Mutu 4

1 Manje tizakamba chani kuti Abram,atate wathu mwa thupi anapeza? 2 Ndaba ngati Abram analungamisiwa nazitchito,asembe alinayo danga yotumbama,koma osati kutumbama mwa Yesu. 3 Chifukwa malemba akamba chani? Abram anakhulupilila Mulungu ndipo chinapasiwa kwa eve chiyelo. 4 Manje kuli wamene asebenza,malipilo yake sichaulele,koma chamene chilichake. 5 Koma kuli wamene sasebenza koma akhulupilila muli wamene alungamisa osalungama,chikhulupililo chake chiyesewa chiyelo. 6 David naye anakamba daliso kuli muntu wamene Mulungu aona oyera kopanda zintchito. 7 Anakamba kuti odalisika nibaja bamene mphulupulu zao zinakhululukiwa,amene machimo yao yanaphimbiwa. 8 Odalisika niwuja munthu wamene Mulungu sazabelengela machimo yao. 9 Manje nishi iyi nidaliso yokambiwa chabe kuli baja bamene niwodulidwa,olo ili nakuliosadulidwa?Pakuti tikamba kuti chikhulupilio chinabelengewa kwa Abram ngati chiyero. 10 Manje chinabelengewa bwanji?pamene Abram anze mumudulidwe,kapena pamene akalibe kudulidwa?Sichinali Mmudulidwe koma mukusadulidwa. 11 Abram analandila chiwoneselo cha mudulidwe.Ichi chenze chisimikizilo chachiyelo cha chikhulupililo chamene anali nacho kudala pamene sanali mumudulidwe.Chochoka muchiwoneselo ichi chinali chakuti anankhala tate wa onse amene anakhulupilila,olo kuti siwodulidwa. 12 Ichi chitanthauza kuti chiyelo chinabelengewa kwa beve.Ichi futi chitanthauza Abram anankhala tate wa baja wodulidwa osati chabe kuli baja wodulidwa koma nakuli baja wolondola ndondomeko za chikhululupilo cha atate wathu Abram akalibe kudulidwa. 13 Pakuti lonjezo kuti Abram nakuli mubadwo wake wamene unafanika kulobela ziko lapansi,sinabwele kamba ka lamulo kupitila muchiyelo cha chikhululupililo. 14 Ndaba ngati baja bamene bankhala na lamulo bangakhale oloba,nisnhi chikhulupililo chilichabe,ndipo lonjezo ilibe phindu. 15 Chifukwa lamulo ileta mkwiyo,koma pamene palibe lamulo,palibe kuchimwa. 16 Mwaichi nimwa chikhulupililo,kuti lonjezo ikapumulile pa chisomo,nakuti ikasimikiziwe kuli mubadwo wa Abram, osati chabe baja bali pansi palamulo koma nakuli bamene bagabana muchikhulupililo cha Abram. Ni tate wa ise tonse. 17 Monga mwamene nicholembedwa kuti'Nakupanga kunkala tate wamaziko yambili. Abram anali pamenso pa uyo wamene anakhulupilila, Mulungu, wamene apasa moyo kuli bakufa nakuitana vinthu vamene sivilipo monga vilipo kunkhalapo. 18 Kuchoselako vonse vamaonekedwe yakunja,Abram anakhulupilila Mulungu nachisimikizo cha msogolo.Ndipo anakhala tate wama ziko yambili,kulingana navamene vinakambika,Uzakhala mutundu wako. 19 Sanafoke muchikhulupililo.Abram anamnvesesa kuti thupi yake sinali kukwanisa kukhala na bana(Chifukwa anali nazaka makhumi khumi)Anazindikila futi kuti sara naye nalingakwanise kubala bana. 20 Koma kamba ka lonjezo ya Mulungu,Abram sananyalanyaze mukusamukhulupilila,koma anapasiwa mphamnvu muchikhulupililo nakumuyamika Mulungu. 21 Anakhala nacho chisimikizo kuti wamene analonjeza,analinso nayo mphamnvu yofikilisa. 22 Motelo naichi chinabelengewa kwa eve monga chiyelo. 23 Manje sichinalembeke kuti chikaphindulile eve eka, kuti chinabelengeka kwa eve. 24 Chinalembeka futi kwa ise, kwa eve amene chizabelengeka,ise amene tikhulupilila mwa eve wamene anaukisa Yesu mbuye wathu kwa akufa. 25 Uyu ndiye wamene anapelekewa kamba ka mphulupulu zathu ndipo anaukisiwa kutilungamisa ise.