Mutu 8

1 Kulibe manje kususiwa kwa baja bali mwa Yesu Christu. 2 Pakuti lamulo ya muzimu ya umoyo mwa Yesu Christu yanimasula ku mphamnvu ya chimo na infa. 3 Chifukwa chamene lamulo sinakwanise chifukwa inalibe mphamnvu kupitila muthupi, Mulungu anakwanisa. Anatuma mwana wake uchimo muchifanizilo cha uchimo wa munthu, kunkhala chopeleka ku chimo, anasusa chimo muthupi. 4 Anachita ichi kuti, zofunika za lamulo zikwanilisike muli ise,ise bamene sitiyenda kulingana na thupi, koma kulingana na muzimu. 5 Baja bamene bankhala kulingana na thupi,bayika nzelu ku zinthu zakuthupi, koma baja bamene bankhala kulingana na muzimu, baika nzelu kuzinthu zaku uzimu. 6 Pakuti kuika nzelu pazathupi ni infa.koma kuika nzelu kuzinthu zaku uzimu niumoyo namtendere. 7 Kuika nzelu pazinthu zakuthupi nimkwiyo kwa Mulungu.chifukwa sichigonjela ku lamulo ya Mulungu,ndipo sichikwanisa kuchita telo. 8 Baja bamene bali muthupi sibangamukondwelese Mulungu. 9 Koma imwe simuli muthupi koma mumuzimu, Ngati nizoona kuti muzimu wa Mulungu unkhala muli imwe.koma ngati mutnu alibe muzimu wa Christu, ninshi siali wake. 10 Koma ngati Yesu ali muli imwe,ninshi thupi niyakufa ku chimo, koma muzimu ali namoyo kuchiyelo. 11 Ngati muzimu wamene anausa Yesu Christu ankhala muli imwe, uja wamene anausa Christu ku infa azapasa futi moyo kumathupi yanu kupitila mu muzimu wamene akhala muli imwe. 12 Manje abale na imwe bankhongole,koma kuthupi kunkhala monga baku thupi. 13 Chifukwa ngati munkhala kulingana na thupi, mulipafupi nakufa, koma ngati mwauzimu,mupaya zochitika za thupi, muzankhala na moyo. 14 Koma onse bamene basogololewa na muzimu nibana ba Mulungu. 15 Pakuti simunalandile muzimu waukapolo kuti munvele mantha. Munalandila muzimu wakutengewa monga bana, muli eve tilila kuti Aba Tate. 16 Muzimu uchitila umboni na muzimu wathu kuti ndise bana ba Mulungu. 17 Ngati ndise bana, ndise futi oloba,oloba ba Mulungu. Ndipo ndise oloba na Yesu, ngati tivutika naye kuti tikakwezedwe futi na eve. 18 Chifukwa niona kuti mabvuto yamene tipitamo manje siyangalingane na ulemelelo wamene uzabvumbulusiwa wa ise. 19 Pakuti chiyembekezelo chakuya chachilengedwe chiyembekezela chivumbuluso cha bana ba Mulungu. 20 Pakuti chilengedwe chinawoneka kuti chilibe phindu, osati kuchifunilo chake, koma kwa uja wamene anachiwonesela. 21 Nichisinsi chosimikizika, kuti chilengedwe chamene chizamasulidwe ku ukapolo ku kuola, nakuti chizabwelesedwa ku ufulu wa ulemelelo wa bana ba Mulungu. 22 Tiziba kuti chilengedwe chonse chibuula,nakusebenza mukubaba pamozi kufikila manje. 23 Osati chabe ichi, koma naife bamene,tilinazo zipaso za Muzimu, naise tibuula mkati mwa ise, kuyembekeza kutengewa monga bana, kupulumusidwa kwa mathupi yathu. 24 Kamba ka chisimikizilo ichi tinapulusiwa, pakuti chamene tisikizila chizachitika chikalibe kuwoneka, nanga nindani wamene ayembekezela chinthu chamene waona kudala. 25 Koma ngati tilinacho chisimikizo cha vinthu vamene tikalibe kuona, tichiyembekeza moleza mtima. 26 Munjila imozi muzimu atithandiza muzofoka zathu.Pakuti sitiziba mopemphelela,koma muzimu amatipemphelela na kubuula kwa kuya. 27 Wame asecha mitima azaiba maganizo ya muzimu, chifukwa apemphelela okhulupilika kulingana na chifunilo cha Mulungu. 28 Tiziba kuti baja bamene bakonda Mulungu,vinthu vonse visebenzela pamozi ku ubwino wao,Baja oitanidwa kulingana na chifunilo cha Mulungu. 29 Chifukwa bamene anaziba, anabakonzela sogolo kuti akalingane na chifanizilo cha mwana wake.kuti akankhale mwana oyamba pali abale bake bambili. 30 Baja bamene anaizibilatu sogolo yao,aba anabaitana, Baja bamene anaitana, anabalungamisa, Bamene analungamisa anabakwezeka. 31 Nanga tizakamba chani pali ivi vinthu?Ngati Mulungu alikumbali yathu nindani angatisuse? 32 Eve wamene sanachite kaso na mwana wake koma anamupeleka kwa ife tonse,nanga azaleka bwanji kutipasa zonse zamene tifuna? 33 Nindani azabwelesa kususa bana ba Mulungu? Mulungu ndiye wamene amalungamisa. 34 Nindani azatisusa? Yesu ndiye wamene anatifela,kupitililapo anaukisidwa.Alamulila na Mulungu pa malo yaulemelelo.ndipo niyeve atipemphelela ise. 35 Nindani azatilekanisa ku chikondi cha Mulungu?Manzunzo,zovutisa,zobaba,njala,usiwa,koyofyewa kapena lupanga? 36 Monga mwamene chinalembedwa,kuti imwe mukaphindule tipaiwa siku lonse,tingewa monga nkhosa zamene ziyenda kupaiwa. 37 Muvonse ivi tichila baja bopambana, kupitila muli wamene anatikonda, 38 Pakuti nilinacho chisimikizo kuti, ngakhale infa, kapena umoyo, angelo, maulamulilo, vinthu vamanje, kapena vinthu vakusogolo, kapena mphamvu, 39 mwamba kapena pansi, kapena chinthu chinangu chilichonse cholengedwa chizalekanisa ku chikondi cha Mulungu, chamene chili muli Yesu Christu mfumu yathu.