Mutu 10

1 Abele kufuna kufuna kwa mtima wanga na pempho kwa Mulungu pali beve, chipulumuso chao. 2 Pakuti nipelekela umboni kuti banchilakolako cha Mulungu,koma osati kulingana na kuziba. 3 Pakuti sibaziba chiyelo cha Mulungu,koma bafuna kukhazikisa chiyelo chao. Sibanazipeleke kuchiyelo cha Mulungu. 4 Pakuti Yesu nichikwanisilo cha lamulo ya chiyelo,kwa aliyense okhulupilila. 5 Chifukwa Mose analemba pa chiyelo chamene chichokela ku lamulo. Munthu wamene achita chiyelo cha lamulo azankhala na chiyelo ichi. 6 koma chiyelo chamene chichokela ku chikhulupililo chikamba ichi'' Osakamba mumtima wanu,' ndani azayenda kumwamba?' (wamene azabwelesa Christu) 7 ndipo osakamba kuti nindani azapita kumanda (wamene azabwelesa Yesu ku akufa) 8 Koma chikamba chani? Mau yali pafupi na imwe, mkamwa mwanu namu mtima mwanu. 9 Ndiye mau ya chikhulupililo yamene tilalikila. Koma ngati nakamwa kanu muzasimikizila kuti Yesu nimfumu nakukhulupilila mumitima yanu kuti Mulungu anamuukisa ku akufa, muzapulumusidwa. 10 Pakuti namutima munthu akhulupilila kuchiyelo, nakamwa kake asimikizila ku chipulumuso. 11 Pakuti malemba yakamba kuti, Aliyense wamene akhulupilila mwa eve sazachitiwa manyazi. 12 Pakuti palibe kusiyana pakti pa Myuda nai mu Giliki.Pakuti mbuye umozi ndi mbuye pa onse, Ndipo niwolemela kwa onse. 13 Pakut onse oitanila pali eve azapulumusiwa. 14 Manje bangaitanile bwanji pali wamene sibanakhulupilile? Bazakhulupilila bwanji wamene sibanamnvelepo? Bazamnvela bwanji ngati palibe mlaliki? 15 Ndipo bazalalikila bwanji ngati sibanatumiwe?Monga mwamene nicholembewa, Okoma nimendo yabaja bamene banyamula mau yauthenga wabwino. 16 Koma siwonse anamnvela uthenga,Pakuti Esaya akuti, Mbuye nindani anakhulupilil uthenga wahtu? 17 Kotelo chikhulupililo chibwela nakumnvela ,ndipo kumnvela mau ya Christu Yesu. 18 Koma nikamba,nanga sibanamnvele?inde makamaka,Mau yao yapita muziko lonse lapansi,na mau yao kumalekezelo onse aziko. 19 Kupitililapo nikamba, Israeli sanamnvele?Choyamba Mose akamba kuti 'Nizakuyambani kunjilu' kuwame siziko, Kupitila muziko yosamnvesa, nizaleta kavundula ku mkwiyo. 20 Esaya anali nachisimikizo pakukamba kuti, Ninapezeka nabaja bamene sibananifune. Ninaonekela kuli baja bamene sibananifunse. 21 Koma kwa Isreaeli akuti, siku yonse ninapeleka manja yanga ku banthu osamnvela nakuyuma mtima.