1 Manje mpingo waku Antioku, mwenzela ma aneneri na aziphunzisi. Benzeli Banabasi, Simiyoni (oyitanidwa Niga, Lusiyasi waku Sailini, Maniyani (muzake wa Herode), na Sauli. 2 Pamene benzeli kutamanda Mulungu nosala kudya, Mzimu Oyela anakamba ati, "munipatulile Banabasi na Sauli, kuti bacite nchito yamene nabaitanila." 3 Pamene banasiliza kusala kudya, nopephela, nobafaka manja yabo pali aba bamuna, banacoka. 4 So Banabasi na Sauli banamvelera Mzimu Oyela ndipo banayenda ku Seleusia; kucoka kuja banakwela boti noyenda kumalo ya Siprasi. 5 Pamene benzeli mu tauni ya Salamisi, banalalikila mau ya Mulungu mumasinagoge ya Ayuda. Benzelinso na Yohane Mariko monga obathandiza. 6 Pamene banayenda pamala ponse pa Pafosi, anapeza wamajiki winangu, mneneri waboza Waciyuda, wamene zina lake ni Bar Yesu. 7 Uyu wamajiki anagwilizana na govana, Segiayasi Paulusi, wamene enzeli mwamuna wa nzelu. Uyu munthu anaitana Banabasi na Sauli, cifukwa enzo funa kumvera mau ya Mulungu. 8 Koma Elimasi "wamajiki" (ndiye mwamene zina lake imasulilidwa) anabasusha; anayesesa kuosa govana kucoka kucikhulupiliro. 9 Koma Saulo, wemenenso ezoitaniwa kuti Paulo, ozazidwa na Mzimu Oyela, anamuyanganisisa maningi nokamba ati, 10 "Iwe mwana wa Satana, ndiwe ozula na maboza yonse nakuipa. Ndiwe mudani paciliconse cabwino. Suzakwanisa kubendesa njila za straiti za Ambuye, kansi uzacita so? 11 Manje ona, kwanja kwa Mulungu kuli paiwe, ndipo uzankhala ulibe menso. Suzaona zuba pakanthawi." Pamene apo panagwela pali Elimasi vambuu namudima; anayamba kuyenda yenda kupempha banthu kuti bamugwile pa kwanja nomusogolela. 12 Pamene govana anawona vamene vinacitika, anakhulupilila, cifukwa anadabwa pali viphunziso pali Ambuye. 13 Manje Paulo nabazake banayenda ku Pafosi nofika ku Pega ku Pafilia. Koma Yohane anabasiya nobwelera ku Yelusalemu. 14 Paulo nabazake anayenda kucoka ku Pega noyenda ku Antioku ku Pisidiya. Kuja banayenda mumasinagoge pa Sabata ndipo anankhala pansi. 15 Pamene banabelenga lamulo naba neneri, asogoleli bamusenagoge anabatumila uthenga kukamba kuti, "Abale, ngati muli nauthenga olimbikisa aba banthu, ukambeni. 16 So Paulo ananyamuka nonyamula kwanja; nokamba ati, "Bamuna baku Israyeli naimwe bamene mulemekeza Mulungu, mverani. 17 Mulungu wa aba banthu waku Israyeli anasankha azitate bathu nopanga banthu kupaka pamene banankhala mumalo ya Egypto,Nakwanja kwamphamvu anabacosamo. 18 Kwazaka ngati 40 anabalekela mucipululu. (Ma baibulo yenengu yebelenga kuti, ko kwanila zaka 40 anabasamalila mu cipululu.) 19 Pamene anabononga vialo vili 7 mu malo ya Kenani, anapasa banthu bathu malo yabo kunkhala yabo. 20 Vonse ivi vocitika vanacitika pazaka zili 450. Pamene vinasila ivi vonse, Mulungu anabapasa oweluza mpaka Samuyeli muneneri. 21 Banthu panapempha kuti abapase mfumu, ndipo Mulungu anabapasa Sauli mwana wa Kishi, mwamuna ocokela ku banja ya Benjamini, kuti ankhale mfumu zaka zokwanila 40. 22 Pamene Mulungu anamucosa pa ufumu, ananyamula Davide kuti ankahale mfumu. Cenzeli pali Davide pamene Mulungu anakamaba, 'Napeza Davide mwana wa Jeseckunkhala mwamuna wapa mtima panga, wamene acita vilivonse vamene nifuna iye acita.' 23 Kucoka kumubado wauyu munthu Mulungu waleta kwa Israyeli mphulumusi, Yesu, monga mwamene analonjezela. 24 Ivi vanayamba kucitika pamene, Yesu sanabwele, Coyambilila Yohane ananounsa upatizo wotembenuka ku wanthu onse waku Israyeli. 25 Pamene Yohane enzosiliza nchito yake, anakamba ati, 'Kodi munganiza kuti ndine ndani? Sindine wamene. Koma mvesesani, kuliwina abwela pasogolo panga, wamene nthambo za sapato zake sindine oyenela kuzimasula.' 26 Abale, bana ocoka kuli Abrahamu, naimwe pakati panu wamene mulambila Mulungu, sikwaise kuti mau yacipulumuso yatumidwa. 27 Kwa iwo wamene ankhala mu Yelusalemu, nabolamulila bawo, sibanamuzindikile iye, ndipo wanakwanilisa zokambika za aneneri zamene zibelengedwa sabata iliyonse pakumuweluza iye. 28 Ngankhale kuti sibana peze cifukwa cenini comupaila iye, anauza Pilato kuti amupaye. 29 Pamene banasiliza zinthu zonse zamene zinalembedwa za yeve, banamucosa mumtengo nomushika mumanda. 30 Koma Mulungu anamuusha kuli wakufa. 31 Banamuona masiku ambili nawaja bamene wanabwela nayeve kucoka ku Galileya kubwela ku Yelusalemu. 32 So tibwelesa uthenga wabwino pamalonjezo yanapangiwa kuli azitate bathu: 33 Mulungu anasunga aya malonjezo kwa ise, kubana bawo, kuti anausha Yesu kubwelesa kumoyo. Izi ndiye zamene zinalembedwa muma Salimo wacibili: 'Ndiwe mwana wanga, lero nankhala Tate wako.' 34 Pali zoona kuti anamuusha kwa kufa kuti thupi yake sizabwele mkubola, akamba socabe: 'Nizakupasani zoyela namadaliso yene ya Davide.' 35 Nicifukwa cake akamba futi muma Salimo inangu, 'Suzalola Oyela wako kuti abole.' 36 Pamene Davide apanga mubado wake kutumikila zenzo funa Mulungu, anagona (anamwalila), noshikiwa na azitate bake, ndipo anabola, 37 koma iye wamene Mulungu anausha sanabole. 38 So lekani cizibika kwa inu, abale, kupitila muli uyu munthu kulalikidwa kukhululukidwa kwa macimo. 39 Kupitila mwa iye aliyense wakhulupilila alungamisiwa kuzithu zonse zamene lamulo ya Mose sinakwanise kulungamisa. 40 So cenjelani kuti zinthu zamene aneneri anakambapo siziza ciktika kwa imwe: 41 'Onani, imwe opepusa, mudabwisike ndipo mubonongeke; cifukwa nicita nchito mumasiku yanu, Nchito yamene simuzaikhulupilila, ngakhale kuti winangu ayinaunsa kuli imwe.'" 42 Pamene Paulo na Banabasi wenzocoka, banthu anabapempha kuti baka kambe futi aya mau yamozi nayamozi sabata yamene ibwela. 43 Pamene musonkhano wamusinagoge unasila, Ayuda bambili nabaja ozipeleka kuciyuda anakonkha Paulo na Banabasi, banakmba nawo nobalimbikisa kuti apitiliza mucisomo ca Mulungu. 44 Sabata yokonkhapo, pafufupi tauni yonse banakumana pamozi kuti bamverele mau ya Ambuye. 45 Pamene Ayuda anabona gulupu, banamvela jelasi noyamba kukamba mosushana navamene enzo kamba Paulo nomunyoza. 46 Koma Paulo na Banabasi anakamba mwaphamvu nokamba ati, "Cenzeli cofunikila kuti mau ya Mulungu ya yambilile kulalikilidwa kuli imwe. Kuoona kuti muyapushing'a kutali kuli imwe ndipo muziyesa osayenela ku umoyo osatha, onani, tizayenda kuli Akunja. 47 Cifukwa Ambuye atilamulila, kunena kuti, 'Nakuikani kunkhala nyali kwa Akunja, kuti mupeleke cipulumuso kumalekezelo yonse ya calo.'" 48 Pamene Akunja banamvera izi, banakondwela noyamikila mau ya Ambuye. Pabambili bamene anasankhidwa ku umuyo osatha banakhulupilila. 49 Mau ya Ambuye yanaperekewa ponse ponse mumzida onse. 50 Koma Ayuda analimbikisa azimai ozipeleka naboyenela, nabamuna benze osogolela mutauni. Banapangisa kusausidwa kwa Paulo na Banabasi nobaponya kupitilila kunja kwa tauni. 51 Koma Paulo na Banabasi anabana kukhumula kalukungu kucoka kumendo yabo. Pamene apo anayenda ku Tauni ya Ikoniyamu. 52 Ndipo ophunzila anambela cimwemwe nozuzhiwa na Mzimu Oyela.