Mutu 3

1 Ndipo tinapindamuka na keyenda munjila yaku Bashani. Og, mfumu ya Bashani, anabwela na kuukila ife, iye na bonse bathu bake, kumenyana ku Edrei. 2 Yehova anati kuli ine, 'Usamuyope; chifukwa napasa iwe kupambana pali eve ndipo naika bonse bathu bake na malo yake pansi paulamulilo wako. Uzachita kuli eve monga mwamene unachitila kuli Sihoni, mfumu yaku Amori, wamene anankala ku Heshbon.' 3 Ndipo Yehova Mulungu wathu anatipasa ife kupambana pali Og mfumu yaku Bashani, na bonse banthu bake banaikidwa pansi paulamulilo wathu. Tinabamenya mpaka kunalibe umozi wa banthu bawo anasala. 4 Tinatenga yonse minzi pali ija ntawi. Kunalibe kapena umozi pa minzi ili sikisite yamene sitinatenge kuchoka kuli beve-yonse malo ya Argob, mfumu yaku Og mu Bashani. 5 Izi zonse zinali mizinda zolimba navipupa vitali, makomo, na nsimbi; izi zinali kuchoselako yambili minzi yosachingiliziwa na vipupa yamene tinatenga. 6 Tinaba onongelatu, monga tinachitila kuli Sihoni mfumu yaku Heshiboni, kuonongelatu muzinda uli onse- bamuna naba kazi na bana bang'ono. 7 Koma vibeto vonse na vintu va pindu vamu mizinda tanatenga kunkala vatu. 8 Pa ntau ija tinatenga malo kuchoka mu manja ya mfumu zibili za baku Amori, banali kusidya kwa Yodano, kuchokela ku chikwa cha Arnoni mpaka ku pili ya Hermoni 9 (pili ya Hemoni imaitaniwa kuti Sirioni nabaku Sidinia, na baku Amori bamaitana kuti Seiri) 10 na mizinda yonse yamu zigwa, Gileadi na Bashani, mpaka kufika ku Saleka na Ederei, mizinda ya ufumu wa Og ku Bashani.'' 11 (Koma kwa osalila ba Rephaim, chabe Og mfumu ya Bashani ndiye anasala. Onani! Bedi yake inali bedi ya nsimbi. Nanga sikunali ku Rabbah, kwamene wobadwa kwa Ammoni bankala? Inali naini kubiti muutali na folo kubiti muufupi, mwamene banthu bamapimila.) 12 '' Aya malo tina tenga kunkala yatu pa ntau ija- kuchokela kuli Aroa, yamene yanali ku chikwa cha Amoni, na pang'ono ku ziko yakumapili ya Gileadi, na mizinda yake-ninapasa kuli bakuli Reubeni na kuli bakuli Gadi. 13 Bosala pali ba Gileadi na bonse ba Bashani, ufumu wa Og, ninapasa kujuba pakati mutundu wa Manasse. ( Yonse malo ya Agobu, na Bashani. Malo ya mozi yaitaniwa malo ya Rafaimu. 14 Jairi, wa mubadwe wa Manasse, anatenga malo yonse ya Agobu kufikila naku malile ya baku Geshurite na Makatite. Anaitana malo, ngankale Bashani, muzina yake, Havvoti Jairi, mpaka lelo.) 15 Ninapasa Gilidi kuli Makir. 16 Kuli ba Rubenaiti na kuli ba Gadite ninapasa malo kuchoka ku chigwa chaku Arnoni-pakati pa chigwa pali malile ya malo na - ku kumumana wa Jabbok, yamene ndiye malile na wobadwa kuli Ammoni. 17 Inangu ya boda ilinso malo ya mumana wa Yodani, kuchoka ku Kinnereth kupita ku nyanja ya Araba (ija ndiye, nyanja ya muchele) mukutentemuka kwa pili ya Pisgah kumumawa. 18 Ninakuuzani pali ija ntawi, nakuti, 'Yehova Mulungu wanu akupasani aya malo kunkala yanu; imwe, bonse bamuna ba nkondo, bazapita wokonzeka pasogolo pa babale banu, banthu ba Israeli. 19 Koma bakazi banu, bana banu, na vibeto vanu ( niziba kuti muli na vibeto vambili), viznkala mumizinda yanu yamene nakupasani, 20 mpaka Yehova apase kupumula ku ba bale banu, monga achitila kuli imwe, mpaka nabeve batenge malo yamene Yehova mulungu wanu abapasa kuseli kwa Yodano; mwaicho muzbwelela, mwamuna aliyense pali imwe, kuvintu vanu vamene nakupasani.' 21 Ninauza Yoswa pali ija ntawi, nakuti, 'Yako menso yaona vonse vamene Yehova Mulungu wako achita kuli aya yabili mafumu; Yehova azachita chimozimozi kuli yonse maufumu kwamene iwe uzayenda. 22 Iwe siuzayopa beve, chifukwa Yehova Mulungu wako niwamene azakumenyela iwe.' 23 Ninamufunsa Yehova pali ija ntawi, nakuti, 24 'Imwe Ambuye Yehova, mwayamba kulangiza wanu wanchito ukulu wanu na kwanja kwanu kolimba; kodi nindani mulungu aliko kuja kumwamba kapena mu ziko lapansi wamene angachite ncito zimozi monga zamene mwachita, na machitidwe yampanvu ? 25 Lekani ine niyende kuja, nakupapatani, na kuona malo yabwino yamene yapitilila ku Yodani, ija ziko yabwino yapapili, na futi Lebanoni.' 26 Koma Yehova anali wokalipa na ine chifukwa cha imwe; Iye sananvele kuli ine. Yehova anakamba kuli ine, 'Leka ichi chinkale chokwana kwa iwe-usakambe nafuti vinangu kuli ine pali iyi nkani: 27 Yenda pamwamba pa Pisgah na kunyamula menso yako kumazulo, kumumwela, kumupoto, na kumumawa; langana na menso yako, chifukwa iwe siuzayenda kuja ku Yodani. 28 Koma, Langiza Yoswa na kumulimbisa, chifukwa azayenda basogolo pali aba bathu, ndipo azalengesa beve kuti batenge malo yamene uzaona.' 29 Ndipo tinankala mu chigwa kulanganana na Beth Peor.