Mutu 41

1 "Mvelani kuli ine osapanga chongo, lekani maziko yanklenso nampamvu; yabwele pafupi nakukamba tibwele pamozi nakusiliza ntota. 2 Nindani wamene ayambanisa baku maba, kumu litana muchilungamo ku nchito yake? Apasila enve doti nalupanga wake, monga chimpepo chamene chi ulusa mapesi. 3 ba konaka nobapitilila, munjila mwamsanga kuti mendo yake yadyaka pangono pansi. 4 Nibandani ba chita ivi naku kwanilisa? nindani wamene ayitana mibadwa ku chokela ku chiyambi? Ine, Yehova, Oyamba, na osilizila, Ndine Ine. 5 Maziko yaku nyanja yaona yopa; kosilizila chalo kwa njema; Ba bwela. 6 Aliyense atandiza ba neba bake, na kukamba kuli wina na munzake, 'kulimbikisiwa.' 7 Mwaicho opala mapulanga alimbisa osula visulo golide, uyo osebenza na sando alimbisa osebenzesa chezulo, ku kamba voshokelela, nicabwino kokomela na misomali kuti chisagwe. 8 Koma, Isilayeli, banchito banga, Yakobo wamne nasanka, mubadwe Abrahamu munzanga, 9 Nina kutenngani ku chokela kumalile ya ziko yapansi nakuba itanani kuchokela kumali yakutali, kukamba kuli imwe, "Ndimwe ba nchito banga." Nakusankani imwe sinina kukaneni. 10 Musayope, pakuti nili naimwe, Musankale bamaganizo, pakuti ndine Mulungu wanu niza kulimbisani imwe, Nizakutandizani, ndipo nizakugwililani imwe nakwanja yanga ya manja yoyela. 11 Onani, ba zamvela nsoni na manyazi, bonse bamene bali naukali kuli iwe; ba zankala bachabe chabe ndipo ba zaonongeka, abo bo sushana naimwe. 12 Muzaka sakila simza kapeza abo boyamaba naimwe; abo bamene bachita nkondo naimwe azankala bachabe chabe, bosililato nchtio. 13 Chifukwa ine, Yehva Mulungu wanu, nizakagwilila kwanja yanu ya manja, kukamba kuli imwe, musayope, nikutandzani.' 14 Musayope, Yakobo, iwe nyongololo, naimwe bamuna baku Isialyeli; niza kutandizani-nivamene akamba Yehova, okuwombolani wanu, oyela wa Isilayeli. 15 Onani, nikupangani imwe monga chisulo choshubilako, chanyowani na yonola-kubili imwe muzagaya malupili nakuya nyanyawula; muzapanga machul monga mauzu yoyuma. 16 muzaba kolola, ndipo mpepo iba nyamulila kutali; mpepo izaba mwazya. Muza kondwela muli Yehova, muza kondwela kulio oyela wa Isilayeli. 17 Bo dyakilila naba sauka bofuna manzi, koma kulibe, namalimi yabo yayuma nanjota; Ine, Yehova niza bayanka mapempelo yabo Ine, Mulungu wa Isilayeli, sinizabalekelela. 18 Niza panga mimana kutilila kumu tentemuko, na manzi yobils pakati pa vikwa. Nizalengea chipululu kunkala manzi, mumalo yoyuma manzi yobila. 19 Muchipululu nizaika keda, akesya, na mato, na mutengo wa olive. nizaika sipresi muchipululu, na pine na saipresi. 20 Niza chita ichi kuti bantu ba one, bazindikile, bamvele pamozi, kuti kwanja kwa Yehova kwa chiya ivi, kuti oyela wa Isilayli wazi panga. 21 "Letani mulandu wanu, "akamba Yehova, "Letani zamene mukambilako mafano yanu, "akamba mfumu ya Yakobo. 22 Lekani balete vosusha vawo kuli ise; babwele kusogolo bati uze vamene vizachitika, pakuti tivi ibe bwino. Ba tiuze vimene onakamba poyamba. kuti tikumbke naku ziba mwamen viza kwanilisiwa. 23 Kambani vaku sogolo, kuti tizibe ngati ndimwe tumilungu; chitani vamushe olo voipa, kuti tiyope na kukondwla. 24 Onani, Imwe mafano nimwe ba chabe chabe na vochita vanu; bamene baku sankani nibo kowela. 25 Nanyamula umozi kuchokela ku mpoto, ndipo babwela; kuchokela pamene zuba ichoka ni itana bonse bamene baitana pa zina yanga, ndipo bazadyaka bolamulila monga matika, monga bobumba bamene badyaka doti yowumba. 26 Niba ndani bana kamba ivi poyambilila, kuti tizibe? pambuyo pa ino ntawi, tingakambe kuti, "Bali bwino"? Nicho-ona palibe bamene bana chikamba, nizo-ona palibe anamvela kukamba kwanu. 27 Nina kamba poyamba kuli Zayoni, "Onani aba bali apa:" Ninatumiza utenga ku Yelusalemu. 28 Nikayangana, palibe bali bonse, palibe pali benve banga pase nzelu zabwino, bamene, nikaba funsa, banga yanke mau. 29 Yangani, bonse balibe nchito, na zohia zabo zilibe nchhito; na zisulo zabo na nsimbi zamangiwa zilibe nchito.