1 Mumwezi wa 8 muchaka cha chibili cha ulamulilo, wa darius, mau ya YEHOVA yanabwela kuli zekariya mwana mwamuna wa berekiya mwana mwamuna wa ido, muneneli, kukamba, 2 ''YEHOVA ana kwiya maningi na mazi tate yanu! 3 Kamba kuli beve, YEHOVA wamakamu akamba ichi: bwelani kuli ine!-uku nikukamba kwa YEHOVA wa makamu- ndiponso nizabwelela kuli imwe, akamba YEHOVA wa makamu. 4 Musankale monga ba zitate banu bamene ba neneli bana lilila kumbuyo uku, kukamba, ''YEHOVA wa makamu akamba ichi: chokani kuma yendedwe yanu ya uchimo na vochita vanu voyipa!'' koma sibana fune kuvela ndiponso sibana ike nzelu kuli ine-ivi nivokamba va YEHOVA,' 5 Mazitate yanu, yali kuti? ba neneli bali kuti, nanga bali pano muyayaya? 6 Koma mau yanga na vokamba vanga vamene nina lamulila ba kapolo banga ba neneli, sivina yende pa sogolo pa mazi tate yanu? mwa ichi bana tembenuka na kukamba, ' monga mwamene YEHOVA wa makamun enzo ganizila kuchita kuli ise vamene mayendedwe na ma chitidwe yatu yenzo yenela, ndipo atichita vamene ivo, ''' 7 7pasiku ya 24 mumwezi wa 11, wamene uli mwezi wa sebati, muchaka cha chibili mu ulamulilo, wa dariusi' mau ya YEHOVA yana bwela kuli zekariya mwana mwamuna wa berekiya mwamuna wa ido, muneneli, kukamba, 8 8''nina wona usiku, na , kuyangana! mwamuna ninshi akwela pa kavalo yo fira, ndipo anali mukati mwa mitengo za masamba zili mu chigwa; ndipo kumbuyo kwake kunali aka valo bo fira, bo sweta na boyera.'' 9 Nina kamba, '' nivichani ivi vintu, ambuye?'' ndipo mungeli enzo kamba na ine ana kamba kuli ine, ''nizakulangiza kuti ivi vintu nivi chani.'' 10 10ndipo mwamuna enze ana yimilila pakati pa mitengo za masamba ana yanka, ''aba ni abo YEHOVA atuma kuyenda muziko yonse ya pansi kuyenda yenda.'' 11 bana muyanka mungeli wa MULUNGU wamene ana yimilila pakati pa mitengo za masamba; bana kamba kuli eve, ''tankala tingo yenda yenda mu ziko yonse ya pansi; ona, ziko yonse inkala ili zii ndiponso ili pa mupumulo.'' 12 12ndiponso mungeli wa YEHOVA una yanka na kukamba, ''YEHOVA wa makamu, muzankala ntawi itali bwanji kulibe kulangiza chifundo kuli yelusalema na ku mizinda za yuda, yamene mwankala muli nayo na ukali pa zaka 70?'' 13 13 YEHOVA ana yanka mungeli wamene enze ana kamba na ine, na mau yabwino, mau yo tontoza. 14 14ndipo mungele enze ana kamba na ine anakamba kuli ine, ''itana na kukamba, 'YEHOVA wa makamu akamba ivi: nankala ni chitila nsanje yelusalema ndiponso ziyoni na chilako lako chikulu! 15 Ndine okalipa maningi na mayiko yali pa mutendele. pamene nenze wokalipa che pa ng'ono na beve, ba vionongelatu vintu. 16 16 mwa ichi YEHOVA wa makamu akamba ichi: nabwelela kuli yelusalema na chifundo chambili. nyumba yanga iza mangiwa mukati mwake- aya ndiye mau ya YEHOVA wa makamu-ndiponso ntambo yo pimila iza tambasuliwa kunja kuli yelusalema!' 17 17 futi uyitane, kukamba, 'YEHOVA wamakamu akamba ivi: mizinda yanga iza taikila futi na vabwino, ndiponso YEHOVA aza tontoza futi ziyoni, ndiponso aza sanka futi yelusalema.''' 18 18 ndiponso nina nyamula menso yanga kumwamba na kuona nsengo zili 4! 19 19nina kamba na mungeli anakamba na ine, ''ni vichani ivi?'' ana niyanka. ''izi ni nsengo zamene za palanganya yuda,isilayeli, na yelusalema.'' 20 20 ndipo YEHOVA ananilangiza bobeza bali 4. 21 21ninakamba, ''aba bantu ba bwela kuchita chani?'' anayanka, na kukamba, ''izi ni nsengo zina palanganya yuda kuti kusankale muntu lai wonse wonyamula muttu. koma ba misiri babwela kuba yofya. kugwesa nsengo za mayiko yamene yana nyamula nsengo yao kuyofya ziko