1 Pamene rayoti inasila, Paulo anaitana ophunzila ndipo anabalimbiksa. Ndipo anabalayila noyenda ku Mesedoniya. 2 Pamene anapitila mizinda ayo nolimbikisa okhulupila maningi, anangena mu Girisi. 3 Pamene anankhalako myezi itatu kuja, kumu ukila kunapangiwa na Ayuda nishi wankhala pang'ono kuyenda ku Siliya, so anaganiza kubwelela kupitila ku Mesedoniya. 4 Kumupelekeza iye kufika ku Asia enzeli Sopata mwana mwamuna wa Filasi ocokela ku Beriya; Arisitakasi na Sekundasi, bonse ocokela kwa okhulupila waku Thesalonika; Gayesi waku Debi, Timoti' na Ticikasi na Trofimasi ocokela ku Asia. 5 Koma aba banthu banasogolako ndipo benzo tiyembekeza ku Tiraosi. 6 Tinayenda kucoka ku Filipi pambuyo pacikodwelelo ca pasaka, ndipo pamasiku yali 5 tinabwelela kwa iwo ku Tiraosi. Kuja tinankhalako masiku 7. 7 Siku yoyamba mu sabata, pamene tinakumana pamozi kti tinyemela buredi, Paulo anakamba kuli wokhulupilila. Enzo pulana kuyenda siku yokokhapo, so anapitiliza kukamba mpaka pakati pa usiku. 8 Kunali manyale yambili mucipinda capa mwamba mwamene tinakumana. 9 Pa windo panankhala Munyamata wingu zina yake Utikasi. wamene anagona maningi. Pamene Paulo anatenga nthawi itali kukamba, uyu munyamata, akali gone, anagwa kucoka pamwamba ndipo anamudoba wakufa. 10 Koma pamene Paulo anayenda pansi, Paulo anamugonela yeve, numukumbatila. Ndipo anakamba ati, osakalipa futi, cifukwa ali moyo." 11 So anayenda pamwamba futi nonyema buredi nakudya. Pamene anakamba nabeve nthawi itali nishi kufuna kucha, anayenda. 12 Anamubwelesa munyamata wa moyo ndipo anatothozidwa maningi. 13 Ise bamene tinayenda pasogolo pali Paulo na boti noyenda ku Asosi, kwamene tinaganiza kuti tiyenda nayeve Paulo. Ici ndiye camene anafuna yeve kucita, cifukwa anapulana kuyenda pansi. 14 Pamene tinakumana nayeve ku Asosi, tinamutenga mu boti ndipo tinayenda ku Mitileni. 15 Tinayenda kucoka paja nofika siku yokokhapo pafupi na pamalo ya Chiyosi. Siku yokokhapo tinafika pamalo ya Samosi, ndipo siku yokokhapo tinafika ku tauni ya Miletasi. 16 Cifukwa Paulo anagaza kuyenda kupitilila Aifenso, kuti asataye nthawi ili yonse mu Asia; cifukwa enzo thamangila ku Yelusalemu kuti apezekeko ku siku ya Pentekositi, kati cenzeli cokwanilisika kwa yeve kucita so. 17 Kucoka ku Miletasi anatuma banthu ku Aifenso ndipo anaitana akulu amu mpingo. 18 Pamene anabwela kuli yeve, anakamba ati kuli beve, kucoka siku yoyamba pamene ninangena mu Asia, mwamne lyonse nimakhalila na imwe. 19 Ninapitiliza kutumikila Ambuye mozicepesa na misozi, namasauso yamene yananicitikila ine cifukwa ca kuniteya kwa Yuda. 20 Muziba mwamene sinina nkhalile zii pakukuuzani camene cinali cofunikila, namwamene ninakuphunzisilani pagulupu nakupitamo muma nyumba. 21 Muziba mwamene ninapitiliza kucenjeza ba Yuda naba Giliki pakutembenukila kuli Mulungu na cikhulupililo mwa Ambuye Yesu. 22 Koma manje, onani, niyenda omangiwa mu Mzimu Oyela ku Yeslusalemu, siniziba zamene zizanicitikila kuja, 23 kucosako cabe kuti Mzimu Oyela amakamba naine mu tauni iliyonse nokamba ati macheni nakubvutika kuku yembekezela. 24 Koma sinibelengela kuti umoyo wanga niwabwino kwa ine, kuti nisilize nchito yanga nautumiki wamene ninalandila kucokela kwa Ambuye Yesu, kuti nipeleke umboni pali uthenga wa cisomo ca Mulungu. 25 Ndipo manje, onani, niziba kuti monse, bamene ninapitamo kulalikila za ufumu, simuzaniwona futi. 26 Cifukwa ca ici nipelekela umboni kwa imwe lero, kuti nilibe mulandu pa mwazi wamunthu aliyense. 27 Cifukwa sininankhale zii kukamba kwa imwe cifunilo conse ca Mulungu. 28 So nkhalani ozisamalila imwe mweka, na nkhosa zonse zamene Mzimu Oyela anakupanga kunkhala oyanganila. Nkhalani osamalila kucita ubusa pa mpingo wa Mulungu wamene anagula na mwazi wake. (Malemba yenangu yakamba ati, Nkhalani ocenjela kusamalila mupingo wa Mulungu wamene anagula namwazi wa mwana wake). 29 Niziba kuti ngati nacoka, mimbulu yolusa izaloba pakati panu, ndipo si izalekelela nkhosa. 30 Niziba kuti ngankhale pakati panu bamuna binangu azabwela nokamba vinthu voononga, kuti bakoke ophunzila kuli beve. 31 So nkhalani pa gadi. Kumbukilani kuti kwa zaka zitatu sininaleke kuuza aliyense wa imwe vocita namisozi usiku na muzuba. 32 Manje nikupelekani kwa Mulungu nakumau yacisomo cake, yamene yakwanisa kukumangani imwe ndiponso kukupasani colowa pakati pabonse bamene bali oyelesedwa. 33 Sininakhubwile siliva, golide kapena malaya yamunthu. 34 Imwe mweka muziba kuti mwanja yanga yananipasa zamene nezofuna nazofuna zabaja bamene nenzeli nabo. 35 Muzinthu zonse ninakupasani cisanzo mwamene mufunikila kuthandizila ofoka pakusebenza, namwamene mufunikila kukumbukila mau ya Ambuye yesu, mau yamene yeve yeka anakamba: "nikodalisika kupasa kupambana kulandila." 36 Pamene anakamba munjila yaso, anagwada pansi nopemphela nabo pamozi bonse. 37 Bonse banalila maningi nomukumbata mumkosi nomu kising'a. 38 Banamvela cifundo maka maka pazamene anakamba, kuti sazamuwonanso. Ndipo anamupelekeza ku boti.