Mutu 1

1 Aya ndiye mau ya Mupunzisi, mubadwo wa Davide na mfumu mu Yerusalemu. 2 "Vachabechabe! Vachabechabe! Akamba Mupunzisi." Vachabechabe! Vonse niva chabechabe!" 3 "Nanga ni mpindu bwanji yamene muntu apeza kuchokela munchito zamene achita pansi pano? 4 Mubadwo winangu uyenda , mubadwo winangu ubwela, koma ziko lapansi izankala muyayaya. 5 zuba imachoka, nakungena naku tamangila kumalo kwamene imachokela. 6 Mpepo imawomba kumwera naku zunguluka kumpoto, kuyenda mozonguluka ntawi zonse munjila yake nakubwelela futi. 7 Mimana yonse imatila munyanja, koma nyanja siimazula. Kwamene misinje iyenda , nikwamene yamayenda futi. 8 Vonse vimankala volemesa , ndipo palibe wamene angavifotokoze. Linso simakutila navamene imawona, kapena kwatu kukutila navamene imanvela. 9 Mwamene chinalili ndiye mwamene chizankalila, na vonse vamene vimachitiwa ndiye vamene vizachitiwa. 10 Palibe chintu chamanje pansi pano. Nanga pali chinangu chilichonse chamene tingakambe kuti, 'Onani, ichi nichamanje'? Chilichonse chamene chinalipo chinanakhalako nthawi itali, mumibadwe yamene inabwera kale ife tisanakhaleko. 11 Palibe wamene aoneka monga angakumbukile zamene zinachitika kale, na zamene zinachitika pambuyo pake ndiponso zamene zizachitika pasogolo sizizakumbukiwa. " 12 Ine ndine Mupunzisi, ndipo nankhala nili mfumu ya Israeli mu Yerusalemu. 13 Ninasimikiza mumutima mwanga kuti nibelenge ndi kusanthula mwanzelu zonse zamene zimachitika paziko lapansi. Kusakila kwameneuko ni nchito yolemesa yamene Mulungu apeleka kuli bana ba banthu kuti bankhale otanganikwa nayo. 14 Naona nchito zonse zochitiwa pansi pano, ndipo onani, vonse vilibe kanthu, ndi mtima. 15 Zopombeka sizingapombosoke! vosoba sivingabelengedwe! 16 Nakamba na mutima wanga, nakuti, ona, napeza nzelu zikulu zopambana bonse banali mu Yerusalemu nikalibe kubadwa; mutima wanga waona nzelu zazikulu na kuziba. 17 Mwaichi ninaika mutima wanga kuti nizibe nzelu komanso misala na kupusa. Ninabwela mukuziba kuti naichi futi chinali choyesa kubeta mphepo. 18 Pakuti mu nzelu zambili muli zokhumudwisa zambili, ndipo wamene awonjezela chizibiso amachulukisa chisoni.