Mutu 13

1 Ngati kuli wanyamuka mwaimwe muneneli kapena wolota maloto, na kukupasani imwe choonesela kapena chodabwisa, 2 ndipo ngati choonesela kapena chodabwisa chabwela, monga iye anakambila kuli imwe na kuti, 'Tiyeni tiyende pambuyo pa milungu inangu, yamene simunaizibe, ndipo tiyeni tiilambile,' 3 musanvelele ku mau ya uyo muneneli, kapena uyo olota maloto; chifukwa Yehova Mulungu wanu akuyesani imwe kuziba ngati imwe mumukonda Yehova Mulungu wanu na mutima wanu wonse na umoyo wanu wonse. 4 Muzayenda pambuyo pa Yehova Mulungu wanu, kumulemeke iye, kusunga malamulo yake, na kunvela mau yake, ndipo muzamulambila na kugwililila kuli eve. 5 Uyo muneneli kapena uyo olota malotoazikidwa ku infa, chifukwa akamba kusanvelela mosusana na Yehova Mulungu wanu, wamene anakuchosani kuchoka mu ziko ya Igputo, ndipo anakuombolani imwe kuchoka mu nyumba ya ukapolo. Uyo muneneli afuna kukuchosani imwe kuchoka munjila yamene Yehova Mulungu wanu analamulila imwe kuyendamo. koma ikani kutali zoipa kuchoka pakati panu. 6 Nanga ngati mubale wako, mwana mwamuna wa amai bako, kapena mwana wako mwamuna, kapena mwana wako mukazi, kapena mukazi wako wapachifuba, kapena munzako wamene ali kuli iwe monga umoyo wako, mobisika akakunyengelela iwe nakuti, 'Tiye ndipo tilambile milungu inangu yamene siunazibe, kapena iwe kapena makolo bako- 7 iliyonse milungu ya banthu yamene yokuzungulilani, pafupi naimwe, kapena patali naimwe, kuchoka kumozi kosilizila ziko lapansi na kufika kwina kosilizila ziko yapansi.' 8 Simufunika kupasa kuli eve kapena kunvela kuli eve, ndipo simufunika kulola menso yanu kumunvelela chifundo, ndiponso simufunika kumulekelela kapena kumuchingiliza eve. 9 Koma, imwe mufunika kumupaya; manja yanu yafunika kunkala yoyamba kufaka eve kuifya, na bambuyo pake manja ya bonse banthu. 10 Muzamulasa eve mpaka infa na myala, chifukwa ayesa kukuchosani imwe kuchoka kwa Yehova Mulungu wanu, wamene anakuchosani imwe ku ziko ya Igputo, kuchoka kunyumba ya ukapolo. 11 Bonse ba Israeli bazanvela na kuyopa, ndipo sibazapitiliza kuchita monga ichi chintu chosayela mukati mwanu. 12 Ngati mwanvela aliyense akuti pali umozi mwa minzi yanu, kuti Yehova Mulungu wanu akupasani kuti munkalemo: 13 Benangu woipa banthu bayenda kuchoka mukati mwanu na kuchosa mibadwe ya minzi yawo na kuti, 'Lekani tiyende na kulambila milingu inangu yamene simuziba.' 14 Ndipo muzayesa chizibiso, kupanga kufuna, na kufunisisa kwabwino. Koma mukapeza kuti nizoona na kuziba kuti icho chonyansa chinthu chachitika mukati mwanu, ndipo muzatenga chisanzo. 15 Imwe zoona mufunika kuononga wonkalamo ba muja mumunzi na lupanga, kuonongelatu na banthu bonse bamene balimo, na vonse vibeto, na lupanga. 16 Muzabwelesa pamozi vonse voonongeka kuchoka uko kufika mukati mwa njila na kushoka mizinda, na pamozi navoonongeka vake- chifukwa cha Yehova Mulungu wanu. muzinda uzankala choononga muyayaya; siifunika kumangidwa futi. 17 Palibe chimodzi mwazinthu zoyikidwa kuti ziwonongedwe siziyenera kukhala m'manja mwanu. Izi zikhale choncho, kuti Yehova atembenuke kuchoka mkwiyo wake woyaka mkwiyo, akuchitireni chifundo ndi kukuchitirani chifundo ndi kukuchulukitsani monga analumbirira makolo anu. 18 Azichita izi chifukwa chakuti mumvera mawu a Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero, ndi kuchita zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.