Yohane mutu 14

1 "Musaleke mitima yanu ivutike. Khulupirilani mwa Mulungu, ndipo khulupirilani mwainenso. 2 Munyumba ya Tate wanga alimo malo yonkalamo yambiri. ngati sichinali so, sembe ninakuuzana, chifukwa nayenda kukonza malo anu imwe. 3 Nikaenda no kukonzhelani malo imwe, nizabwela ndipo nizakulandilani kwaine pakuti kwamene nili naimwe mukhankeleko. 4 Muiziba njiila ya kwamene niyenda." 5 Thomasi ananena kwa Yesu, "Ambuye, sitiziba kwamene muyenda, nanga njiila tingaiziba bwanji?" 6 Yesu anamuuza ati, ine "ndine njiila, ndine choonadi ndipo ndine moyo, kulibe wina angabwele kwa Tate kupanda mwaine. 7 Ngati mwenze kuniziba asembe munamuziba naeve Tate wanga. Kuchoka apa mwamuziba, ndipo mwamuona." 8 Filipo anakamba kwa Yesu, Ambuye, tilangizeni Atate, icho chabe chizatikwanila." 9 Yesu anakamba kwa iye, "nankala naimwe ntawi itali maninga koma sumuniziba, Filipo? Aliense aniona amuona Tate. Manje iwe ungakambe bwanji ati, 'tilangize Tate'? 10 Ninshi sukhulupirila kuti ine nili muli Tate na Tate ali mwaine? Mau yamene nikuuzani imwe sinikamba mu mphavu zanga iyayi, koma ni Tate wamene ankhala mwaine wamene achita chinto yake. 11 Nikhulupirileni kuti ine nili mwa Tate, na Tate ali mwaine, ndiponso khululupirani chamachitidwe yamene. 12 Choonadi, Choonadi, nikuuzani kuti uyo wamene akhulupirila mwaine azachita nchito zamene nichita, ndipo azachitanso nchito zikulu kupambana nazamene izi chifukwa ine niyenda kwa Tate. 13 Zonse zamene muzapempa muzina langa, nizakuchitilani pakuti Tate alemekezediwe mu Mwana mwamuna. 14 Mukanipempa chilichonse muzina yanga, nizakuchitilani. 15 Ngati munikonda imwe, muzasungu malamulo yanga. 16 Ndipo nizakupempelelani kwa Tate wanga, naye azakupasana Omipuzya(Omitontoza) wina pakuti akankhale naimwe masiku onse: 17 Muzimu wa choonadi. Wamene ziko singalandile chifukwa sinamuonepo ndipo simuziba iyayi. Koma inu mumuziba, chifukwa ankhala naimwe ndipo anzankhala mukati kaimwe. 18 Sinizakusiyani mweka; nizabwela futi kwainu. 19 Ndipo ntawi ing'ono ziko sizanionanso, koma imwe muniona. Chifukwa ine nili na umoyo, nainu muzankala na umoyo. 20 Pasiku ija muzaziba kuti ine nili mwa Tate, ndipo inu muli mwaine, naine nili mwainu. 21 Wamene ali namalamula yanga ndipo ayasunga ninsi niwamene anikonda, elyo wamene anikonda azakondewa na Tate wanga, nainenso nizamukonda na kuilangiza ine kwaeve. 22 Yuda (uyu si Isikario iyayi) anuuza Yesu ati, "Ambuye, nanga nichani muzazilangizi mweka kwaise osati ku ziko?" 23 Yesu anamuyanka no kamba kwaeve kuti, "ngati muntu aliyense anikonda, azasunga mau yanga. Tate wanga azamukonda, ndipo tizabwela kwaiye nakumanga nyumba yatu naye. 24 Wamene sanikonda samasunga mau yanga. Mau yamene munvela siyachokela kwaine koma niyochokela kwa Tate wamene ananituma. 25 Nakuuzani zinthu izii, nikali kunkhala naimwe. 26 Koma, Mutonthozi - Muzimu Oyela wamene Tate azatuma muzina langa - iye azakupunzisani zonse ndipo azakukumbusani zonse zamene nakuuzani ine. 27 Nakusiyilani mutendere; nakupasani mutendere. Sinikupasani mwamene ziko ipasila. Mutima wanu usavutike, ndipo musayope. 28 Munanvela kuti nakuuzani imwe, 'Ine niyenda, ndipo nizabwelanso kwaimwe.' Ngati mwenzonikonda, asembe mwakondwera kuti niyenda kwa Tate, chifukwa Tate nimukulu kunichila ine. 29 Manje nakuuzani chikalibe kuchitika, chikachitika muzakulupirila. 30 Sinizakambanso futi zambiri na imwe, chifukwa olamulila ziko ili lapansi abwela. Alibe mphavu pa ine, 31 koma pakuti ziko izibe kuti ine nikonda Tate, nichita chabe mwamene Tate ananilamurila. Tiyeni tinyemuke, tichokepo apa.