Mutu 132

1 Nyimbo yokwela. Yehova, chifukwa cha Davide, kumbukilani masauso yake yonse. 2 Kumbukilani mwamene analumbilila Yehova, mwamene analumbilila Wamphamvu wa Yakobo. 3 Anakamba kuti , “Sinizangena muchi hema cha munyumba mwanga, kapena kulowa pabedi yanga, 4 sinizapasa manso yanga tulo kapena mpumulo ku zikope zanga 5 mpaka nikapeze malo ya Yehova, chihema cha Wamphamvu wa Yakobo.'' 6 Onani, tinamvela ku Efrata; tinaupeza muminda ya Yaari. 7 Tizalowa muchihema cha Mulungu; tizalambila pa chopondapo pamendo yake. 8 Nyamukani, Yehova, ku mpumulo wanu, Imwe na likasa ya mphamvu yanu! 9 Bansembe banu bavale ungwilo; okhulupilika banu akambe mokondwela. 10 Chifukwa cha Davide mutumiki wanu , musapatuke kuli wozozedwa wanu mfumu. 11 Yehova analumbilia Davide na lumbilo losimikizilika kuti sazabweza eve : “Nizaika umozi wa mbadwo wako pamupando wako wachifumu. 12 Ngati bana bako basunga chipangano changa na malamulo yamene nizabaphunzisa, bana bonse bazankhala pamupando wako wachifumu wamuyayaya.” 13 Zoona Yehova wasanka Ziyoni , ndipo wamufuna kuti unkhale mupando wake. 14 “Apa ni malo yanga yopumulilamo mpaka muyayaya. Ndipo nizankhala pano, chifukwa nimamufuna . 15 Nizamudalisa kwambili na chakudya. nizakhutisa bosauka bake na buledi. 16 Bansembe bake nizabavalika chipulumuso, okhulupilika bake azafuula mokondwela . 17 Kwamene uko nizameresa nyanga ya Davide ndipo nizamuyashila nyali wozozedwa wanga. 18 Adani bake nizabavalika manyazi, koma korona wake izawala pali iye.