Mutu 4

1 Nafuti anayamba kuphunzitsa mumbali ya chimana. Ndipo anthu ambiri anaza kwa iye, ndipo anasika mu boti inali pachimana, nakhala pansi. Anthu wonse anali kumbali kwa chimana. 2 Anabaphunzisa zinthu zambiri mumafanizo, ndipo anati kwawo muciphunzinso, 3 Mvelani, mlimi anayenda kukafesa mbeu zake. 4 Pamene analikubyala, mbeu zina zinagwela munjila, mbalame zinabwela nakudya mbeu. 5 Mbeu zina zinagwela pamwala, panalibe doti yambili. Nthawi yamene zinangomela, cifukwa mizyu siinayende kwambili pansi pa doti. 6 Koma pamene zuwa inacoka, zinapya, cifukwa zinalibe mizyu zinayuma. 7 Mbeu zina zinagwela mitengo ya minga. Mitengo ya minga inakula ndipo mbeu inalasidwa, ndipo siinabale mbeu iliyonse. 8 Mbeu zina zinagwela panthaka yabwino ndipo zinabala zipaso pamene zinali kukula ndikuculuka, zina zinabala makumi yatatu (30), zina makumi asanu ndi imodzi (60), ndi zina makumi kumi (100)." 9 Ndipo anati, "uyo ali ndimakutu omvela, amve!" 10 11 12 Pamene Yesu anali yeka, iwo amene anali naye pafupi ndi iye ndi aja twelufu anamufunsa iye za fanizo. Ndipo anati kwawo, "kuli imwezapasidwa zisinsi za ufumu wa Mlungu. Koma kwa iwo ali kunja zonse zili mumafanizilo, kuti pamene apenya, inde azapenya, koma sazaona, ndipo pamene azamva, inde zamva, koma sazamvesa, kuti angabwelele kuli Mlungu ndikubakhululukila macimo yawo." 13 Ndipo anati kwa iwo, "Simvesesa fanizo iyi? Muzamvesesa bwanji mafanizo yena? 14 Mlimi amaene anafesa mbeu yake ndiye amane afesa mau. 15 Zina zimene zinagwela mbali mwa njila, mwamene mau anagwela. Ndi pamene amvela mau, Satana panthawi yamene iyo amabwela ndikutenga mau amene anafesedwa mwa iwo. 16 Ndi zina zimene zinafesedwa pa mwala, ndi iwo amene amamva mau, nthawi yamene amalalikidwa mau amalandila ndi chimwemwe. 17 Ndipo alibe mizu mwa iwo, koma amalimbikila kwa kathawi kocepa. Pamene akumana ndi mabvuto kapena abanzunza cifukwa ca mau nthawi yamene ija amagwa. 18 19 Ndipo zina zamene zinagwela pa minga. Amamva mau, 19 koma nkhawa ya zamudziko, chinyengo ca vya cuma, cilakolako ca vinthu vina cimabangena, cimaononga mau, ndipo amankhala opanda cipatso. 20 Ndipo zina zinja zamene zinafesedwa pa nthaka yabwino. Iwo amamva mau ndikulandila ndikubala zipatso; zina makumi yatatu(30) ndi zina makumi asanu ndi imozi(60) ndi zina makumi kumi (100) 21 Yesu anati kwa iwo, "Kodi mungabwelese nyali mukati mu nyumba naku iika pansi pa basiketi kapena pansi pa bedi? Muzaileta mukati naku iika poika nyali. 22 Chifukwa kulibe chamene nichobisika chamene sichizazibika, ndiponso kulibe chamene chili chosazibika chamene sichizabwela po-onekela. 23 Ngati wina ali onse ali na matu yomvelela, lekani amvele!" 24 Anati kwa iwo, "Ikankhoni nzeru pa zimene mumvela, cifukwa ndimpimo wamene mupimilamo, azasebenzesya mupimo wamene uyo uzapasidwa kwanu. 25 Cifukwa aliwonse amene alinavo, kuli yeve zizapasidwa zambiri, ndi kuli uyo alibe , zizapokedwa cukanga zimene alinazo." 26 Ndipo anati, "Ufumu Pamene wa Mlungu uli ngati munthu amene anafesa mbeu yake pansi. 27 Pamene anagona usiku pamene anauka mmawa, mbeu inayamba kumela ndikukula, cukanga iye sanazibe zimene zinacitika. 28 Nthaka inayamba kubeleka zipatso: poyamba mpunga, pavuli pake mbeu. 29 Pamene inapya mumela nthawi yamene iyo anatuma bavikwakwa, cifukwa nthawi yokolola inafika." 30 Ndipo anati, "Tizayelekeza ndiciyani ufumu wa Mlungu, kapena ndifanizo yabwanji yamene tizasebezesha kukamba? 31 uli ngati kambeu kampiru, kapene kanafesedwa, ndikang'ono kwambiri pambeu zonse pa dziko lapansi. 32 Koma pamene kafesedwa, ndikukula kamakala kakulu kupambana cimutemgo cilicose ca mdimba, ndipo kamankhala ndi misambo zikulu, ndipo mbalame zamumulenga-lenga zimabwela ndikumanga visa mucifule cake." 33 Ndi mafanizo yambili yotelo anakamba mau kwa iwo, monga mwamene anamvesesa, 34 ndipo sanakambepo ciliconse kosasebenzesha fanizo, koma pamene anali yeka, anafotokoza zonse kwa wophunzila ake. 35 Pa siku ija, pamene kunali mumazulo, anati kwa iwo, "Tiyeni kusidya ina," 36 Ndipo anasiya anthu ambiri, anayenda pamodzi ndi Yesu, cifukwa anali kale muboti. Ndipo maboti yena anali naye. 37 Ndipo cimphepo cikulu cinanyamuka mu boti, ndipo boti inazula kwambiri cifukwa ca mawevu. 38 Koma Yesu iye anali pansi pa boti atagona pa kushoni. Ndipo anamuuusha nati, "Mphunzisi, kodi simusamalila kuti tili kufa?" 39 Ndipo, anauka, ndikuzuzula cimphepo cija nati kucimana, "Mtendele, nkala cete." Ndipo mphepo ija inaleka, ndipo kunali cete. 40 Ndipo anabafunsa iwo, "Kodi ndiciyani munacita mantha? Kufikila tsopano mulibe cikhulupirilo?" 41 Anali ndi mantha yakulu ndipo anati kwa wina ndi mzace, " Nidani uyu, cukanga cimphepo na cimana cimumvelela iye?"