Mutu 15

1 Davide anamanga manyumba yake muzinda ya Davide. Eve anakonzekela malo ya likasa ya Mulungu na kuyipangila hema. 2 Pamene apo Davide anakamba kuti, aLeviti chabe ndiye bazatenga likasa ya Mulungu, chifukwa beve bana sankiwa kuli Mulungu kuti batenge likasa ya Yehova, nakumusebenzela eve muyayaya. 3 Davide ana sokanisa bonse aIsrael ku Yerusalemu, kubwelesa likasa ya Yehova ku malo yamene anayikonzekela. 4 Davide anasokaniza pamozi mubado wa Aaroni na wa ALevi. 5 Kuchokela mubado wa Kohath, kunali Uriel musogoleli na banja yake, amuna 120. 6 Kuchokela mubado wa Merari, kunali Asaiah musogoleli na banja yake,amuna 220. 7 Kuchokela mubado wa Gershom, kunali Joel musogoleli na banja yake, amuna 130. 8 Kuchokela mubado wa Elizaphan, kunali Shemaiah musogoleli na banja yake, amuna 200. 9 Kuchokela mubado wa Hebroni, kunali Eliel musogoleli na banja yake, amuna eyite. 10 Kuchokela mubado wa Uzziel, kunali Amminadab musogoleli na banja yake, amuna 112. 11 Davide anayitana Zadok na Abiathar ansembe, na aLevi Uriel, Asaiah, Joel, Shemaiah, Eliel, na Amminadab. 12 Eve anakamba kuli beve kuti, '' Imwe ndimwe asogoleli yama banja ALeviti. Muzipatule imwe, imwe nababale bako, pakuti imwe mungabwelese liksa ya Yehova, Mulungu wa Israel, kumalo yamene ninayigonzekela. 13 Simuna nyamule pa nthawi yoyamba. Nichifukwa chake Yehova Mulungu wathu watisusa ife, popeza kuti sitinamufunefune kapena kumvela lamulo yake. '' 14 Ansembe na ALevi anazipatula kuti atenge likasa ya Yehova, Mulungu wa Israel. 15 Chifukwa chake ALevi ananyamula likasa ya Mulungu pa mapeya yawo na mizati, monga analamulila Mose - kukonka malamulo yamene yanapasiwa na mawu ya Yehova. 16 Davide analankhula na asogoleli ALevi kuti asanke abale awo ngati oyimba amene azayimba mokwezeka na zida zoyimbila, azeze na zeze na zinganga, kuti akwezeke zikumveka zachimwemwe. 17 Ndipo ALevi anasanka Hemani mwana mwamuna wa Joel na umozi mubale wake, Asafu mwana mwamuna wa Beereya. Beve bana sanka futi achibale ochokela ku mbado wa Mereri na Ethan mwana wa Kushaiah. 18 Abale awo achibili anali nawo: Zekariya, Yezieli, Shemiramoti, Yehieli, Unni, Eliabu, Benaya, Maaseya, Mattithiya, Eliphelehu, Mikneya, Obedi Edomu, na Jeieli, akamilonda a pazipata. 19 Oyimba nyimbo monga Heman, Asafu, na Ethani anasankiwa kuti azimenya kwambili zinganga zamkuwa. 20 Zekariya, Azieli, Shemiramoti, Yehieli, Unni, Eliabu, Maaseya na Benaya ezoliza azeze, konza ku Alamoth. 21 Mattithiya, Eliphelehu, Mikneya, Obedi Edomu, Jeieli, na Azaziah anasogolela njila na azeze okonzekela ku Sheminith. 22 Kenaniya, musogoleli wa ALevi, ndiye anali woyanganila kuyimba chifukwa eve anali muphunzisi wanyimbo. 23 Beereya na Elikana banali baka mlonda wa likasa. 24 Sebaniya, Yosafati, Netaneli, Amasai, Zekariya, Benaya, na Eliezere, ansembe, enzofunika kuliza malipenga pasogolo pa likasa ya Mulungu. Obedi Edomu na Jehiya anali malonda ya likasa. 25 Davide, akulu Aisrael, na asogoleli a masausande anayenda kutenga likasa ya chipangano ya Yehova kuchokela munyumba ya Obedi Edomu na chisangalalo. 26 Pamene Mulungu anathandiza ALevi amene anatenga likasa ya chipangano cha Yehova, beve banapeleka nsembe ng'ombe zisanu na ziwili na nkhosa zamphongo zisanu na ziwili. 27 Davide anavala mukanjo ya nula yabwino kwambili, monga ALevi amene anatenga likasa, oyimba nyimbo, na Kenaniya, musogoleli wa nyimbo pamozi na woyimba. Davide anavala nula ya efodi. 28 Onse Aisraeli anabwelesa likasa ya chipangano cha Yehova kufuula mokondwela, na kuwomba kwa nyanga na malipenga, na zinganga, na azeze na zeze. 29 Koma pamene likasa ya chipangano cha Yehova inabwela ku muzinda wa Davide, Michal mwana wa Saul, anayangana panja pa zenela. Eve anaona mfumu Davide avina nakusangalala. Pamene apo anamunyoza eve mumutima mwake.