Mutu 12
1
Pa siku ija muzaka kamba, '' Nizakapasa kuyamika kuli iwe, Yehova. Olo unali okalipa naine, kukalipa kwako kwapindamuka, ndipo wanitontoza ine.
2
Onani, mulungu ndiye chipulumuso changa; nizakulupilila siniza yopa, chifukwa Yehova, inde, Yehova ndiye mpanvu zanga na nyimbo yanga. Ankala chipulumuso changa.''
3
Ndi chisangalalo mudzatunga madzi ku zitsime za chipulumutso.
4
Tsiku lomwelo mudzati, Yamikani Yehova, ndipo itanani pa dzina lake; lengezani zochita zake mwa mitundu ya anthu, lalikirani kuti dzina lake lakwezedwa.
5
Imbirani Yehova, chifukwa wachita zinthu zazikulu; izi zidziwike padziko lonse lapansi.
6
Fuulani mokweza ndi mokondwera, inu okhala m'Ziyoni, pakuti Woyera wa Israyeli ali pakati panu.