Mutu 5

1 Mose anaitana ba Israeli bonse nakukamba kuli beve, '' Nvelani, Israeli, kuvo funika kukonka na malamulo yamene niza kamba mu matu mwanu lelo, kuti mungaya punzile na kuyasunga. 2 Yehova mulungu watuanapanga chipangano naife ku Horebu. 3 Yehova sanapange chipangano namakolo yatu, koma naife, bonse tili na moyo lelo. 4 Yehova anakamba naimwe menso na menso pa lupili kuchoka mukati mwa mulilo 5 (Ninaimilila pakati pa Yehova na imwe pali ija ntawi, kuvumbulusa kuli imwe mau yake; chifukwa munali na manta chifukwa cha mulilo, ndipo simunayende pamwamba pa lupili). Yehova anati, 6 'Ndine Yehova Mulungu wanu, wamene anakuchosani ku ziko ya Igupto, kuchoka mu nyumba ya ukapolo. 7 Simuzankala na milungu inangu pasogolo panga. 8 Imwe simuzapanga kwa imwe mweka chosema chooneka kapena chilichonse chofanizila cha chilichonse chamene chili kumwamba, kapena chamene chili mu ziko lapansi, kapena chamene chili pansi pa manzi. 9 Simuzagwada pansi kuli beve kapena kusebenzela beve, chifukwa ine, Yehova Mulungu wanu, ndine Mulungu wa jelasi. Nimapasa chilango pa kuchimwa kwa makolo paku leta chilango pa bana, kufikila wachitatu na wanamba folo mubadwe kuli awo bamene bazonda ine, 10 na kulangiza chamuyaya chikondi kuma sauzande, kuli awo bamene bakonda ine na kusunga malamulo yanga. 11 Imwe musatenge zina ya Yehova Mulungu wanu mwa chabe, chifukwa Yehova sazaleka kumugwila mulandu wamene atenga zina yake mwachabe. 12 Sungani siku ya Sabata kuisunga inkale yoyela, monga Yehova Mulungu wanu alamulila imwe. 13 Pa masiku yali sikisi muzasebenza na kugwila zonse nchito zanu; 14 koma siku ya namba seveni ni sabata kwa Yehova Mulungu wanu. Pali iyo simufunika kuchita iliyonse nchito- osati imwe, kapena bana banu bamuna, kapena bana banu bakazi, kapena banchito banu bamuna, kapena banchito banu bakazi, kapena ng'ombe zanu, kapena mabulu yanu, kapena iliyonse nyama yanu, kapena mulendo wamene ali mukati mwa geti yanu. Ichi nichakuti banchito banu bamuna na bakazi banchito bangapumule monga na imwe. 15 Muzaitanila kunzelu kuti munali ba kapolo mu ziko ya Igputo, ndipo Yehova Mulungu wanu anakuchosani imwe kuchoka kuja na kwanja yampanvu na kotambuluka kwanja. Ndiponso Yehova Mulungu wanu alamulila imwe kusunga siku ya sabata. 16 Lemekezani batate banu na bamai banu, monga Yehova Mulungu wanu alamulila imwe kuchita, kuti munkale ntawi yaitali mu ziko yamene Yehova Mulungu wanu akupasani, na kuti viziyenda bwino naimwe. 17 Iwe siuzapaya. 18 Siuzachita chigololo. 19 Siuzaba. 20 Siuzapasa umboni waboza mosusana na wapafupi panu. 21 Iwe siuzatengela mukazi wa munzako, siuzapasula nyumba ya munzako, munda wake, kapena wanchito bake bamuna, kapena wanchito wake mukazi, ng'ombe zake, kapena ma bulu yake, kapena chilichonse chamene chili chamunzako.' 22 Aya mau Yehova anayakamba monveka kuli bonse banasonkana palupili kuchoka pakati pa mulilo, yamu makumbi, na chimudima chikulu; sanafakilepo yaliyonse yambili mau. Analemba ayo pansi pa mwala na kubapasa beve. 23 Kunabwela kuti, pamene munanvela mau kuchokela mukati mwa mudima, pamene lupili lunali kupya, kuti munabwela pafupi naine- bonse bakulu banu na wosogolela ba mitundu yanu. 24 Munakamba kuti, 'Onani, Yehova Mulungu wathu atilangiza ife ulemelelo wake na ukulu wake, ndipo tanvela mau yake kuchoka mukati mwa mulilo; taona lelo kuti Mulungu amakamba na bathu, bangankale namoyo. 25 Nanga nichani chamene tingafele? Chifukwa uyu mulilo ukulu uzatishoka ife; ngati tanvela mau ya Yehova Mulungu wathu mopitilila, tizamwalila. 26 Nanga nindani kumbali kwatu aliko pakati pa yonse tupi wamene ananvela mau ya Mulungu wamoyo akamba kuchoka mukati mwa mulilo na kunkala naumoyo, monga mwamene tachitila? 27 Monga kuli imwe, mufunika kuyenda na kunvela kuli vilivonse vamene Yehova Mulungu wanu akamba; mubwezepo kwa ife vilivonse vamene Yehova Mulungu wanu akamba kuli imwe; tizanvela kuli icho na kukonka.' 28 Yehova ananvela mau yanu pamene munakamba kuli ine. Anakamba kuli ine, Nanvela mau ya aba bathu, vamene banakamba kuli iwe. Vamene banakamba vinali bwino. 29 Ya, kapena kunali monga wachonco mutima muli beve, kuti banganilemekeze ine na lyonse kusunga malamulo yanga, kuti zizibayendela bwino na bana bawo muyayaya! 30 Yenda nakuuza beve, ''Bwelelani ku misasa yanu.'' 31 Koma kuli imwe, imililani pano naine, ndipo nizakuuzani yanse malamulo, zoikika, na zokambidwa zamene muzabapunzisa beve, kuti bayasunsunge ayo mu malo yamene nizabapasa kuti batenge.' 32 Muzasunga, chamene Yehova Mulungu wanu akuuzani; Simuzapindamukila kumbali inangu ku kwanja lamanja kapena kukwanja lamanzele. 33 Muzayenda muli zonse njila zamene Yehova Mulungu wanu akuuzani, kuti munkale namoyo, ndipo kuti ziyende bwino naimwe, nakuti yayende pasogolo masiku yanu mu malo yamene muzatenga.