1 1ndipo nina pindamuka na kunyamula menso yanga, ndipo ni naona, cholembelapo chimbululuka! 2 2mungelo anakamba na ine, ''uona chani?'' ninayanka, ''niona cholembelapo chimbululuka, mupimo okwanila 20 mu utali ndiponso 10 mu ukulu.'' 3 ndipo anakamba kuli ine, ''iyi nitembelelo yamene iyenda pa ziko yonse ya pansi. pakuti kawalala ali wonse az jubiwako kulingana na vamene vina lembewa kumbali inango, ndiponso ali wonse wamene alumbila va boza aza chosewako kulingana na vamene vina lembewa kumbali inango. 4 4''niza itumiza-uku nikukamba kwa YEHOVA wamakamu-mwa ichi izangena munyumba ya kawalala na munyumba ya wamene alumbila va boza pa zina yanga. izankalilila munyumba mwake na kuononga mitengo ya timba na myala.'' 5 ndipo mungeli wamene enzo kamba na ine anachoka panja na kukamba kuli ine, ''nyamula menso yako na kuona chamene chibwela!'' 6 6ninakamba, '''nichani?''anakamba, ''iyi ni swanda yamene ili nagondolo yamene ibwela. uyu ni uchimo wao muziko lonse.'' 7 7ndiponso chivininkilo china chosewapo pa swanda ndiponso munali muzimai pansi pake enze nkezi mukati mwa swanda! 8 8mungeli anakamba, ''uku nikuipisa!'' anamuponya kumubweza mu swanda, ndiponso anabwezelapa chivalilo. 9 9 ninanyamula menso yanga nakuona bazimai ba bili babwela kuli ine, ndiponso pempo inali mumapapiko yao-pakuti banali na mapapiko monga ya kakowa. bana nyamula swanda pakati pa ziko na kumwamba. 10 ndipo nina kamba kuli mungeli wamene enzo kamba na ine, ''bapeleka kuti swanda?'' 11 11anakamba kuli ine, ''ku imangila tempele mu ziko ya shinara, kuti tempele ikasila, swanda iza ikiwa pa malo yake yokonzewa.''