Mutu 10

1 Pamene Ezra anapempela na kulapa, analila nakuziponya pansi pa nyumba ya Mulungu. Bantu bambili ba Israyeli bamuna, bakazi, na bana banakumana pali eve, pakuti bantu beze kulila maningi. 2 Shekaniah mwana mwamuna wa Jehiel obadwa mumbuyo mwa Elam anakamba, " Ise tankala osakulupililika kuli Mulungu wantu ndipo takwatila bakazi bakwinangu kuchokela kubantu baku malo yenangu. Koma ngakale izi, kukali chiyembekezo pali Israyeli. 3 Manje lekani tipange chipangano na Mulungu wantu kutuma bakazi bonse na bana bao kuchoka kuno kulingana na mwamene Ambuye bakambila na bamene bakakonka malamulo ya Mulungu wantu bama njenjemela, ndipo tileke chichiteke kulingana na malamulo. 4 Nyamukani, pakuti ichi chintu chifunika imwe muchichite, ndipo tili naimwe. Nkalani bolimba na kuchita ichi." 5 Ndipo Ezra anauka nakupanga ba sembe, Balevi, na bonse ba Israyeli lonjeza kuchita munjila yamene iyi. 6 Manje bonse bana panga lumbilo ya ulemu. Ndipo Ezra ananyamuka kuchokela kusogolo kwa nyumba ya Mulungu na kuyenda ku zipinda za Jehohanan mwana mwamuna wa Eliashib. Sanadye mukate uli wonse kapena kumwa manzi, chifukwa ezeli kulila zokhuza kusakulupililika kwa bamene bezeli mu ukapolo. 7 Pamene banatuma mau mu Yuda na Yerusalemu kubantu bonse banachoka kuukapolo kuti bakumane mu Yerusalemu. 8 Aliyense wamene sana yende kumasiku yatatu kulingana namalamulo yabakulu-bakulu banataya vintu vonse vabo ndipo bana chosewa kukukumana kwa bambili bantu bazeli babwela kuchokela kuukapolo. 9 Manje bamuna bonse ba Yudah na Benjamin banakumana mu Yerusalemu masiku yatatu. Weze mwezi wa naine pasiku ya 20 ya mwezi. Bonse bantu banankala pamalo yakulu pa nyumba ya Mulungu, kunjenjemela chifukwa chaichi na chifukwa cha bvula. 10 Ezra wa nsembe anakamba. "Imwe mweka mwapanga mulandu. Munankala nabakazi bakwinangu kuikilako uchimo wa Israyeli. 11 Koma manje pasani matamando kuli Yahwe, Mulungu wamakaolo banu bakale. Chokani palibantu bakumalo na bakazi bakwinangu." 12 Bonse banakumana banayanka kumpunda, " Tizachita mwamene mwakambila. 13 Koma, palibantu bambili, nafuti ni nthawi yamvula. Tilibe mphamvu zoimilila panja, ndipo ino siskiu yoyamba kapena yachibili yanchito, pakuti tachimwa manigi pakanakni iyi. 14 Manje lekani bakulu bayimilile kukumana konse. Lekani bonse bamene balola bakazi bakwinangu kunkala mu siti yantu babwele panthawi yamene izayikiwa naba kulu ba siti nabo weluza kufikila kupya kwa mtima kwa Mulungu wantu kutachoka pali ise." 15 Jonathan mwana mwamuna Asahel na Jahzeiah mwana mwamuna wa Tikvah banasusa ichi, na Meshullam na Shabbethai ba Levi banavomeleza ichi. 16 Motero bantu bamene banabwelela kuchaka kuukapolo banachiyta ichi. Ezra wasembe anasanka bamuna, basogoleli muma banja yamakolo yakale na manyumba - bonse nama zina yabo, banaona pankani iyi pasiku yoyamba ya mwezi wa 10. 17 Kufika pa siku yoyamba ya mwezi bana siliza kupeza bamuna bamene baze bankala nabakazi bakwnangu. 18 Pakati pabo badwa mumbuyo ba basembe pezeli baja bamene banankala nabakazi bakwinangu. Pakati pabobadwa mumboyo ba Yeshua mwana mwamuna wa Jozadak na balongo bamuna bake peze Maaseiah, Eloiezer, Jarib, na Gedaliah. 19 Motelo beze bolimbikila kutuma bakazi bao kunangu. Chifukwa beze bolakwa, banapeleka khosa kuchokela pa gulu yakhosa za pakuti bezeli bolakwa. 20 Pakati pa bobadwa mumnuyo ba Immer: Hanani na Zebadiah. 21 Pakati pa bobadwa mumbuyo ba Harim: Maaseiah, Elijah, Shemaiah, Jehiel na Uzziah. 22 Pakati pabobadwa mumbuyo ba Pashhur: Elioenai, Maaseiah, Ishmael, BNethanel, Jozabad, na Elasah. 23 Pakati pa ba Levi: Jozabad, Shimei, Kelaiah - peze, Kelita, Pethahiah, Yudah, na Eliezer. 24 Pakati paboyimba: Eliashib. Pakati pabo londa zipata: Shallum, Telem, na Uri. 25 Pakati pabonse ba Israyeli - pakati pabobadwa mumbuyo ba Parosh: Ramiah, Izziah, Malkijah, Mijamin, Eleazar, Malkijah, na Benaiah. 26 Pakati pabobadwa mumbuyo ba Elam: Mattaniah, Zechariah, Jehiel, Abdi, Jeremoth, na Elijah. 27 Pakati pabobadwa mumbuyo ba Zattu: Elioenai, Eliashib, Mattaniah, Jeremoth, Zabad, na Aziza. 28 Pakati pabobadwa ba Bebai: Jehohanan, Hananiah, Zabbai, na Athlai. 29 Pakati pabobadwa mumbuyo ba Bani: Meshullam, Malluk, Adaiah, Jashub, na Sheal Jeremoth. 30 Pakati pabo badwa mumbuyo ba Pahath - Moab: Adna, Kelal, Benaiah, Maaseiah, Mattania, Bzalel, Binnui, na Manasseh. 31 Pakati pabobadwa mumbuyo ba Harim: Eliezer, Ishijah, Mulkijah, Shemaiah, Shimeon, 32 Benjamin, Malluk, and Shemariah. 33 Pakati pa bobadwa mumbuyo ba Hashuna: Mattenai, Mattattah, Zabad, Eliphelet, Jeremai, Manasseh, and Shimei. 34 Pakati pa bobadwa mumbuyo ba Bani: Maadai, Amram, Uel, 35 Benaiah, Badeiah, Keluhi, 36 Vaniah, Meremoth, Eliashib, 37 Mattaniah, Mattenai, na Jaasu. 38 Pakati pabobadwa mumbuyo ba Binnui: Shoimei, 39 Shelemiah, Nathan, Adaiah, 40 Maknadebai, Sheshai, Sharai, 41 Azarel, Shelemiah, Shemariah, 42 Shallum, Amariah, Joseph. 43 Pakati pa bobadwa mumbuyo ba Nebo: Jeiel, Mattithiah, Zabad, Zebina, Jeddai, Joel, and Benaiah. 44 Bonse aba bezeli banatenga bakazi bakwinangu ndipo banankala nabana nabo.