Mutu 55

1 "Bwelani, bonse bamene bomvela njota, bwelani ku manzi, naimwe bamene ,ulibe ndalama, bwelani, mugule nakudya! Bwelani, mugule vinyo nakukaka palibe ndalama namutengo wake. 2 Nichani mupima kulema kwa siliva pamene si buledi, nichani chamene musebenza osa kutila? Mvelani mosamala kuli ine nakudya za bwino, naku kondwela muku ina. 3 konsesani matu yanu nak bwela kwaine! kuti mukale na moyo! Niza panga chipangano chamene sichizasila naiwe odalila-wanga, chikulupililo chachikondi chamene nina uzilatu kuli Davide. 4 Onani, na muika kunkala mboni ku maiko, kunkala musogoleli naku nkala mukulu pa bantu. 5 Onai,Uza itana pa ziko yamene siwenze kuziba; na ziko yamene siyenze kuku ziba iza tamanga ku bwela kuli iwe chifukwa cha Yehova Mulungu wako, Woyela wa Isilayeli, wamene aku kwezani inu." 6 Funani Yehova pamene oyenela kupezeka; mu itaneni pamene ali pafupi. 7 Lekani boipa basiye njila yabo, na muntu wochimwa muma ganizo yake. Lekani abwelelel kuli Yehova, ndipo ozamumvelela chifundo, na kuli Mulungu watu, amati chizati kululukila mosalekeza. 8 "Maganizo yanga simanganizo yanu, kapena njila zanu sinjila zanga-uku ndiye kukamba kwa Yehova- 9 monga mwamene mwamba ili pamwamba paziko lapansi, ndiye njila zanga zili pamwamba pali njila zanu, na maganizo yanga simaganizo yanu. 10 Mwamene mvula na matala a yamagwa pansi kuchoka ku mwamba ndipo sima bwelela kufika yahilila ziko la pansi na kulenga zomela kupukila ndi kubala mbeu kuli mulimi omene azashanga ndipo muledi kuli bamene bakudya, 11 mau yanga ni mau yamene yachoka mukamwa mwanga-siyaza bwelela kwaine palibe, koma yama kwanilisa cholinga chomene nina yatuma. 12 Pakuti muzapita muchisangalalo naku sogoleledwa pamozi ndi mutendele; malupili yangono yaza kondwela naku punda maningi pamenso pako, na mitengo zamu munda zizatota manga yabo. 13 Mumalo mwavi saka saka, mutengo wa sipras uzakula; na mulala mwa mutengo wa Brier, mutengo wa myrlt uzakula, ndipo chinkala kuli Yehova, na zina yake, chowonesa chamuyayaya chamene sichiza jubika.