Mutu 2

1 Manje solomoni analamulila kuti bamange nyumba ya zina ya Yehova na kumananga nyumba ya ufumu mu ufumu wake. 2 Solomo anaika bamuna 70,000 bonyamula katundu, na bamuna 80,000 kuti bankale bojuba myala kumalupili, na bamuna 3,600 kuti bazibayanganila. 3 Pamene apo Solomo anatumiza mau kuli Hiramu mfumu ya ku Turo, kukamba kuti, “Monga mwamene munachitila na tate wanga Davide, pakumutumizila mitengo ya mkunguza kuti amange nyumba yonkalamo, imwe muchite so chabe na kuli ine. 4 Ona nasala pan'gono kumangila nyumba zina ya Yehova Mulungu wanga, kuti niyipatule, na kuputiza vonunkila pamenso pake, kupeleka mukate wopatulika, na nsembe zopseleza kuseni na kumazulo, pa Masabata na pa myezi yanyowani, na pa mapwando yo yikiwa ya Yehova Mulungu watu. ivi niva ntau zonse, kuli Israeli. 5 Nyumba yamene nizamanga izankala ikulu maningi, chifukwa mulungu watu ni mukulu kuchila milungu zinango zonse. 6 Koma nindani angakwanise kumangila Mulungu nyumba, pakuti cholengewa chonse ngankale kumwamba sikungankale na eve? Ndine ndani kuti nimumangile nyumba, koma kuperekela nsembe zopsereza pamenso pake? 7 ndiye Chifukwa chake nitumizileni muntu waluso pa nchito ya golide, siliva, mkuwa, chisulo, na nyula ya chibakuwa, yofiila, na tonje yamanzi; azankala na bamuna baluso bamene bali na ine ku Yuda na ku Yerusalemu, bamene Davide tate banga anapasa. 8 Nitumizileni futi mitengo ya mkunguza, mkunguza, na mialigamu yochokela ku Lebanoni, chifukwa niziba kuti batumiki banu bamaziba kujuba mitengo ku Lebanoni. onani, banyamata banga bazankala na bakapolo banu, 9 kuti banikonzele mitengo yambili; 10 onani, nizapasa bakapolo banu, bamene bazadula mitengo, zikwi makumi yabili ya tiligu, makilogilamu zikwi makumi yabili ya balele, malita makumi yabili ya vinyo, na misuko ya mafuta zikwi makumi yabili. 11 Pamene apo Hiramu, mfumu ya ku Turo, anayanka na kulemba, nakutumiza kuli Solomo,'' nakukamba, pakuti Yehova akonda bantu bake, anakuyika iwe mfumu yao. 12 Kuwonjezerapo, Hiramu anakamba, "Adalisike Yehova, Mulungu wa Israeli, wamene analenga kumwamba na ziko yapansi, wamene anapasa mfumu Davide mwana wanzelu, wanzelu na woziba, bamene bazamangila Yehova nyumba na nyumba ya ufumu yake mwine. 13 Manje natumiza muntu waluso, Huram-Abi, wamene anapasiwa mpaso yo mvesesa. 14 Na mwana mwamuna wa mukazi wa bana bakazi ba Dani. Batate bake banali ba ku turo. eve ni waluso pa nchito yagolide, siliva, yamkuwa, yachisulo, yamyala, yamitengo, na yofiirira, yamtambo, na yofiira, na bafuta yotelela. Futi niwaluso mukupanga vili vonse vo beza futi na kapangidwe ka vili vonse vosiyanasiyana. Mumupase malo pakati pa ba nchito banu baluso, na kuli ba Ambuye wanga Davide tate wanu. 15 Manje tiligu, balele, mafuta na vinyo, vamene mbuye wanga mwanena, atumize ivi kuli bakapolo bake. Tijuba mitengo kuchokela ku Lebanoni, mitengo yambili yamene munga fune. 16 Tizayenda na imwe monga matanga yoyenda panyanja kuyenda ku Yopa, ndipo imwe muyende nabo ku Yerusalemu. " 17 Ndipo Solomo anabelenga balendo bonse bonkala muziko ya Israyeli, monga machitidwe Anababelenga Davide, atate bake. Beve banapezeka kuti benze 153,600. 18 Anabapasa bantu 70,000 kuti banyamule katundu, benango 80,000 kuti bankale Bojuba myala mumapili, ndipo 3,600 bankale boyang'anila bantu bogwila nchito.