1 Bwelani manje, imwe bolemela, lilani mopunda chifukwa cha mavuto yamene yabwela kuli imwe. 2 Chuma chanu chaonongeka, navovala vanu vadyewa na vidoyo. 3 Golide na siliva yanu yaonongeka. Kuonongka kwabo kuzankala kamboni osusha imwe. Chizadya nyama yatupi yanu mona mulilo. Munasunga mozula chuma chanu kusungila masiku yosilizila. 4 Onani, malipilo ya wantchito yalila-malipilo yamene munakana kulipila baja bamene banakolola minda zanu, na kulila kwa bokolola kwa fika mu matu ya Ambuye wa makamo. 5 Munankala mozimvesa bwino pa ziko na kusangalalisa moyo zanu. Munainisa mitima zanu kulindila siku ya pwando. 6 Muna weluza naku paya muntu olungama. Sana ku shusheni. 7 Mwa ici nkalani oleza mutima, abale, mpaka kubwela kwa Ambuye. Onani, mulimi ama embekezela vokolola vake vamutengo vochokela mumunda. Amankala oleza mutima kulindila, mpaka pamene alandila mvula yoyamba na yosilizila. 8 Naimwe, chimozo-mozi, nkalani odeka mutima. Limbikisani mitima zanu, chifukwa kubwela kwa Ambuye kuli pafupi. 9 Musadaundaule, abale, wina pali muzake, mwakuti musaweluziwe. Onani, eve oweluza aimilila pa chiseko. 10 Tenganiponi chisanzo, abale, pa kuvutika na kudeka mutima kwa aneneli, bamene bana kamba muzina ya Ambuye. 11 Onani, tima lemekeza baja bana pilila kuti nibo dalisika. Munamvela kulimbikila kwa Yobo, ndipo muziba lingo ya Ambuye, mwamene balili na chikondi komanso ba chifundo. 12 Pavonse, abale, musalape, kapena kumwamba kapena pansi, kapena kulapa kuli konse. Koma, lekani "kuvomela" kwanu kunkale "kuvomela" na ku "kana" kwanu kunkale "kukana," mwakuti musagwele muchiweluzo. 13 Nanga pali aliyense pakati panu wamene avutika? Mulekeni apempele. 14 Nanga pali wamene ali na chimwemwe? Mulekeni aimbe nyimbo zama tamando. Nanga pali odwala? Mulekeni aitane bakulu bamu pingo, lekani bamupempelele. Lekani bamu zoze na mafuta muzina ya Ambuye. 15 Pempelo ya chikululupilo izachilisa eve odwala, ndipo Ambuye baza muimya. Ngati anachimwa, Mulungu azamu kululukila. 16 Mwa ici lapani machimo yanu kuli wina na muzake, ndiponso mupempelelane, mwakuti mu polesewe. Pempeleo ya uja olungama niya mpavu mukusebenza kwake. 17 Eliya anali muntu monga ise. Anapempela mokululupira kuti mvula isagwee, ndipo mvula si inagwe paziko zaka zitatu na myezi sikisi. 18 Ndiponso Eliya anapempela kachibili. Kumwamba kunapeleka mvula, na minda inapeleka vipaso vake. 19 Abale, ngati wina aliyense ataika kucho-onadi, ndiponso winangu amubweza, 20 uja muntu ayenela kuziba kuti aliyense wamene abwezela ochumwa kuchoka mukutaika kwake amupulumusa ku imfa, komanso azavinikila machimo yambili.