Mutu 4

1 Mose anayanka, nanga ngati sibazani kulupilila olo kunimvelela koma benve kukamba, Yehova sana onekela kuli iwe?" 2 Yehova anakamba kuli enve, nichani chili mu manja mwako? Mose anakamba," nkoli." 3 Yehova anakamba kuti, "Iponye pansi." Mose anaiponya pansi, naku sanduka njoka. Mose anatabila kumbuyo. 4 Yehova anakamba kuli Mose Kuti, "Tambusula kwanja uyigwile kumuchila." Chakuti anatambulusa nakuyigwila njoka. Inankala futi nkoli mumanja mwake. 5 "Ivi vili chakuti ba kulupilile kuti Yehova, Mulungu wa makolo yao, Mulungu wa Abrahamu, Isaki ndi Mulungu wa Yakobo aonekela kuli iwe." 6 Yehova anakamba kuli enve, "Manje apa faka kwanja yako mu chovala chako, "Ndipo Mose anaika kwanja kwake mu chovala futi." Pamene anaichosa, onani, kwanja kwake kunali namakate yoyela monga matalala. 7 Yehova ankamba kuti, "faka kwanja yako mu chovala futi, "Ndipo Mose anaika kwanja yake mu chovala futi." Pamene anaichosa, anaona kuti ya nkala bwino futi, monga tup yonse. 8 Yehova anakamba kuti, "ngati sibana kulupilile iwe-ngati sibanaku fakeko nzelu kuchi zindikilo choyamba champamvu zanga olo ku kulupilila pamene apo bazakulupilila chachibili. 9 Ngati sibazakulupilila ngakale ivi vizindikilo vibili va mpamvu, olo kumvela kuli iwe, pamene apo tenga manzi ya mumana nakutatila pa doti yoyuma. ,anzi yamene uzatenga yaza sanduka magazi pa doti yoyuma. 10 Pamene Mose anakamba kuli Yehova kuti, "Ambuye" nikalibe kukambapo bwino, kapena kudala olo kapena mwamene muna kambilapo nayenve kapolo wanu ndine wachibwibwi na lulimi yanga niyolem." 11 Yehova anakamba kuli enve, nindani anapanga kamwa yamuntu? Nindani anapanga mu tu kuti asakambe olo asakame olo ayangane olo aleke kuyangana? kodi sindine, Yehova? 12 Manje yenda, nizankala na kamwa kako na ku kupunzisa vamene ufunika kukamba." 13 Koma Mose anakamba, "Ambuye, napapata tumani alionse wamene mu ngafune kutuma." 14 Koma Yehova anakalipa na Mose. Anakamba, "Nanga Aroni, mubale wako, mu Levi? Niziba kutianga kambe bwino. Komanso, abwela kukumana naiwe, ndipo akaona iwe, aza kondwela mumutima mwake. 15 Uzakamba nayenve nakufakamo mau yokama mukamwa mwake. Ine nizankala na kamwa kako na kamwa kake, ndipo niza kuonesani mose vochita. 16 Ndiye azaku kambilako kuli bantu. Azankala kamwa kako. Ndipo uzankala kuli enve monga ine, Mulungu. 17 Uzatenga mumanja mwako nkoli iyi. Nayenve uzachita zizindikilo." 18 Pamene apo Mose anabwelela kuli mupongozi wake Yetelo naku kamba naye. "Nilekeni niyende nibwelele kuli babululu banga bali ku Iguputo nione ngati bakali namoyo." Yetelo anakamba kuli kuti, "Yenda mu mutendele." 19 Yehova anakmba kuli MOse mu Mdiyani, "Yenda, bwelela ku Iguputo, chifukwa bonse bantu benze kufuna kutenga moyo wake banafa." 20 Mose anatenga bakzi bake na bana bake na kubaika pa bulu. bwelela kuziko la Iguptuo, ndipo ananyamula nkoli ya Mulungu mumanja mwake. 21 Yehova anakamba kuli MOse kuti, "Pamene uzabwelela ku Iguputo, ona kuti uchite pamenso ya Farao vonse vodabwisa vamene baika mu mpamvu zako. KOma nizza kosesa mutima wake, ndipo sazaleka bantu bayende. 22 Ufunika kukamba kuli Farao, 'Ivi ndiye vamene Yehova akamba: Isilayeli ni mwana wanga mwamuna, mwana wanga oyamba. 23 ndipo nikamba kuli iwe, "Leka mwana wanga mwamuna ayende, chakuti akaniyamike." Koma chifukwa wakana kumuleka kuti ayende, ni zapaya mwana wako, mwana oyamba wako mwamuna." 24 Manje munjila, pamene banaimilila usiku, Yehova anakumana Mose nakuyesa kumupaya. 25 Koma Zipola anatenga mupeni wamwala na kujuba nyama ya mwana wake mwamuna, naku igwilisa kumendo yake. Nakukamba, "Zo'ona iwe ndiwe mukwati wanga wamagazi kuli ine." 26 Pamene apo anamulekelela eka. Anakamba, ndimwe mukwati wanga wama magazi chifukwa chamudulidwe. 27 Yeho a anakmba kuli Aroni, "Yenda muchipululu uka kumane na MOse." Aroni anayenda, anakumana naye palupili ya Mulungu, na kumu pyopyonta. 28 Mose anauza Aro i mau yonse ya Yehova yamene anamutuma kukamba pali zizindikilo za mpamvu zamene anamula mulila enve kuchita. 29 Pamene apo Mose na Aroni banayenda nakuika pamozi bakulu bonse bamu Isilayeli. 30 Aroni anakamba mauyonse yamene Yehova anakmba kuli MOse. Anaoselanso zizindikilo va mpamvu ya Yehova mu muenso ya bantu. Bantu bana kulupilila. 31 Pamene bana mvela kuti Yehova ayangana ba Isilayeli na kuona kutitiliza kwao, pamene benve banagwada pansi naku muyamika.