Mutu Wa 4

1 Manje pamene Yesu anaziba kuti Afalisi ananvela kuti Yesu enzo panga no batiza bopunzila ba mbiri kuchila Yohane 2 (chingankale siYesu wamene anali kubatiza koma bopunzila bake ndiye benzeli kubatiza), 3 Anachokamo mu Yudeya no bwerela ku Galileya. 4 Koma chenzofunika kuti apitiretu mu Samariya. 5 Iye anangena mu komboni ya mu Samariya yenzo itaniwa Sukari, iyi komboni, yenze pa fupi na malo yamene Yakobo ana pasa mwana wake wa chimuna, Yosefe. 6 Chisime cha Yakobo chenzepo. Yesu anafuna kupumulako chifukwa ulendo unamulemesa. Ntawi yenze ku ma tweluvu. 7 Muzimayi waku Samariya anabwela kutapa manzi pamena paja pa chisime, Yesu anamuuza ati, "iwe muzimayi nipaseko manzi nimwe." 8 Ndipo bopunzila bake sibenzepo chifukwa banabwelela mu komboni mukugulako vakudwa. 9 Manje muzimayi waku Samariya anayanka Yesu ati, "nanga nichani iwe bambo wachi Yuda upempha manzi kwaine muzimayi wachi Samariya?" Chifukwa bantu ba Yudeya na bantu ba Samariya sibaendelana. 10 Yesu naye amuyanka ati, "asembe wenzoziba mphaso ya Mulungu, na wamene akuuza ati 'nipase chakumwa,' sembe wamupempha, nayeve sembe akupasako manzi ya moyo osasila." 11 Muzimayi anamuuza ati, "Bambo, baketi yotapilako manzi mulibe, ichi chisime nichitali ngako. Nanga manzi ya moyo muzayachosa kuti? 12 Ninshi mungamuchile tate wathu Yakobo, anatipasa chisime chamene ichi, nakumwamo eve pamozi nabana bake banalume na ng'ombe zake?" 13 Yesu anayanka muzimayi ati, "onse akumwa manzi yamene yachoka pa chisime ichi azanvela futi njota, 14 koma uyo wamene akumwa manzi yamene ine nipasa sazanvela njota futi. Ndipo manzi yamene nizamupasa yanzankala kasupe ka manzi mwayeve yo leta umoyo osasila." 15 Muzimayi amuuza Yesu ati, "Mbuye, nipaseni manzi yamene ayo nimweko pakuti, nisankanvele njota futi nileke kubwelanso kuno ku chisime mukatapa manzi masiko onse." 16 Yesu naye amuyankha ati, "iwe yenda ku nyumba kwako uyitane mwamuna wako, mubwele bonse kuno." 17 Muzimayi anamuyanka kuti, "nilibe mwamuna." Yesu anayanka kuti, "ndipo wakamba zoona kuti ulibe mwamuna, 18 chifukwa iwe unakwatiwapo ku ba muna faivi, ndipo wamene uli naye apa si mwamuna wako, ni gayi wako chabe. Chamene wakamba ni chazoona." 19 Muzimayi anakamba ati, "Ambuye, naona kuti imwe ndimwe m'neneri. 20 Makolo batu banalambila pa lu phiri apa, koma imwe mukamba ati ku Yerusalemu ndiye kumalo kwamene bantu bafunika kulambilila." 21 Yesu anamuuza ati, "nikulupirila ine, muzimayi, ntawi ibwela yamene simuzalambila Tate pa phiri apa, kapena mu Yerusalemu. 22 Imwe mulambila chamena simuziba. Ise tilambila chamene tiziba, chifukwa chipulumuso chichokela kwa Ayuda. 23 Koma, ntawi ibwela ndipo ntawi yafika, yamene bolambila ba zoona bazalambila Atate mu muzima na mu choonadi; chifukwa Atate basakila banthu ba so kuti bankale omulambila. 24 Mulungu ni Muzimu, ndipo bonse bolambila bafunika kulambila Ambuye mu muzimu na muchoonadi. 25 Muzimayi anakamba kwa iye ati "niziba kuti Mesiya abwela, (oitaniwa Kristu). Akabwela azatipunzisa zintu zonse." 26 Yesu anamuuza ati, "ine wamene ukamba naye pemeneapa ndine." 27 Pa ntawi yamene ija, bopunzila bake banabwelela. Manje banadabwa kupeza Yesu akamba namuzimayi, koma kulibe anakamba ati, "nichani chamene ufuna?" olo kuti "nanga nichani ukamba nauyu muzimayi?" 28 Ndipo uyu muzimayi anasiya poto yake yamanzi nobwerela ku komboni noyenda kuuza bantu ati, 29 "Bwelani, muone mwamuna wamene aniuza zonse zamene ninachita. Uyu sangankhare Kristu, angankhale?" 30 Banachokamo mu komboni no yenda kwa iye. 31 Pantawi yamene ija, bopunzila bake benze kumulikisa ati, "Mupunzisi, dyani." 32 Anabayanka ati, "ine niri nachakudwa chamene inu bonse simuziba olo pang'ono." 33 Bopunzila nabo bayamba kufunsani, "kulibe wamene amubwelesela chilichonse chakudwa, bushe bamuletela?" 34 Yesu abauza ati "chakudya changa nikuchita chifuniro cha iye wamene ananituma na kusiriza nchito yake. 35 Bushe simumakamba kuti 'kwasala chabe myezi folo kuti kukolola kuchitike?' Nikuuzani kuti imyani manso yanu no ona minda, chifukwa minda yakonzekela ku kolola na ku bweza va mu minda. 36 Uyo wamena akolola amalandila malipilo yake, ndipo akututa mbeu ku moyo osasila, pakuti ofesa ndi okolola akondwerere pa mozi. 37 Ndipo chineneri chokamba kuti, 'wina afesa, wina akolola,' ni cha chendi. 38 Ine nakutumani kuti mukolole minda yamene simunalime. Benangu banasebenza, imwe mwangena chabe munchito yamene ba nzanu banasebenza kudala. 39 Ba Samariya bambiri mu muzinda uja banayamba kumukulupirila Yesu chifukwa cha umboni wamene enzo pasa uja muzimayi, kuti, "ananiuza zonse zamene ni nachita." 40 Pamene ba Samariya banabwela kwa iye banamupempa ati ayambe kunkala nabo, naye anankala nabo masiku yabili. 41 Na bambiri banakulupirila chifukwa cha mau yake. 42 Banamuuza muzimayi ati, "sitinakhulupirile futi chifukwa cha mau yamene watiuza, takhulupilila chifukwa cha mau yamene tazinvelera na mutu yatu, ndipo taziba kuti uyu ni mupulumusi wa ziko lonse." 43 Patapita masiku yabili, anachokako kuja no yenda ku Galileya. 44 Chifukwa Yesu wamene anakamba kuti muneneri sibamamupasa ulemu mu ziko lakwao. 45 Pamene anangena mu Galileya, anthu amu Galileya anamulandila bwino. Benze banaona zonse zamena anachita kuja ku Pwando inankhalila ku Yerusalemu, chifukwa aba banthu nabo benzeko ku Pwando yameni iyi. 46 Anabwelelanso ku Kana muzinda wa Galileya, kwamene anasanduza manzi vinyo. Ndipo kunali mukulu wina wa ufumu, mwana wake enze odwala ku Kapernaumu. 47 Pamene ananvela kuti Yesu achokako ku Yudeya no bwela ku Galileya, anayenda kwa Yesu no pempha kuti abwele achirise uja mwana enze pafuti na kufa. 48 Yesu anabauza kuti, "imwe ngati simunaone vizindikilo na zoziziswa, simuzakulupirila." 49 Mukulu uyu anamuuza ati, "Ambuye imwe, bwelani kuno mwamusanga mwana wanga akalibe kufa!" 50 Yesu anamuyankha ati, "Yenda. mwana wako ali na umoyo." Mwamuna uyu ana kulupirila zamene anakamba Yesu nakuyenda anayenda. 51 Akali kuyenda, ba nchito bake banakumana naye pa njila naku muuza ati mwana wako ali namoyo. 52 Ndipo anabafunsa ntawi yamene mwana anachirisidwa, nabo banamuyanka ati "anachirisidwa mailo na ntawi ya wanu koloko ya mu zuba." 53 Ndipo tate wamwana ana zindikila kuti iyo nthawi yenze pamene Yesu ananena ati "mwana wako ali na umoyo." Iye na banja yake yonse inakhulupirila mwa Yesu. 54 Ichi ndiye chizindikilo chachibiri chomwe anachita Yesu paneme anachoka ku Yudeya no yenda ku Galileya.