Mutu 8

1 Sauli anavomelezana nayo ifa yake. So mpingo unali ku Yelusame unayamba kusausidwa kwakukulu siku yamene iyo; ndipo okhulupirila anamwazikana ponse ponse kumizinda ya Yudeya na Samaria, kucoselako ma apostozi. 2 Amuna ozipileka anamushika Stefano ndipo anamulila maningi yeve. 3 Koma Saulo ananzunza mpingo maningi; anayenda nyumba na nyumba nodosa amuna na akazi, nobafaka mu jele. 4 Koma okhulupilila amene anamwazikana anapitana-pita kulalikila mau. 5 Filipo anayenda ku tauni ya Samaria nobalalikila beve Kristu. 6 Pamene banthu bambiri banamvera nowona vizindikilo vamene Filipo anacita, banafakako nzelu pamozi kuzamene enzokamba. 7 Cikufakwa kucoka kubanthu ambili amene anali navo, mizimu yonyansa inacoka mopunda maningi; ndipo bambili ozizila nabolemala mendo anacilisiwa. 8 Ndipo mwenzeli cisangalalo cikulu mu tauni. 9 Koma mwenzeli munthu winangu mu tauni zina lake ni Simoni, wamene kumbuyo inzo citata vaufwiti; enzo badabwisa banthu baku Samaria, pamene enzo kamba kuti nimunthu ofunikila maningi. 10 Ba Samaria bonse, kucokela kumwana kufikila mukulu, enzno mufakila nzeru yeve; anakamba, "Uyu munthu ndiye ija mphambu ya Mulungu yamene iyitaniwa kuti Yaikulu." 11 Anamumvelera yeve, cifukwa cakuti anabadabwisayeve kwa nthawi kwa nthawi itali na ufwiti ake. 12 Koma pamene banakhulupila Filipo pazamene analalikila pa uthenga okamba paza ufumu wa Mulungu na zina ya Yesu Krsitu, anabatizika, amuna nabazimai nabo. 13 Ndipo Simoni nayeve anakhulupilila, anapitiliza kunkala na Filipo; pamene anabona visanzo na zocita zikulu kucitika, anadabwa. 14 Manje pamene ma apostozi banamvera kuti Samaria inalandila mau amulungu, anabatumizila Peturo na Yohane. 15 Pamene banabwela, anabapemphelera , kuti alandile Mzimu Oyela. 16 Cifukwa kufikila ija nthawi, Mzimu Oyela enze akalibe kubwela pali aliyense wa beve; benze banapatizika cabe mu zina la Ambuye Yesu. 17 Pamene apo Peturo na Yohane anafaka manja yabo pali beve, ndipo analandila Mzimu Oyela 18 Manje pamene simoni anabona kuti Mzimu Oyea wapaswa kupitila mukuikapo manja yama apostozoi, anabwela abapasa ndalama. 19 Anabwela akamba ati "Ninepaseni izi mphamvu, naine, kuti aliyense wamene nizafakaka manja yanga payeve azalandil a Mzimu Oyela." 20 Koma Peturo anakamba kwa yeve, leka siliva yako ibonongeke pamozi naiwe, cifukwa waganiza kuti ungalandile mphaso ya Mulungu nandalama. 21 Ulibe mbali pali ici, cifukwa mtimwa wako sulibwino na Mulungu. 22 Cifukwa caici tembenuka kuzoipa zako, ndipo upemphere kwa Ambuye, kuti mwina akukhululukile manganizo umumtima mwako. 23 Cifukwa nabona kuti uli mu poisoni yalukhubwa ndi maunyolo ya ucimo." 24 Simoni anayankha nokamba ati, Nipempherele kwa Ambuye, kuti visacitike kwa ine pavamene wakamba." 25 Pamene Petro na Yohane anankhala na umboni nokamba mau ya Ambuye, anabwelela ku Yelusalemu; penzo yenda munjira, analalikila uthenga ku minzi yambili ya Asamaria. 26 Manje mungelo wa Ambuye anakamba na Filipo kuti, "Nyamuka ndipo uyende kumazulo ku njila yamene icokela ku Yelusalemu kuyenda ku Gza." (Iyi njila ili mucipululu.) 27 Ananyamuka noyenda. Onani apo, kunali munthu ocokela ku Ethiopia, olemekezeka wamene anali naulamulilo ukulu kuli mafumu, mkazi wa mfumu yama Ethiopians. Ndiye enzeli osunga ndalama za mkazi wa mfumu. Enzeli anabwela ku Yelusalemu kumbela ku pembeza. 28 Enzo bwelelamo nishi wankhala mucikocikali, ndipo enzo belenga mneneri Yesaya. 29 Mzimu unakamba kuti kwa Filipo, "Yenda pafupi nokhala pafupi na cikocikali." 30 So Filipo anathamangila kuli yeve, nomumvera abalenga Yesaya mneneri, ndipo anakamba ati, "Kansi umvela vamene ubelenga?" 31 Mu Ethiopian anakamba ati, Ningamvele bwanji, koma kapena winangu anisogolele?" Anapempha Filipo kuti angene mucikocikali nonkhala nayeve. 32 Manje ndime ya mau yenzo belenga mu Ethiopian yenze iyi, "Anapelekewa ngati mberere kuyenda upaiwa; monga mwana wa mberere akhalila zii kuli uja wamene agela usako wake, sasegula pakamwa: 33 Mukumupepusa ciweluzilo cake wacicosa: azakamba zamubado wake nindani? cifukwa umoyo wake unacosewa pa ziko lapansi." 34 So uyu olemekezeka anafunsa Filipo, nokamba ati, nikupempha, nindani wamene mneneri akamba? Akamba zayeve olo munthu winangu?" 35 Filipo anayamba kukamba; anayamba na mau yali mu Yesaya kulalikila pali Yesu kuli Yeve. 36 Pamene anapitiliza kuyenda mnjila, anafika panali manzi; wolemekezeka anakamba ati, Ona pali manzi apa; cizanilesa kubatizika nicani?" 37 (Filipo anakamba ati, ngati ukhulupilila na mtima wako bonse, ungabatiziwe." Olemekezeka anakamba ati, "Nikhulupilila kuti Yesu Kristu nimwana mwamuna wa Mulungu.") 38 So mu Ethiopian analamulila kuti cikocikali kuti ci imilile. Banayenda mu manzi, bonse babili Filipo na wolemekezeka, ndipo Filipo anamubatiza yeve. 39 Pamene banacoka mu manzi, Mzimu wa Ambuye unamutenga Filipo; wolemekezeka sanauone futi, ndipo anapitiliza na ulendo wake wosangalala. 40 Koma Filipo anabonekela ku Azotasi. Anapitila ku mzinda wamene uja nolalikila uthenga kuma tauni yonse, mpaka anafika ku Sizalia.