Mutu 8

1 Mufunika kusunga yonse malamulo yamene nikupasani imwe lelo, ndiye kuti munkale na moyo na kuchuluka, na kuyenda mukati na kutenga malo yamene Yehova Mulungu analumbila kwa batate banu. 2 Muzaitanila ku nzelu zonse njila zamene Yehova Mulungu wanu akusogolelani izi zaka zili fote muchipululu, kuti akupangeni munkale ozichepesa, kuti akuyeseni kuti azibe zamene zili mumutima wanu, ngati nizoona mungasunge malamulo kapena iyai. 3 Anakuchepesani, na kupangani imwe kunvela njala, na kukudyesani imwe ndi mana, yamene imwe simunazibe na yamene batate banu sibanaizibe. Anachita icho kuti akupangeni imwe kuziba kuti sibuledi yeka ingalengese munthu kunkala namoyo; koma, ni muli chilichonse chamene chichoka mukamwa ka Yehova kuti munthu angankale naumoyo. 4 vovala vanu sivinasile na kugwa kuchoka kuli imwe, na mendo yanu siyanavimbe muli izo zaka zili fote. 5 Muzaganiza pali ichi mumutima, bwanji, monga mwamuna apunzisa mwana wake, nayenso Yehova Mulungu apunzisa imwe. 6 Muzasunga malamulo ya Yehova Mulungu wanu, kuti muyende munjila zake na kumulemekeza iye. 7 Pakuti Yehova Mulungu wanu alikulowetsani m'dziko lokoma, dziko la mitsinje yamadzi, la akasupe, ndi akasupe oyenda m'zigwa ndi zitunda; 8 dziko la tirigu ndi barele, la mipesa, mkuyu, ndi makangaza; dziko la mitengo ya azitona ndi uchi. 9 Aya ni malo yamene simuzadya buledi mu njala ndipo simuzasoba kanthu kalikonse; malo yamene myala niyopangidwa ndi nsimbi, na kuchoka ma chulu yake mungakumbe mwala wa kopa. 10 Muzadya ndiponso muzakuta, ndipo muzadalisa Yehova Mulungu wanu pa yabwino malo yamene akupasani imwe. 11 Munkale wosamala kuona kuti simunaibale Yehova Mulungu wanu, mu kulepela kusunga malamulo na zolamulila zake na zoikika zamene nikulamulilani imwe lelo. 12 Chifukwa, mukadya ndiponso mwakuta, ndiponso mukamanga yabwino manyumba na kunkalamo, mitima yanu izanyamuka. 13 Nkalani wosamala pamene zobeta na ng'ombe zanu zikapaka ndiponso siliva na golide yanu ikachuluka, na vonse mulinavo vikachuluka, 14 ndipo mitima yanu inkala yonyamuka pamwamba na kuibala Yehova Mulungu wanu, wamene anakuchosani imwe ku ziko ya Igputo, kuchoka mu nyumba ya ukapolo. 15 Musamuibale iye wamene anakusogolelani imwe kupita mu chikulu ndipo choyofya chipululu, pamozi na zinkali njoka na sikopiyoni na malo yoyuma kwamene kunalibe manzi, wamene anakubweleselani manzi kuchoka mu mwala wokosa. 16 Anakudyesani imwe mu chipululu na mana yamene makolo banu sibanaizibe, kuti akuchepeseni imwe na kukuyesani imwe, kukuchitilani imwe zabwino pakusiliza kwake, 17 koma mungakambe mumitima yanu, 'mpavu zanga na kwampanvu kwanja kwanga kwasebenzela konse uku kulemela.' 18 Koma muzaganiza mu nzelu Yehova Mulungu wanu, chifukwa niwamene wamene akupasani imwe mpavu zotenga chuma; kuti ankazikiseni chipangano chake chamene analumbila kuli batate banu, monga chilili lelo. 19 chizachitika ngati, ngati muzaibala Yehova Mulungu wanu na kuyenda pambuyo pa inangu milungu, kuipembeza, na kuilemekeza iyo, nizachita umboni mosusana na imwe lelo kuti zoona muzaonongeka. 20 Monga ma ziko yamene Yehova ayapanga kuonongeka pasogolo panu, nanga imwe muzaonongka, chifukwa simunafune kunvela ku mau ya Yehova Mulungu wanu.