Mutu 5

1 Pakuti tinayelesewa na chikhulupililo,Tilinawo mtendere mwa Mulungu kupitila mwa Yesu Christu. 2 Kupitila mulieve tilinadanga kupitila muchikhulupililo,muchisomo chake tiimilila.Tisangalala na chisimikizo Mulungu atipasa chasogolo,Chisimikizo chakuti tizagabana mu ulemelelo wa Mulungu. 3 Osati chabe ichi,koma tisangalala futi mumasauso yathu. 4 Tiziba kuti masauso yabala kupilila,Kupilila kubala kuvomelezewa,ndipo kuvomelezewa kubala chisimikizo cha sogolo lathu. 5 Ichi chisimikizo sichitaisa mtima,chifukwa chikondi cha Mulungu chathiliwa mumitima yathu kupitila mu Muzimu Oyera,wamene anapasiwa kuli ise. 6 Chifukwa pamene tenze tikali ofoka,panthawi yake Yesu anafela banthu osalungama. 7 Pakuti nichovuta kuti umozi afele olungama. Ndiye kuti kapena munthu angafune kufela munthu wabwino. 8 Koma Mulungu aonesela chikondi chake kwa ise, chifukwa pamene tenze tikali ochimwa,Yesu anatifela ise. 9 Kwambiri manje,lomba chifukwa tinalungamisiwa na mwazi wake. 10 Pakuti ngati pamene tenze tikali badani,tinalungamisiwa kwa Mulungu kupitila mu infa ya mwana wake,kupitililapo,pamene talungamisiwa kwa Mulungu,tipulumusiwa na umoyo wake. 11 Osati chabe ichi,koma tisangalala futi mwa Mulungu kupitila muli mbuye wathu Yesu Christu, wamene kupitila mwa eve talandila kulungamisiwa kwa Mulungu. 12 Kotelo manje,kupitila mu munthu umozi chimo inangena muzioko lapansi,munjila yamene iyi infa inangena kupitila mu chimo.Ndipo infa inasefukila ku banthu onse,chifukwa onse anachimwa. 13 Pakuti kufikila pamene lamulo,chimo inali muziko,pakuti palibe kubelengewa kwa chimo ngati palibe lamulo. 14 Kotelonso,infa inalamulila kuchokela kwa Abram kufikila kwa Mose,ngakhale pali baja bamene sibanachimwe kulingana na kusamnvela kwa Adam,wamene alichoonelako cha uyo wamene abwela. 15 Olo kuti vili telo, mphaso siili monga chimo.Koma ngati kupitila muchimo ya munthu omozi,bambili banafa,chisomo cha mulungu chinachita kwambili kupitila na mphaso na chisomo cha munthu umozi,Yesu Christu,vipaka kuli bambili. 16 Pakuti mphaso siili monga vochoka muli munthu ochimwa.Chifukwa munjila imozi,chiweluzo chakususiwa chinabwela kamba ka chimo ya munthu umozi.Munjila inangu,mphaso yochokela mukulungamisiwa inabwela pamene bambili banachimwa. 17 Pakuti ngati kupitila mumachimo ya banthu umozi,infa inalamulila kupitila mu umozi,kwambili futi baja bamene balandila chisomo chambili,na mphaso ya chiyelo izalamulila kupitila mu omuyo waumozi,Yesu Christu. 18 Apa manje kupitila muchimo imozi,Banthu onse anasusiwa,motelonso kupitila mumachitidwe ya chiyelo,kunakhala kulungamisiwa kwa umoyo wa banthu bonse. 19 Kupitila mukusamnvela kwa munthu umozi,bambili banankhala ochimwa,futi kupitila mukumnvela kwa umozi bambili bapangiwa oyela. 20 Koma lamulo inangemo,kuchitila kuti chimo ipake. Koma chimo inapaka, chisomo chinapakilako. 21 Ichi chinachitika kuti mwamene chimo inalamulila mu infa, momwemonso chisomo chikalamulile kupitila mu chiyelo ku umoyo osatha kupitila mwa Yesu Christ mbuye wathu.