Mutu 9

1 Nvelani, Israele; muli pan'gono nakujumpa Yolodani lelo, kuyenda mukati na kutenga ma ziko yakulu kuchila imwe ndiponso yamphavu kuchila imwe, na mizinda yamene ili yonveka ndipo yochingiliziwa kufika kumwamba, 2 banthu wonveka ndiponso batali, bana bamuna ba Anakimu, wamene imwe muziba, ndipo uyo wamene munvela bantu kumukambapo, 'Nindani angaimilile pasogolo pa bana bamuna ba Anaki?' 3 Zibani mwaichi lelo kuti Yehova Mulungu wanu ndiye wamene ayenda pasogolo panu monga woononga mulilo; azabaononga iwo, nakugwesa beve pasogolo panu; ndipo muzabachosa beve panja na kubapanga beve kuonongeka mwamusanga, monga Yehova akambila kuli imwe. 4 Musakambe mumutima yanu, pambuyo Yehovah Mulungu wanu abawononga beve kubachosa kuchoka pasogolo panu, 'Chinali chifukwa cha kuyela kwanga chamene Yehova abwelesa ine kungwena muno na kutenga yano malo; ndiye chifukwa cha kuchimwa kwa aya ma ziko yamene Yehova ayachosa kuchoka pasogolo panu. 5 Sindicho chifukwa cha kulungama kwanu kapena kukoma mutima wanu kuti muyenda mukati na kutenga malo, koma chifukwa cha kusalungama kwa aya maziko yamene Mulungu wanu ayachosamo kuchoka basogolo panu,na kuti anga pange kubwela ya zoona mau yamene analumbila kuli makolo yanu, kuli Abrahamu, Isake, na Yakobo. 6 Muzibe sopano, kuti Yehova Mulungu wanu sakupasani imwe aya malo kuti mutenge chifukwa cha chilungamo chanu, chifukwa ndimwe banthu wosanvela. 7 Kumbukilani ndipo musaibale mwane imwe munasokoneza Yehova Mulungu wanu kukalipa muchipulu; kuchokela pa siku yamene imwe munachoka mu ziko ya Igputo mpaka imwe mubwela kuli yano malo, imwe mwankala osanvela mukusana na Yehova. 8 Napaja pa Horebu imwe munakalipisa Yehova ku ukali, ndipo Yehova anakalipa kwambili na imwe kuti akuonongeni imwe. 9 Pamene ninayenda pamwamba pa lupili mukulandila malamulo pa mwala, malamumulo ya chipangano yamene Yehova anapanga kwa imwe, ninankala pa lupili kwa kwa masiku yali fote na usiku ili fote; sininadye ngankale buledi kapena kumwa manzi. 10 Yehova ananipasa ine zolembewa zibili za mwala zolembewa na chimbombo chake; pali ivo panalembewa vilivonse monga mwamene yonse mau yamene Yehova anaulusa kuli imwe pa lupili kuchoka mukati mwa mulilo pa siku yo sonkana. 11 Chinachitika pakusila kwa masiku ayo yali fote na usiku uli fote kuti kuti Yehova ananipasa yabili volembelapo ya mwala, volembelapo va chipangano. 12 Yehova anakamba kuli ine, 'Nyamuka, yenda pansi mwamusanga kuchoka kuno, kubanthu bako, bamene munachosa ku Igputo, bazionongela beka. Bachita mwamusanga kupindamukila kumbali kuchoka munjila yamene ninalamulila iwo. Bazipangila beka chinthu.' 13 Mopililapo, Yehova anakamba naine na kuti, 'nabaona aba bathu; nibanthu bamene bali na ntonta. 14 Nisiye ine neka, kuti nibaononge beve na kuchosa zina yawo kuchoka pansi pa ziko yakumwamba, ndipo nizapanga iwe ziko yampavu ndipo yonveka kuchila beve.' 15 Ndipo ninapindamuka na kubwela pansi kulupili, ndipo lupili lunali kupya. Mapilisi yabili ya chipangano yanali mumanja yanga. 16 Ninalangana, ndipo onani, munachimwila mukususana na Jehova Mulungu wanu. Munazipangwila mweka mwana wa ng'ombe. Munapindamukila mwamusanga kumbali kuchoka mu njila yamene Yehova analamulila imwe. 17 Ninatenga mapilisi yabili na kuyataya kuchochoka mumanja mwanga. Ninayapwanya basogolo ba menso yanu. 18 Nafuti ninagona pansi pamenso pa Yehova masiku yali fote na usiku uli fote; sininadyepo ngankale buledi kapena kumwa manzi, chifukwa cha wonse uchimo wanu wamene munachita, mukuchita chija chamene chinali choipa pa menso ya Yehova, mwa kuti mumukalipise ku ukali. 19 Chifukwa ninali namanta ya ukali na kupya kosakondwela kwamene Yehova anali wokalipa kwambili mosusana naimwe kuti akuonongeni. Koma Yehova ananvela kwa ine ija ntawi futi. 20 Yehova anali wokalipa kwambili na Aaroni nafuti pali yamene ija ntawi. 21 Ninatenga uchimo wanu, mwana wa ng'ombe wamene munapanga, na kumushoka, kukamenya, na kukagaya kang'ono, mpaka kanankala monga doti. Ninataya doti yake mu mumana wamene unachokela pansi kuchoka kulupili. 22 Ku Tabera, ku Massa, na ku Kibroth Hattaava, munakalipisa Yehova to mukwiyo. 23 Pamene Yehova anakutumani imwe kuchoka ku Kadeshi Barnea na kuti, 'yendani pamwamba na kunkala nayo malo yamene ine nakupasani imwe; koma munapandukila mosusana na malamulo ya Yehova Mulungu wanu, ndiponso simunakulupilile kapena kunvela ku mau yake. 24 Imwe mwankala wopandukila mosusana na Yehova kuchoka pa siku yamene ninakuzibani. 25 Ninagona cha menso yanga pansi pasogolo pa Yehova ayo masiku fote na usiku uli fote, chifukwa anakamba nakuti azakuonongani imwe. 26 Ninapempela kwa Yehova nakuti, 'Imwe Ambuye Yehova, musaonenge banthu banu kapena cholowa chamene imwe mwachiombola kupitila mu ukulu wanu, chamene imwe mwachibwelesa kuchoka ku Igputo na kwanja kwa mpavu. 27 Itanilani kunzelu zanu bakapolo banu Abrahamu, Isaki, na Yakobo; musalangane kuyuma mutima kwa aba banthu, kapena kuipa kwawo, kapena pa uchimo wawo, 28 kuti malo kuchoka kwamene imwe munatibwelesa ife yangakambe kuti, ''Chifukwa Yehova sanali kukwanisa kuti ababwelese mu malo yamene analonjeza beve, ndipo chifukwa anabazonda, ababwelesa beve kuti abapaye beve mu chipululu.'' 29 Koma nibanthu banu ndipo choloba chanu, bamene munabwelesa kuchoka kupitila mu ukulu wa mpavu zanu na kuonesela kwa mpavu zanu.'