1 Ninati mumutima mwanga, "manje bwela, nizakuyesa na chisangalalo. Sangalalani nazo." Koma onani, ivi vonse vilibe tandauzo. 2 Ninakamba pa kuseka, "Nizosokonezeka," ndiponso zosangalasa, "Nganga zingatandize chani?" 3 Ninazifunsa mumutima mwanga mwamene ningakwanilisile zokumbila zanga ndi vinyu. Ninavomeleza maganizo yanga yanisogolele na nzelu ngakhale ninagwililila ku zopusa. Ninali kufuna kuziba zamene zili zabwino kuti bana babanthu bazichita paziko lapansi mumasiku ya umoyo wawo. 4 Ninakwanilitsa vinthu vikulu. Ninazimangia nyumba zanga nakuzilimila minda yamphesa. 5 Ninazipangila minda yamaluba na mapaki, na kubyala mitengo ya vipaso vamitundumitundu. 6 Ninapanga visime vamanzi votilila nkhalango mwamene mumamela mitengo. 7 Ndinagula bakapolo bamuna na bakapolo bakazi; Ninali na bakapolo banabadwila munyumba yanga yaufumu. Ninalinso na ng'ombe zobeta zambili, na zobeta zambili, kupambana mafumu yonse yamene yanalamulila ine nikalibe kunkala mu Yerusalemu. 8 Ninazipezela siliva na golide, na chuma cha mafumu na zigawo. Ninatenga oyimba, bamuna na bakazi, na bazikazi bambili, chisangalalo cha bana babanthu. 9 Ndipo ninankhala wolemela na wachuma kuchila bonse banakhala mu Yerusalemu nikalibe kubadwa, na nzelu zanga zinasalilila muli ine. 10 Chilichonse chamene menso yanga yanafuna, sininavisiye. Sininayumise mutima wanga chisangalalo chilichonse, chifukwa mutima wanga unakondwela na nchito zanga zonse na chisangalalo chinali mphotho yanga panchito zanga zonse. 11 Mwaichi ninayang'ana pa zonse nchito zonse zamene manja yanga yanachita, na nchito zamene ninagwila, koma futi, vonse vinalibe pindu-monga chabe kutamangisa mpepo. Panalibe pindu paziko lapansi. 12 Pamenepo ndinatembenuka kuti nione nzelu, na misala, na usilu. Kodi munthu wina wamene azankala mfumu wosatila angachite chani kupambana zamene mfumu inachita kale? 13 Mwaichi ninayamba kuziba kuti nzelu zili na phindu kuchila kupusa, monga mwamene kuunika kuli bwino kuchila mudima. 14 Munthu wanzelu amagwilisa nchito menso yake pamutu kuti aone kwamwene ayenda, koma wopusa amayenda mumudima, ngankale aziba kuti zamene niziba kuti zochitika kuli bonse. 15 Ndipo ninakamba mumutima mwanga, "Chamene chimachitika ku opusa, chizachitika kuli ine. Nanga vimasiyana bwanji nikankhala wanzelu kwambili?" Ninamaliza mumutima mwanga, "Nazamene izi zilibe matantauzo." 16 Pakuti wanzelu munthu, monga wopusa, samakumbukiliwa ku nthawi yayitali. Mumasiku yobwela vonse vizaibalika. Munthu wanzelu amafa monga mwamene amafela wopusa. 17 Mwaichi ninanyasidwa na umoyo chifukwa nchito zilizonse paziko lapansi zinali zoipa kwa ine. Ichi nichifukwa chakuti vonse vinalibe pindu-monga kutamangisa mphepo. 18 Ninazonda nchito zanga zonse zamene ninagwila paziko lapansi chifukwa nifunika kuzisiya ku munthu wamene abwela pambuyo panga. 19 Pakuti nindani wamene aziba ngati azankhala wanzelu kapena wopusa? Koma iye azankhala wolamulila vinthu vonse paziko lapansi kuti nchito zanga na nzelu zanga zamanga. Navamene ivi vilibe pindu. 20 Chifukwa chake mutima wanga unayamba kusila nzelu pa nchito zonse ninachita paziko lapansi. 21 Pakuti pafunika kunkhala munthu winangu wamene asebenza nchito na nzelu, na kuziba, na luso, koma azasiya zonse zamene ali nazo kuli munthu wamene sanapangepo chilichonse. Naichi futi chilibe pindu — kulibe chilungamo chachikukulu. 22 Nanga munthu amapindula chani na nchito zake zonse na kunjenjemela kwa mutima wake panchito za ziko lapansi? 23 Siku ililonse nchito yake imankhala yobaba na youlemesa, ndipo usiku muzimu wake siupeza kupumula. Izi nazo zilibe pindu. 24 Palibe chinangu chabwino ku munthu kuchila kudya na kumwa, na kukuta na vabwino vamunchito yake. Ninawona kuti chazoona chimachokela mukwanja kwa Mulungu. 25 Pakuti nindani angadye kapena nindani angasangalale mumutundu ulibonse kulibe Mulungu? 26 Pakuti kuli munthu wamene amukondwelesa, Mulungu amamupasa nzelu na kuziba, na chimwemwe. Koma, amapasa wochimwa nchito yakuti asonkhanise na kusunga kuti apeleke kwa munthu wamene amakondwelesa Mulungu. Ivi vonse vilibe pindu, vii monga kutamangisa mpepo.