1 Book yakudala yamene ninalemba, Fiyofilisa, inakamba vonse vamene Yesu anayamba kuchita nakupunzisa, 2 mpaka ija siku yamene analandiliwa ku mwamba. Ivi venzeli pambuyo pamene anapasa lamulo kupitila mwa Mzimu Woyela kuli ma apostoli bamene anasanka. 3 Pambuyo paku vutisiwa kwake, anazilangiza wamoyo kuli beve na umboni osashushika. Pamasiku yo kwanila 40 enzeli ku onekela kuli beve, ndipo anakamba za ufumu wa Mulungu. 4 Pamene enzeli kusonkhana pamozi nabeve, anabalamulila kuti basachoke mu Yelusalemu, koma kuti bayembekezele lonjezo ya Batate, yamene, banakamba, "Munavela kuchokela kuli ine 5 kuti Yohane zoona anali kubatiza na manzi, koma muzabatiziwa mu M'zimu Oyela mu masiku yang'ono.'' 6 Pamene banakumana pamozi banamufunsa, "Ambuye, kodi iyi ndiye nthawi yamene muzabwezela ufumu wa Israeli?" 7 Anakamba kuli beve, "Sindimwe mufunikila kuziba nthawi nangu nyengo yamene Batate banaika mwa mphamvu yabo. 8 Koma muzalandila mphamvu, pamene Muzimu Oyela azabwela pa imwe, ndipo muzankhala mboni zanga mu Yerusalemu namu Yudeya monse namu Samaria, nakosilizila kwa chalo." 9 Pamene Ambuye Yesu anakamba ivi vinthu, pamene beve benzeli kuyangana kumwamba, ananyamuliwa kuyenda kumwamba, na kumbi inamubisa kumenso yabo. 10 Pamene benzeli ku yanganisisa kumwamba pamene enzo yenda, Mosayembekezela, bamuna babili banaimilila pambali pabeve muli vovala voyela. 11 Banakamba ati, "Imwe bamuna baku Galileya, ni chifukwa chani muli imilile apa muyangana kumwamba? Uyu Yesu wamene anayenda ku mwamba azakabwela na futi chimozi -mozi monga mwamene munamuonela kuyenda kumwamba." 12 banabwelela ku Yerusalemu kuchokela pa lupili ya Olivu, yamene ili pafupi na Yerusalemu, mutunda ovomelezeka pa sabata. 13 Pamene banafika, banayenda mu chipinda chapamwamba, mwamene benzeli ku nkala. Panali Petulo, Yohane, Yakobo, Ndeleya, Philipo, Thomasi, Batlomeyo, Mateyo, Yakobo mwana wa Aliphasi, Simoni mu Ziloti, na Yudasi mwana wa Yakobo. 14 Banali bogwilizana pamozi bonse, pamene banapitiliza kupemphela maningi.Ku ikilapo panali futi bazimai, Maria mai wake wa Yesu, na babale bake. 15 Mumasiku yamene yaja Petulo anabwela nakuimilila pakati pa babale, bantu bokwanila ngati 120, nobwela ku kamba ati, 16 "Abale, chenzeli chofunikila kuti malemba yakwanilisike, yamene Muzimu oyela anakamba kudala kupitila mukamwa mwa Davide pa nkhani ya Yudasi, wamene anasogolela baja bamene bana manga Yesu. 17 Anali umozi wathu ndipo analandila gawo yake ya uno utumiki." 18 (Manje uyu mwamuna anagula munda nandalama zamene analandila mu umambala wake, ndipo pamene apo anagwa kuyambila mutu, na thupi yake inaseguka chifukwa cho pholeka, namatumbo yake yonse yanataika panja. 19 Bonse bonkhala mu Yelusalemu banamvela pali ivi, ndipo banaitana munda uja mucitundu cao "Akeldama," ndiyekuti "Munda wa Magazi.") 20 Cifukwa nicholembewa mu buku yama Salimo, 'Lekani munda wake unkhale owonongedwa, nakuti musavomeleze aliyense kuti ankhalemo'; 'Lekani munthu winagu atenge mupando wake wausongoleli.' 21 Nichofunikila, chifukwa chake, kuti umozi pali ba muna wamene anatikonkha nthawi zonse Ambuye Yesu anabwela nakuchoka pakati pathu, 22 kuyambila ku ubatizo wa Yohane kufikila siku yamene anayenda kumwamba kuchoka pali ise, afunika ankhale boni naise pa kuuka kwake." 23 Banapeleka bamuna ba bili, Yosefe oitaniwa Barsabasi, wamene anali anali kuitaniwanso kuti Jusitasi, na Matiyasi 24 Banapemphela nokamba ati, "Imwe, Ambuye, muziba mitima ya banthu bonse, ndipo woneselani kuti nindani pakati pali babili aba wamene mwasankha 25 kuti atenge malo mu utumiki wa apositoli kuchokela kuli Yudasi wamene anachoka kuyenda munjila zake." 26 Banachita masankho pali beve, ndipo kusankha kunagwela pali Matiyasi ndipo banamupendelapo pali ma apositozi bali 11.