1 Manje munthu winangu zina lake Ananiasi, namukazi wake Saphira, anagulisa katundu wabo, 2 nosungako ndalama zinangu (nakuti mukazi izoziba pali ici), noletako zinangu nozifaka pamendo yama apostoli. 3 Koma Petulo anakamba ati, "Ananiyasi, cifukwa nicani Satana wazula mumtima wako kuti uname boza kwa Mzimu woyela nakuti usungepo ndalama inangu yamalo yamene wagulisa? 4 Pamene ukalibe kuyagulisa, kansi siyenzeli pansi paulamulilo wako? Cifukwa nicani waganiza pali ici mumtima mwako? Sunaname boza kubanthu, koma kuli Mulungu." 5 Pakumvela mau aya, Ananiyasi anagwa pansi nopeme kalasti. Ndipo mantha yakulu yanafika pali onse bamene banamvela izi. 6 Banyamata banabwela pasogolo nobwela umupomba, nobwelwela kumunyamula noyenda kumushika. 7 Pamene panapita 3 hours, mkazi wake anabwela, sanazibe camene cinabwela cacitika. 8 Petulo anakamba kwa yeve, "Niuza ngati munagulisa malo pa mtengo wa so." Anabwela akamba, "Eye, pamtengo wa so." 9 Pamene apo Petulo anabwela akamba kwa yeve ati, Cifukwa nicani mwangwilizana kuti muyese Mzimu wa Ambuye? Ona, mendo yabaja bamene ashika ba muna bako yali paciseko, ndipo bazakunyamula panja naiwe." 10 Pamene apo anabwela anagwela pamendo pake, nobwelo peme ka lasti, banyamata banangena nobwela kumupeza wakufa; banamunyamula noyenda kumushika pafupi namwamuna wake. 11 Mantha yakulu yanabwela pa mupingo bonse, napali bonse bamene banamvela izi zinthu. 12 Vizindikilo na vodabwisa vambili vezocitika pa banthu kupitila mumanja yama apostoli. Benzeli bonse pamozi mu kholido ya Solomoni. 13 Koma kwenzelibe aliyense enzeli olimbikila kuti abajoine, koma banabapasa ulemu banthu. 14 Nangu cenzeli so, bokhulupila benzo bwelelapo kwa Ambuye, bamuna na bakazi bambili, 15 paka benzo nyamula nabodwala mumiseu nobagoneka pama bedi napama cila, kuti pamene Petulo anabwela, cimvwili-mvwila cake cingagwele pali bena ba iwo. 16 Kunabwela futi banthu bambili kucoka kuma tauni yozungulila Yelusalemu, kubwelesa odwala nabonse bovutikila na vibanda voipa, ndipo bonse banacilisiwa. 17 Koma mukulu wa asembe ananyamuka, nabonse benzeli na yeve (yamene nigulu yama saduki); benzeli anakhala na jelasi 18 ndipo banagwila ma apostoli nobamanga nobafaka mundende za banthu bonse. 19 Koma panthawi ya usiku mu ngelo wa Ambuye anasegula viseko vamundende nobacosa panja, nobauza ati, 20 "Yendani mukaimilile mu tempele nokamba kubanthu mau yonse ya umoyo uyu." 21 Pamene banamvela izi, banangena mu tempele camumawa ndipo anaphunzisa. Koma mukulu wa asembe anabwela, nabanja enzeli nayeve, noitanisa musonkhano pa mozi, bonse bakulu ba banthu baku Israyeli, nobatuma ku ndende kuti babwelese ma apostoli. 22 Koma ma ofisazi bamene anatumiwa sanabapezemo mu ndende, ndipo banabwelela nopeleka repoti, 23 "Napeza ndende niyokhomewa bwino ndipo magadi oyimilila pa ciseko, koma pamene tinasegula, tinapeza mulibe munthu mukati." 24 Manje pamene kaputeni wamu tempele na mukulu wa asembe banamvela mau aya, banadabwa maningi naveve pazamene zinacitika. 25 Ndipo winangu anabwela abauza, "Bamuna bamene munafaka mundende ayimilila mu tempele ndipo aphunzisa anthu." 26 Ndipo kaputeni anayenda nama ofisazi, nowabwelesa, kulibe viongo, cifukwa cakuti banayopa kuti anthu angabateme miala. 27 Pamene banababwelesa, banaba nkhazika pali pa khanso. Mkulu wa asembe anabafunsa beve, 28 kukamba kuti, "Tinakulamulilani maningi kuti musaphunzise muzina iyi, ndipo manje, mwazuzya Yelusalemu naziphunziso zanu, ndipo mufuna kuleta mwazi wa uyu munthu pa ise." 29 Koma Petulo nama apostozi wanayankha, "Tifunika kumvelela Mulungu kupambana banthu. 30 Mulungu waba tate bathu anamuusha Yesu, wamene munapaya pakumupacika pamtengo. 31 Mulungu anamukweza yeve kukwanja kwake kwa manja kunkhala mwana wa mfumu na mupulumusi, kupasa kutembenuka kuli Israyeli, naku khululukiwa kwa macimo. 32 Ndise mboni pali ivi vinthu, cimozi-mozi na Muzimu Oyela, wamene Mulungu anapasa kuli baja bamene amumvelela iye." 33 Pamene ba khaso banamvela izi, banakalipa ndipo banafuna kupaya ma apostozi. 34 Koma mfarisi zina yake Gamaliyeli, mphunzisi wama lamulo, wamene enze olemekezeka na banthu wonse, ananyamuka nolamulila kuti ma apostozi bapelekewe panja pakanthawi kang'ono. 35 Ndipo anakamba kwa beve, " Ba muna ba Israyeli, mvesesani pazamene mukamba kucita kuli aba banthu. 36 Panthawi yapita iyi, Teudasi ananyamuka nokamba kuti anali munthu wapandela, ndipo amuna ambiri, okwanila ngati 400 anamujoina iye. Anapaiwa, ndipo bonse benzomumvelela banamwazikana, nosililatu. 37 Pamene anacoka uyu munthu, Yudasi waku Galileya ananyamuka pamasiku ya cibelengelo ndipo anadonsa banthu kukonkha yeve. Nayeve anaonongeka, nabonse benzo mumvelela banamwazikana. 38 Manje nikamba kwa imwe, nkhalani kutali na aba banthu ndipo basiyeni, ngati iyi plani kapena nchito niya banthu, izagonjesewa. 39 Koma ngati niya Mulungu, simuzakwanisa kubagonjesa; mungapeze kuti mwina mumenyana na Mulungu." Pamene apo anamvelela. 40 Pamene apo anabaitana ma apostozi kuti bangene nobamenya nobalamulila kuti basakambe futi muzina la Yesu, nobwelo batailila. 41 Banacoka ku khanso wosangalala kuti banabelengelewa boyenela kuvesewa nsoni cifukwa ca Zina. 42 Pambuyo pake siku na siku, mu tempele ndipo kucoka kunyumba noyenda nyumba kwinangu, banapitiliza kuphunzisa nolalikila Yesu kunkhala Kristu.