1 Mumwezi wa Nisani, mumwaka wa twenti wa Artaxerxes mfumu, anasanka vinyu, ndipo ninatenga vinyu nakupasa mfumu. Manje sininakalepo wachisoni pamenso pake. 2 Koma mfumu anakamba kuti kuli Ine, "Nichani pachisoni pamenso pako? suwoneka monga wodwala. Ichi nichisoni chakumutima." Ndipo nannkala na manta maningi. 3 Ninakamba kuti kuli mfumu, "mfumu inkale kwamu yayaya! Sikuzankalila wachisoni bwanji pamenso panga? muzinda, malo ya manda ya batate banga, yagora ma mawonongeka, nazipata za wonegeka na mulilo." 4 Ndipo mfumu anakamba kuti kuli ine, "Nichani chamene ufuna kuti nichite?" Ndipo nina pempela kuli Mulungu waku mwamba. 5 Ninayanka kuli mfumu, "ngati chiwoneka mushe kuli mfumu, ndipo ngati kapolo wanu achita zamushe pamenso panu, munganitume kuli Yuda, kumuzinda wa manda batate banga, chakuti nika yimange nafuti. 6 Mfumu ananiyanka (ndipo mfumu mukazi analikale pambali pake), "Uzankala kutali bwanji ndipo azabwelela liti?" mfumu anakondwela kunituma pamene ninamupasa ntawi yoikika. 7 Ndiponso ninakamba kuti kuli mfumu, "ngati nichokondwelesa kuli mfumu, nipsaiwe nkalata yaba kazembe bamu chigawo chopitilia mumana chakuti bakanivomelese kuti nipite muma madera yawo pamene niyenda kuli Yuda. 8 Kunkala nafuta na nkalata ya Asafiwosunga kalango yamfumu, chakuti anganipase mataba yopangila ma mataba ya linga pansongolo pa tempele naku koma yamuzinda, nayamunyumba mwanene ninkala." Ndipo chifukwa kwanja kwamushe kwa Mulungu kunali pali ine, mfumu ananipasa zamene nina pempa. 9 Nina bwela kuli Kazembe mu chigawo chopitilila mumana nakumupasa nkalata yamfumu. Manje mfumu enze ananitumana olamulila gulu langondo nabokwela pama ichi. 10 Pamene Sanbalate waku Holomayiti na Tobiya waku Amonayiti kapolo anavela, sibana kondwele maningi kuti winangu anabwela wamene enzo sakila tandizo kubantu ba Isilayeli. 11 Nina bwela ku Yelusalema ndipo ninankala kwa masiku yatatu. 12 Ninanyamuka usiku, Ine nabamuna bang'ono. Siniwuze ulionse zamene Mulungu enze anafaka mumutima wanga kuti nichitile Yelusalemu. Kunalibe vinyama kuchoselako yamene nenze ninankwela. 13 Nina yenda panja usiku kupila kuchipata chachigwa, kupila ku chinsime cha nkandwe naku chipata cha ndowe, nakuyenda koma ya Yelusalemu, yamene inali yowonongeka nakuseguliwa, ndipo zipata zamitingo zina wonogewa namulilo. 14 Ndipo nina yenda kuchipata cha kasupa naku ziwe ya mfumu. Malo yanalu yang'ono kutizinyama nezeninankwela zipite. 15 Choncho ninayenda panja usiku kupila ku chigwa nakuyendela koma, ndipo ninabwelela nakungenela kuchipata cha chigwa, ndipo nina bwelela. 16 Wolamulila sibana zibe kwamene neze nina yenda nangu zamene nina chita, nenze nikalibe kubazibisa ba Yuda, nangu ansembe, nangu olemekezeka, nangu bolamulila, nangu ponse banachita chinto. 17 Ninakamba kuti kuli benve, "mwayawina mavuti yamene tilimo, mwamene Yelusalemu agona mowonogeka nazipata za wononogeka namulilo. Bwelani, tiyeni tiamnge koma ya Yelusalemu. Ndipo sitizanka nafuta mulichamanyazi." 18 Nina bauza kuti zanja la mushe la Mulungu wanga inali pali ine ndipo namwau yamene mfumu ananiwiza. babakmba kuti, "Tiyene tinyamuke nakumanaga." Ndipi bana limbisa manja yawo nchtio yamushe. 19 Koma pamene Sanbalate mu Horomiyiti, na Tobiya Kapolo wa Amonayity, na Geshemu mu Arabiyoni banavwela, bana nyoza nakutilangiza nyoza, nakukamba kuti, "Muchita chani? Muli kuwikira mfumu?" 20 Ndipo ninabayanka, "Mulungu wakumwamba azatipasa pambanisa. Ndise bakapolo bake ndipo tiza nyamuka naku manga. Koma mulibe gawo, mulbe ufulu, mulibe mbili yakale mu Yelusalemu.