Mutu 2 7

1 Manje pamene Solomoni anasiliza kupempela, mulilo unabwela pansi kuchoka kumwmba na kushoka nsembe zoshoka na nsembe zopasa, ndipo ulemelelo wa Yehova unazula mu nyumba. 2 Bansembe sibanakwanise kungena mu nyumba ya Yehova, chifukwa ulemelelo wake unazula munyumba yake. 3 Pamene bana ba Israyeli banaonamulilo ubwela pansi na ulemelelo wa Yehova pamwamba pa nyumba, banagwada pansi nankope zawo pansi pa mwala woikika na kulambila na kuyamika Yehova. Banati, "Pakuti ni wabwino, chifukwa chipangano chake nichamuyayaya." 4 Ndipo mfumu na bantu bonse banapeleka nsembe kwa Yehova. 5 Mfumu Solomoni inapeleka nsembe ya ng'ombe 22,000 na nkosa na mbuzi 120,000. Ndipo mfumu na bantu bonse banaipeleka nyumba ya Mulungu. 6 Bansembe banaimilila, aliyense kuimilila kwamene asebenzela; ma Levi nawo navilimba vawo vanyimbo kwa Yehova, vamene Davide mfumu anapanga zoyamikila Yehova munyimbo, "Chifukwa chipangano chake chili chamuyayaya." Bonse bansembe banaliza malupenga pasogolo pawo, ndipo Israeli yonse inaimilila. 7 Solomoni anapatula pakati pa bwalo pasogolo pa nyumba ya Yehova. Kwamene uko anapeleka nsembe zoshoka na mafuta ya nsembe za kuyanjana, chifukwa guwa yansembe yamukuwa yamene banamanga siinakwanise kugwila nsembe zoshoka, nsembe zambeu na zamafuta. 8 Ndipo Solomoni anachita chikondwelelo masiku yali 7, na bonse ba Israeli, musonkano waukulu kwambili, kuchokela ku Lebo Hamati mpaka ku mumana wa ku Igupto. 9 Pa siku lachisanu na chitatu anachita musonkano waukulu, chifukwa anapatulila guwa ya bansembe masiku yasanu na yabili, na madyelelo masiku yasanu na yabili. 10 Pa siku ya 23 ya mwezi wachisanu na chibili, Solomoni anatuma bantu kuti bayende ku matenti yawo na chimwemwe na mitima yokondwela chifukwa cha zabwino zamene Yehova anachitila Davide, Solomoni, na Israeli, bantu bake. 11 Momwemo Solomoni anasiliza kumanga nyumba ya Yehova na nyumba yake. Chilichonse chamene chinabwela mumutima wa Solomoni kupanga mu nyumba ya Yehova na munyumba yake, anachikwanilisa bwino. 12 Yehova anaonekela kuli Solomoni usiku nakumuuza kuti, "Nanvela pempelo yako, ndipo nazisankila yano malo monga nyumba yopelekelamo nsembe. 13 Nanga ngati navala kumwamba kuti kulibe nvula, kapena nalamulila zombekuononga ziko, kapena nikatuma matenda pakati pa bantu banga, 14 ndipo ngati bantu banga, bamene baitaniwa pazina yanga, bazazichepesa, kupempela, nakufuna nkope yanga, na kuchoka kunjila zawo zoipa, nianvela kuchoka kumwamba, kubakululukila machimo yawo, na kupolesa ziko yawo. 15 Manje nizasegula menso yanga na makutu yanga kunvela ku mapempelo yamene yachitikila pamalo yano. 16 Chifukwa nasanka na kupatula ino nyumba kuti zina yanga izankalapo muyayaya. Menso yanga na mutima wanga yazankala kwamene uko masiku yonse. 17 Koma iwe, ukayenda pamenso panga monga Davide batate bako banayendela, kumvelela vonse vamene nakulamulila, na kusunga malamulo yanga, malemba anga, 18 nizankazikisa mupando wako wachifumu, monga ninakambila muchipangano na Davide batate bako , pamene ninakamba kuti, 'Mwana wako sazakangiwa kunkala olamulila Isiraeli.' 19 Koma ngati wachokako, na kukana malemba na malamulo yanga yamene naika pasogolo pako, ndipo ukayenda kupembeza milungu inangu na kuigwadila, 20 nizabachosa kuchoka mu ntaka yamene nabapasa. Iyi nyumba yamene naipatula chifukwa cha zina yanga, nizayitaya kuchoka pamenso panga, ndipo nizaipanga mwambo na chosekewa mukati mwa bantu. 21 Ngakhale iyi tempele niyokwela kwambili, aliyense wamene azapita pafupi azadabwa eka. Bazafunsa kuti, 'Nichifukwa chani Yehova achita izi ziko lino na nyumba iyi?' 22 Benangu bazayanka, 'Chifukwa banakana Yehova, Mulungu wawo, wamene anabwelesa makolo yawo kuchoka mu ziko ya Aiguputo, ndipo banagwililila milungu inangu ndi kuigwadira na kuigwadia na kuipembeza. Ndiye chifukwa chake Yehova abwelesa chionongeko ichi chonse."