana mukubwa mu ziko nawo banabwelesa golide na siliva kwa Solomoni. 15 Mfumu Solomoni anapanga vishango vikulu vili 200 va golide yopangika. Masekeli yali 600 ya golide yanangenelana. 16 Anapanganso vishango vili 300 va golide wopondelezedwa. Mainasi yatatu yagolide ya pachikopa chilichonse; mfumu inaziponya munyumba ya musanga ya Lebano. 17 Ndipo mfumu inapanga mupando wachifumu waukulu wa minyanga ya njovu ndipo unakuta na golide woyengeka bwino kwambili. 18 Mpando wachifumuwo unali na masitepe yasanu na limozi, ndipo chopondapo mapazi chinali cholumikizidwa pampandowo. Kumbali iliyonse ya mpandowo panali mipando yolumikizila mikono iwili na mikango ibili inaimilila pambali pa chilichonse cha izi. 19 Mikango khumi ndi zibili zinaimilila pamakwelelo, imozi kumbali kwa inzake ya wina mbali iyi na imozi ya masitepe yasanu na limozi. Panalibe mupando wachifumu wolingana nauyo mu ufumu wina uliwonse. 20 Chiko chili chonse chomwelamo Mfumu Solomoni chinali chagolide, na chiko chilichonse zakumwa mu Nyumba ya Nkhalango ya Lebanoni zinali za golide boyenga bwino. Kunalibe chinali cha chifukwa siliva sibanali kuipenda mu masiku ya Solomoni. 21 Mfumu inali na zombo zapanyanja zambili, pamozi na zombo za Hiramu. Kamozi lyonse pa zaka zitatu zombozi zimabwelesa golide, siliva, minyanga ya njovu, komanso anyani na anyani. 22 Momwemo Mfumu Solomoni inachila mafumu yonse ya maziko yapansi mu chuma ndi nzelu. 23 Mafumu yonse yapa ziko lapansi yamafuna pamenso pa Solomoni kuti banvele nzelu zake, zamene Mulungu anaziyika mumutima mwake. 24 Bamabwela kuzapeleka musonko, zibiya zasiliva ndi zagolide, zovala, zida zankhondo, ndi zonunkhiritsa, komanso akavalo na nyulu, chaka na chaka. 25 Solomoni anali na makola 4,000 ya mahachi na magaleta, na bapakavalo 12,000, bamene anayika mumizinda ya magaleta na ku Yerusalemu. 26 Anakalamulila mafumu yonse kuyambila ku Mumana mpaka ku ziko ya Afilisiti, mpaka kumalile na Igupto. 27 Mfumu inali na siliva mu Yerusalemu, monga chabe minyala ili pansi. Anapanganso matabwa a mukunguza yolingana na mitengo ya mukuyu yamene ili ku chigwa. 28 Banabwelesa mahachi ya Solomoni kuchokela ku Igupto na maziko yonse. 29 Monga pa khani zinangu zokamba pali Solomoni, zoyamba na zosiliza, nanga sizinalembewe mu mbili ya muneneli Natani, mu uneneli wa Ahiya wa ku Silo, na mumasomphenya ya Iddo oona.(wamene naye anali na utenga pali Yeroboamu mwana mwamuna wa Nebat)? 30 Solomoi analamulila bonse ba Israeli mu Yerusalemu kwa zaka 40. 31 Anagona pamozi na makolo yake ndipo banamuyika mumanda mu muzinda wa Davide batate bake. Rehobowamu, mwana wake, anankala nfumu mumalo mwake.